12:1 2Nya 20:4; Yoe 1:14; 2:16; Yer 3:3; 6:15Kusanyikeni pamoja, kusanyikeni pamoja,
enyi taifa lisilo na aibu,
22:2 Isa 17:13; Hos 13:3; 2Fal 23:26; Yer 4:4; 10:25; Eze 7:19; Mao 4:11kabla ya wakati ulioamriwa haujafika
na siku ile inayopeperusha kama makapi,
kabla hasira kali ya Bwana haijaja juu yenu,
kabla siku ya ghadhabu ya Bwana
haijaja juu yenu.
32:3 Amo 5:6; Yoe 2:4; Isa 1:17; Za 45:4; 57:1; 76:9Mtafuteni Bwana, enyi nyote wanyenyekevu wa nchi,
ninyi ambao hufanya lile analoamuru.
Tafuteni haki, tafuteni unyenyekevu;
labda mtahifadhiwa
siku ya hasira ya Bwana.
Dhidi Ya Ufilisti
42:4 Mwa 10:19; Amo 1:6-8; Zek 9:5-7; Yer 6:4; 47:5Gaza utaachwa
na Ashkeloni utaachwa magofu.
Wakati wa adhuhuri Ashdodi utaachwa mtupu
na Ekroni utangʼolewa.
52:5 1Sam 30:14; Law 26:31; Eze 25:16; Yos 13:3; Isa 14:30Ole wenu ninyi ambao mnaishi kando ya bahari,
enyi Wakerethi;
neno la Bwana liko dhidi yenu,
ee Kanaani, nchi ya Wafilisti.
“Mimi nitawaangamiza,
na hakuna atakayebaki.”
62:6 Isa 5:17; 17:2Nchi kando ya bahari, mahali ambapo wanaishi Wakerethi,
patakuwa mahali pa wachungaji
na mazizi ya kondoo.
72:7 Isa 11:11; Hag 1:12; Mik 5:7; 4:10; Kut 4:31; Lk 1:68; Mwa 45:7; Kum 30:3; Za 126:4; Yer 23:3; 32:44; Hos 6:11; Eze 39:25; Yoe 3:1; Amo 1:6-8Itakuwa mali ya mabaki ya nyumba ya Yuda,
hapo watapata malisho.
Wakati wa jioni watajilaza chini
katika nyumba za Ashkeloni.
Bwana Mungu wao atawatunza,
naye atawarudishia wafungwa wao.
Dhidi Ya Moabu Na Amoni
82:8 Mwa 19:37; Yer 48:27; 49:1; Eze 25:3, 8; 21:28; Mao 3:61; Isa 16:6“Nimeyasikia matukano ya Moabu
nazo dhihaka za Waamoni,
ambao waliwatukana watu wangu
na kutoa vitisho dhidi ya nchi yao.
92:9 Kum 23:6; 29:23; Isa 11:14; Yer 48:1-47; 49:1-6; Eze 25:1-11; 2Fal 19:31; Amo 1:13; 2:1-3Hakika, kama niishivyo,”
asema Bwana Mwenye Nguvu Zote,
Mungu wa Israeli,
“hakika Moabu itakuwa kama Sodoma,
Waamoni kama Gomora:
mahali pa magugu na mashimo ya chumvi,
nchi ya ukiwa milele.
Mabaki ya watu wangu watawateka nyara;
mabaki ya taifa langu watarithi nchi yao.”
102:10 Ay 40:12; Isa 16:6; Yer 48:27; Za 9:6Hiki ndicho watarudishiwa kwa ajili ya kiburi chao,
kwa kutukana na kudhihaki
watu wa Bwana Mwenye Nguvu Zote.
112:11 Mwa 49:10; 10:5; Za 2:8; 22:27; Isa 2:2, 3; Mal 1:11; Yn 4:21; 1Tim 2:8; Yoe 2:11; 1Nya 19:1; Eze 25:6-7; Isa 12:4; Za 86:9; Sef 3:9Bwana atakuwa wa kuhofisha kwao
atakapoangamiza miungu yote ya nchi.
Mataifa katika kila pwani yatamwabudu,
kila moja katika nchi yake.
Dhidi Ya Kushi
122:12 Mwa 10:6; Isa 18:1; 20:4; Yer 46:10“Ninyi pia, ee Wakushi,
mtauawa kwa upanga wangu.”
Dhidi Ya Ashuru
132:13 Mwa 10:5-11; Zek 10:11; Mik 5:6Mungu atanyoosha mkono wake dhidi ya kaskazini
na kuangamiza Waashuru,
akiiacha Ninawi ukiwa
na pakame kama jangwa.
142:14 Isa 5:17; 13:21; 14:23; Ufu 18:2; Za 102:6Makundi ya kondoo na ngʼombe yatajilaza pale,
viumbe vya kila aina.
Bundi wa jangwani na bundi waliao kwa sauti nyembamba
wataishi juu ya nguzo zake.
Mwangwi wa kuita kwao utapita madirishani,
kifusi kitakuwa milangoni,
boriti za mierezi zitaachwa wazi.
152:15 Isa 32:9; 47:8; Eze 27:36; 28:2; Ufu 18:7; Yer 49:33; Nah 3:19Huu ndio mji uliotukuka na kuishi kwa furaha
wakijisikia salama.
Ulisema moyoni mwako,
“Mimi ndimi, na wala hapana mwingine ila mimi.”
Jinsi gani umekuwa gofu,
mahali pa kulala wanyama pori!
Wote wanaopita kando yake wanauzomea
na kutikisa mkono kwa dharau.
1Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
inu mtundu wochititsa manyazi,
2isanafike nthawi yachiweruzo,
nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
3Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
mwina mudzatetezedwa
pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Za Afilisti
4Gaza adzasiyidwa
ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
ndipo Ekroni adzazulidwa.
5Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
ndipo palibe amene adzatsale.”
6Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
7Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
adzabwezeretsa mtendere wawo.
Za Mowabu ndi Amoni
8“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
9Choncho, pali Ine Wamoyo,”
akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
10Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
uliwonse ku dziko la kwawo.
Za Kusi
12“Inunso anthu a ku Kusi,
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Za Asiriya
13Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
ndi owuma ngati chipululu.
14Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15Umenewu ndiye mzinda wosasamala
umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
ndi kupukusa mitu yawo.