Ufunuo 18 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ufunuo 18:1-24

Kuanguka Kwa Babeli

118:1 Ufu 17:1; 10:1; Eze 43:2Baada ya haya nikaona malaika mwingine akishuka kutoka mbinguni, akiwa na mamlaka makuu na dunia ikamulikiwa na mngʼao wake. 218:2 Ufu 18:4; Yer 51:37Naye akalia kwa nguvu kwa sauti kubwa, akisema:

“Umeanguka! Umeanguka Babeli Mkuu!

Umekuwa makao ya mashetani

na makazi ya kila pepo mchafu,

makazi ya kila ndege na kila mnyama achukizaye.

318:3 Ufu 14:8; 17:2; Eze 27:9-25Kwa maana mataifa yote yamekunywa

mvinyo wa ghadhabu ya uasherati wake.

Nao wafalme wa dunia wamefanya uzinzi nao,

nao wafanyabiashara wa dunia

wametajirika kutokana na wingi wa utajiri wake.”

418:4 Isa 48:20; 2Kor 6:17Kisha nikasikia sauti nyingine kutoka mbinguni ikisema:

“Tokeni katikati yake, enyi watu wangu,

ili msije mkashiriki dhambi zake,

ili msije mkapatwa na pigo lake lolote;

518:5 2Nya 28:9; Ezr 9:6; Ufu 16:19kwa kuwa dhambi zake zimelundikana hadi mbinguni,

naye Mungu ameukumbuka uhalifu wake.

618:6 Za 137:8; Yer 50:15-29; Ufu 14:10; 17:10Mtendee kama yeye alivyotenda;

umlipe mara mbili kwa ajili ya yale aliyotenda.

Katika kikombe chake mchanganyie

mara mbili ya kile alichochanganya.

718:7 Eze 28:2-8; Za 10:6; Sef 2:15Mpatie mateso na huzuni nyingi sawa na

utukufu na anasa alizojipatia.

Kwa kuwa moyoni mwake hujivuna, akisema,

‘Mimi ninatawala kama malkia;

mimi si mjane, wala sitaona huzuni kamwe.’

818:8 Isa 9:14; 47:9Kwa hiyo mapigo yatampata kwa siku moja:

mauti, maombolezo na njaa.

Naye atateketezwa kwa moto,

kwa maana Bwana Mungu amhukumuye ana nguvu.

918:9 Ufu 14:8, 11; 19:13; Yer 51:8; Eze 26:17-18“Wafalme wa dunia waliozini naye na kushiriki anasa zake watakapoona moshi wa kuungua kwake, watamlilia na kumwombolezea. 1018:10 Ufu 18:15, 17; 18:16-19; 17:12Kwa hofu kubwa ya mateso yake, watasimama mbali na kulia na wakisema:

“ ‘Ole! Ole, ee mji mkubwa,

ee Babeli mji wenye nguvu!

Hukumu yako imekuja katika saa moja!’

1118:11 Eze 27:27; 27:31; 18:15, 19“Wafanyabiashara wa dunia watalia na kumwomboleza kwa sababu hakuna anunuaye bidhaa zao tena: 1218:12 Eze 27:12-22Bidhaa za dhahabu, za fedha, za vito vya thamani na vya lulu, kitani safi, nguo za rangi ya zambarau, hariri, nguo nyekundu, aina zote za miti ya udi, na vifaa vyote vya pembe za ndovu, vifaa vyote vya miti yenye thamani kuliko yote, shaba, chuma na marmar, 1318:13 Eze 27:13; 1Tim 1:10bidhaa za mdalasini, vikolezi, za uvumba, manemane, na uvumba wenye harufu nzuri, za divai, na mafuta ya zeituni, za unga mzuri na ngano; ngʼombe na kondoo; farasi na magari; na miili na roho za wanadamu.

14“Watasema, ‘Yale matunda ambayo roho yako iliyatamani yamekoma. Utajiri wako wote na fahari yako vimetoweka, wala haviwezi kupatikana tena kamwe!’ 1518:15 Ufu 18:3, 10, 17; Eze 27:31Wale wafanyabiashara waliotajirika kwa bidhaa hizo kutoka kwake watasimama mbali naye kwa hofu kubwa ya mateso yanayompata. Watalia na kuomboleza wakipiga kelele wakisema:

1618:16 Ufu 17:4; 18:10, 19“ ‘Ole! Ole, ee mji mkubwa,

uliyekuwa umevikwa mavazi ya kitani safi,

ya rangi ya zambarau na nyekundu,

ukimetameta kwa dhahabu,

vito vya thamani na lulu!

1718:17 Ufu 17:16; Eze 27:28-30Katika muda wa saa moja utajiri wote mkubwa

kama huu umeangamia!’

“Kila nahodha, na wote wasafirio kwa meli, na wote wapatao kipato chao kutokana na bahari, watasimama mbali. 1818:18 Eze 27:32; Ufu 13:4Watakapouona moshi wa kuungua kwake watalia wakisema, ‘Je, kulipata kuwako mji mkubwa kama huu?’ 1918:19 Eze 27:30; Ufu 17:16Nao watajirushia mavumbi vichwani mwao, huku wakilia na kuomboleza, wakisema:

“ ‘Ole! Ole, ee mji mkubwa,

mji ambao wote wenye meli baharini

walitajirika kupitia kwa mali zake!

Katika saa moja tu ameangamizwa!

2018:20 Yer 51:48; Ufu 12:12; 19:2Furahia kwa ajili yake, ee mbingu!

Furahini watakatifu, mitume na manabii!

Mungu amemhukumu

kwa vile alivyowatendea ninyi.’ ”

2118:21 Ufu 5:2; Yer 51:63Kisha malaika mmoja mwenye nguvu akainua jiwe kubwa kama la kusagia akalitupa baharini akisema:

“Hivyo ndivyo mji mkubwa Babeli

utakavyotupwa chini kwa nguvu

wala hautaonekana tena.

2218:22 Isa 24:8; Eze 26:13; Yer 25:10Nyimbo za wapiga vinubi na waimbaji,

wapiga filimbi na wapiga tarumbeta

kamwe hazitasikika tena ndani yako.

Ndani yako kamwe hataonekana tena fundi

mwenye ujuzi wa aina yoyote.

Wala sauti ya jiwe la kusagia

kamwe haitasikika tena.

2318:23 Yer 16:9; 25:10; Isa 23:8; Nah 3:4Mwanga wa taa

hautaangaza ndani yako tena.

Sauti ya bwana arusi na bibi arusi

kamwe haitasikika ndani yako tena.

Wafanyabiashara wako walikuwa watu maarufu wa dunia.

Mataifa yote yalipotoshwa kwa uchawi wako.

2418:24 Ufu 16:6; 17:6; Yer 51:49Ndani yake ilionekana damu ya manabii na ya watakatifu

na wote waliouawa duniani.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 18:1-24

Kugwa kwa Babuloni

1Zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika kuchokera kumwamba. Iye anali ndi ulamuliro waukulu, ndipo dziko lapansi linawala ndi ulemerero. 2Mngeloyo anafuwula ndi mawu amphamvu kuti:

“ ‘Wagwa! Wagwa Babuloni Wamkulu!’

Wasandulika mokhalamo ziwanda

ndi kofikako mizimu yonse yoyipa

ndi mbalame zonse zonyansa

ndi zodetsedwa.

3Pakuti mayiko onse amwa

vinyo ozunguza mutu wazigololo zake.

Mafumu a dziko lapansi achita naye chigololo,

ndipo amalonda a dziko lapansi analemera kuchokera pa zolakalaka zake zosefukira.”

Awachenjeza kuti Athawe Chiweruzo cha Babuloni

4Ndiponso ndinamva mawu ena kuchokera kumwamba akuti:

“ ‘Anthu anga tulukani, mwa iye,’

mungachimwe naye

kuti musadzalandire nawo gawo lililonse la miliri yake;

5pakuti machimo ake awunjikana mpaka kumwamba,

ndipo Mulungu wakumbukira milandu yake.

6Bwezerani Iye monga momwe iye anakuchitirani.

Mubwezereni mowirikiza pa zimene anachita.

Mumusakanizire magawo awiri kuchokera mʼchikho chake.

7Mumuzunze, kumumvetsa chisoni kwambiri

monga mwaulemerero ndi zolakalaka

zimene anadzaza mu mtima mwake. Iye anadzikuza nʼkumati,

‘Ndinakhala monga mfumu yayikazi,

ine sindine wamasiye

ndipo sindidzalira maliro.’

8Chifukwa chake miliri yake idzamugonjetsa tsiku limodzi;

imfa, kulira maliro ndi njala.

Iye adzanyeka ndi moto

pakuti wamphamvu ndi Mulungu Ambuye amene wamuweruza.

Tsoka la Babuloni

9“Mafumu a dziko lapansi, amene anachita naye chigololo nachita naye pamodzi zosangalatsa moyo uno, akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzalira nakhuza maliro ake. 10Iwo adzayima kutali nalira chifukwa choopsedwa ndi mazunzo ake.

“ ‘Tsoka! Tsoka mzinda waukulu

iwe, Babuloni mzinda wamphamvu!

Mu ora limodzi chiwonongeko chako chafika!’

11“Amalonda a dziko lapansi adzalira nakhuza maliro ake chifukwa palibenso amene akugula katundu wawo, 12katundu wagolide, siliva, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale; nsalu zoyera kwambiri zapamwamba ndi zofiira; nsalu zasilika ndi zapepo; mitengo iliyonse yonunkhira ndi zinthu zilizonse zopangidwa ndi mnyanga, kapena matabwa ogulidwa ndi ndalama zambiri kapena mkuwa kapena chitsulo ndi mwala wonyezimira; 13zokometsera zakudya, mure, lubani ndi zofukiza zina, vinyo ndi mafuta a olivi, ufa wosalala ndi tirigu; ngʼombe ndi nkhosa; akavalo ndi ngolo; ndi anthu adzagulitsidwa ukapolo.

14“Iwo adzanena kuti, ‘Chipatso chimene unachilakalaka chakuchokera. Chuma chako chonse ndi ulemerero zatha, sizidzapezekanso.’ 15Amalonda amene anagulitsa zinthu izi napeza chuma kuchokera kwa iye adzayima patali potero ataopsedwa ndi mazunzo ake. Adzalira ndi kukhuza maliro 16ndipo adzalira mokuwa kuti,

“ ‘Tsoka! Tsoka! Mzinda waukulu,

iwe wovala nsalu zoyera kwambiri, zapepo ndi zofiira,

ndi wonyezimira ndi golide, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale!

17Chuma chambiri choterechi chafika powonongeka mu ora limodzi!’

“Oyendetsa sitima ndi onse oyenda pa sitima ya pamadzi, ogwira ntchito mʼsitima ndi onse amene amadalira nyanja pamoyo wa tsiku ndi tsiku adzayima patali potero. 18Akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzakuwa kuti, ‘Kodi panalinso mzinda wina ngati mzinda waukuluwu?’ 19Adzathira fumbi pamitu pawo ndipo adzalira nakhuza maliro kuti,

“Tsoka! Tsoka mzinda waukulu iwe,

kumene onse anali ndi sitima pa nyanja

analemera kudzera mʼchuma chake!

Mu ora limodzi wawonongedwa.

20“Kondwerani chifukwa cha iye inu kumwamba!

Kondwerani oyera mtima

ndi atumwi ndi aneneri!

Mulungu wamuweruza iye

monga momwe anakuchitirani inu.”

Chiwonongeko Chotsiriza cha Babuloni

21Kenaka mngelo wamphamvu ananyamula mwala waukulu ngati mphero yayikulu nawuponya mʼnyanja nanena kuti,

“Mwa mphamvu chonchi

mzinda waukulu wa Babuloni udzaponyedwa pansi,

sudzapezekanso.

22Mwa iwe simudzamvekanso liwu la woyimba zeze, ndi akatswiri a zoyimbayimba,

oyimba zitoliro, ndi lipenga.

Mwa iwe simudzapezekanso

mʼmisiri wina aliyense.

Mwa iwe simudzapezekanso

phokoso la mphero.

23Kuwala kwa nyale

sikudzawunikanso mwa inu.

Mawu a mkwati ndi mkwatibwi

sadzamvekanso mwa iwe.

Amalonda anu anali akuluakulu a dziko lapansi.

Mitundu yonse inasokonezedwa ndi zamatsenga zako.

24Mwa iye munapezeka magazi a aneneri ndi a oyera mtima,

ndi onse amene anaphedwa pa dziko lapansi.”