Walawi 18 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Walawi 18:1-30

Uhusiano Wa Kukutana Kimwili Kinyume Cha Sheria

1Bwana akamwambia Mose, 218:2 Mwa 17:7; Eze 20:5; Kut 6:7“Sema na Waisraeli uwaambie: ‘Mimi ndimi Bwana Mungu wenu. 318:3 Kut 23:24; Kum 18:9; 2Fal 16:3; 17:8; 1Nya 5:25; Eze 23:8Msifanye kama wafanyavyo huko Misri, mahali mlipokuwa mnaishi, wala msifanye kama wanavyofanya katika nchi ya Kanaani, mahali ninapowapeleka. Msifuate matendo yao. 418:4 Mwa 26:5; Kum 4:1; 1Fal 11:11; Yer 44:10, 23; Eze 11:12Ni lazima mzitii sheria zangu, na mwe waangalifu kuzifuata amri zangu. Mimi ndimi Bwana Mungu wenu. 518:5 Mwa 26:5; Neh 9:20; Isa 55:2; Eze 18:9; 20:11; Amo 5:4-6; Mt 19:17; Rum 10:5; Gal 3:12Zishikeni amri zangu na sheria zangu, kwa maana mtu anayezitii ataishi kwa hizo. Mimi ndimi Bwana.

6“ ‘Hakuna mtu awaye yote atakayemsogelea ndugu wa karibu ili kukutana naye kimwili. Mimi ndimi Bwana.

718:7 Law 20:11; Kum 27:20; Eze 22:10-11“ ‘Usimvunjie heshima baba yako kwa kukutana kimwili na mama yako. Yeye ni mama yako; usiwe na mahusiano kama hayo naye.

818:8 1Kor 5:11; Mwa 35:22; Law 20:11; Kum 22:30; 27:20“ ‘Usikutane kimwili na mke wa baba yako; hiyo itamvunjia heshima baba yako.

918:9 Law 20:17; Kum 27:22; 2Sam 13:13; Eze 22:11“ ‘Usikutane kimwili na dada yako, wala binti wa baba yako, au binti wa mama yako, awe amezaliwa katika nyumba hiyo au mahali pengine.

10“ ‘Usikutane kimwili na binti wa mwanao ama binti wa binti yako; utajivunjia heshima.

11“ ‘Usikutane kimwili na binti wa mke wa baba yako, aliyezaliwa na baba yako; huyo ni dada yako.

1218:12 Law 20:19“ ‘Usikutane kimwili na dada wa baba yako; ni ndugu wa karibu wa baba yako.

1318:13 Law 20:20“ ‘Usikutane kimwili na dada wa mama yako, kwa sababu ni ndugu wa mama yako wa karibu.

14“ ‘Usimvunjie heshima ndugu wa baba yako, kwa kukutana kimwili na mke wake; yeye ni shangazi yako.

1518:15 Mwa 11:31; 38:16; Eze 22:11; Law 20:12“ ‘Usikutane kimwili na mkwe wako, yeye ni mke wa mwanao; usiwe na mahusiano kama hayo naye.

1618:16 Law 20:21; Mt 14:4; Mk 6:18“ ‘Usikutane kimwili na mke wa kaka yako; utamvunjia heshima kaka yako.

1718:17 Law 20:14; Kum 27:23“ ‘Usikutane kimwili na mwanamke kisha na binti yake. Usikutane kimwili na binti wa mwanawe au binti wa binti yake; hao ni ndugu zake wa karibu. Huo ni uovu.

1818:18 Mwa 30:1; Mal 2:15“ ‘Usimchukue dada wa mke wako kuwa mke mwenza, na kukutana naye kimwili wakati bado mke wako anaishi.

1918:19 Law 15:24-30; 20:18; Eze 18:6“ ‘Usimsogelee mwanamke ili kukutana naye kimwili wakati wa unajisi wa siku zake za mwezi.

2018:20 Kut 20:14; Mt 5:27-28; 1Kor 6:9; Ebr 13:4; Mit 6:29“ ‘Usikutane kimwili na mke wa jirani yako na kujitia naye unajisi.

2118:21 Kum 9:4; 12:31; 18:10; 2Fal 16:3; 17:17; 21:6; 23:10; 2Nya 28:1-4; 33:6; Za 106:37-38; Isa 48:11; 57:5; Yer 7:30-31; 19:5; 32:35; Eze 16:20; 22:26; 36:20; Mik 6:7; Law 19:12; 20:2-5; 21:6; Amo 2:7; 1Fal 11:5, 7, 33; Sef 1:5; Mal 1:12; Kut 6:2“ ‘Usimtoe mtoto wako yeyote awe kafara kwa mungu Moleki, kwani hutalinajisi kamwe jina la Mungu wako. Mimi ndimi Bwana.

2218:22 Law 20:13; Kum 23:18; Rum 1:27; 1Kor 6:9; Mwa 19:5“ ‘Usikutane kimwili na mwanaume kama mtu akutanaye na mwanamke; hilo ni chukizo.

2318:23 Kut 22:19; Law 20:15; Kum 27:21“ ‘Usikutane kimwili na mnyama na kujitia unajisi kwake. Mwanamke asijipeleke kwa mnyama ili kukutana naye kimwili; huo ni upotovu.

2418:24 Law 20:23; Kum 9:4; 18:12; Mt 15:18; 1Kor 3:17“ ‘Msijitie unajisi kwa njia yoyote katika hizi, kwa sababu hivi ndivyo mataifa nitakayoyafukuza mbele yenu yalivyojitia unajisi. 2518:25 Hes 35:34; Kum 9:5; 12:31; 18:12; 21:23; Law 20:23; Ay 20:15; Yer 51:34Hata nchi ilitiwa unajisi, hivyo nikaiadhibu kwa dhambi zake, nayo nchi ikawatapika wakazi wake. 2618:26 Mwa 26:5; 18:28; Law 20:22; Ezr 9:11; Mao 1:17Lakini ni lazima uzitunze amri zangu na sheria zangu. Mzawa na wageni waishio miongoni mwenu kamwe wasifanye mambo yoyote ya machukizo haya, 27kwa kuwa mambo haya yote yalifanywa na watu walioishi katika nchi hii kabla yenu, na nchi ikawa najisi. 28Kama mkiinajisi nchi, itawatapika kama ilivyowatapika mataifa yaliyowatangulia.

29“ ‘Kila mtu atakayefanya mojawapo ya machukizo haya, watu hao ni lazima wakatiliwe mbali na watu wao. 3018:30 Law 8:35; Kum 11:1; 19:2; Hes 14:5; Za 68:26; Kut 20:2; 15:11; 1Pet 1:16; Law 11:44; 20:26Shikeni maagizo yangu, wala msifuate desturi za machukizo yoyote yaliyofanywa kabla hamjafika katika nchi hii, na kujitia unajisi kwa hayo. Mimi ndimi Bwana Mungu wako.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 18:1-30

Kugonana Koletsedwa

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 3Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo. 4Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 5Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.

6“ ‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.

7“ ‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.

8“ ‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.

9“ ‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.

10“ ‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.

11“ ‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.

12“ ‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.

13“ ‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.

14“ ‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.

15“ ‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.

16“ ‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.

17“ ‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.

18“ ‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.

19“ ‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.

20“ ‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.

21“ ‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.

22“ ‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.

23“ ‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.

24“ ‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera. 25Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo. 26Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi, 27pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa. 28Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.

29“ ‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake. 30Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”