Nahumu 3 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Nahumu 3:1-19

Ole Wa Ninawi

13:1 Eze 22:2; Mik 3:10; Za 12:2Ole wa mji umwagao damu,

uliojaa uongo,

umejaa nyara,

usiokosa kuwa na vitu vya kuteka nyara.

23:2 Isa 34:3; Yer 47:3Kelele za mijeledi,

vishindo vya magurudumu,

farasi waendao mbio

na mshtuo wa magari ya vita!

3Wapanda farasi wanaenda mbio,

panga zinameremeta,

na mikuki inangʼaa!

Majeruhi wengi,

malundo ya maiti,

idadi kubwa ya miili isiyohesabika,

watu wanajikwaa juu ya mizoga:

43:4 Isa 47:9; 23:17; 2The 2:9, 10; Dan 2:2; Ufu 9:20, 21; Eze 16:25-29yote haya kwa sababu ya wingi wa tamaa za kahaba,

anayeshawishi, bibi wa mambo ya uchawi,

anayewatia utumwani mataifa kwa ukahaba wake

na pia jamaa za watu kwa ulozi wake.

53:5 Nah 2:13; Isa 47:2-3; 20:4; Yer 13:22Bwana Mwenye Nguvu Zote anasema,

“Mimi ni kinyume na ninyi.

Nitafunika uso wako kwa gauni lako.

Nitaonyesha mataifa uchi wako

na falme aibu yako.

63:6 Kut 29:14; Ay 9:31; 1Sam 2:30; Yer 51:37; Isa 14:16Nitakutupia uchafu,

nitakufanyia dharau

na kukufanya kioja.

73:7 Isa 13:14; 31:9; Nah 1:1; Ay 3:14; Yer 51:37Wote wanaokuona watakukimbia na kusema,

‘Ninawi ipo katika kuangamia:

ni nani atakayeomboleza kwa ajili yake?’

Nitampata wapi yeyote wa kukufariji?”

83:8 Amo 6:2; Yer 46:25; Isa 19:6-9Je, wewe ni bora kuliko No-Amoni,

uliopo katika Mto Naili,

uliozungukwa na maji?

Mto ulikuwa kinga yake,

nayo maji yalikuwa ukuta wake.

93:9 Mwa 10:6; 2Nya 12:3; Eze 27:10; 30:5Kushi3:9 Kushi ni Ethiopia. na Misri walikuwa nguvu zake zisizo na mpaka;

Putu na Libia walikuwa miongoni mwa wale walioungana naye.

103:10 Isa 20:4; 2Fal 8:12; Isa 13:16; Hos 13:16; Ay 6:26-27; Eze 24:6; Yer 40:1; Yoe 3:3; Oba 1:11Hata hivyo alichukuliwa mateka

na kwenda uhamishoni.

Watoto wake wachanga walivunjwa vunjwa vipande

kwenye mwanzo wa kila barabara.

Kura zilipigwa kwa watu wake wenye heshima,

na watu wake wote wakuu walifungwa kwa minyororo.

113:11 Isa 49:26; 2:10Wewe pia utalewa;

utakwenda mafichoni

na kutafuta kimbilio kutoka kwa adui.

123:12 Wim 2:13; Ufu 6:13; Isa 28:4Ngome zako zote ni kama mitini

yenye matunda yake ya kwanza yaliyoiva;

wakati inapotikiswa,

tini huanguka kwenye kinywa chake alaye.

133:13 Isa 19:16; 45:2; Yer 50:37; Nah 2:6Tazama vikosi vyako:

wote ni wanawake!

Malango ya nchi yako

yamekuwa wazi kwa adui zako;

moto umeteketeza mapingo yake.

143:14 2Nya 32:4; Nah 2:1Teka maji kwa ajili ya kuzingirwa kwako,

imarisha ulinzi wako,

Ufanyie udongo wa mfinyanzi kazi,

yakanyage matope,

karabati tanuru la kuchomea matofali!

153:15 Isa 27:1; 2Sam 2:26; Yer 51:14; Yoe 1:4Huko moto utakuteketeza,

huko upanga utakuangusha chini

na kama vile panzi, watakumaliza.

Ongezeka kama panzi,

ongezeka kama nzige!

163:16 Kut 10:13Umeongeza idadi ya wafanyabiashara wako

mpaka wamekuwa wengi kuliko nyota za angani,

lakini kama nzige wanaacha nchi tupu

kisha huruka na kwenda zake.

173:17 Ufu 9:7; Yer 51:17Walinzi wako ni kama nzige,

maafisa wako ni kama makundi ya nzige

watuao kwenye kuta wakati wa siku ya baridi:

lakini wakati jua linapotokea wanaruka kwenda zao,

na hakuna ajuaye waendako.

183:18 Za 76:5-6; Yer 25:27; 50:18; Eze 31:3; Isa 56:10; 1Fal 22:17Ee mfalme wa Ashuru, wachungaji wako wanasinzia;

wakuu wako wanalala chini mavumbini kupumzika.

Watu wako wametawanyika juu ya milima

bila kuwa na mtu yeyote wa kuwakusanya.

193:19 Yer 30:13; Mik 1:9; Ay 27:23; Mao 2:15; Sef 2:15; Isa 14:8; 37:18Hakuna kitu kinachoweza kuponya jeraha lako;

jeraha lako ni la kukuua.

Kila anayesikia habari zako,

hupiga makofi kwa kuanguka kwako,

kwa kuwa ni nani ambaye hajaguswa

na ukatili wako usio na mwisho?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 3:1-19

Tsoka la Ninive

1Tsoka kwa mzinda wopha anthu,

mzinda wodzaza ndi mabodza,

mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo,

mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!

2Kulira kwa zikwapu,

mkokomo wa mikombero,

kufuwula kwa akavalo

ndiponso phokoso la magaleta!

3Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo,

kungʼanima kwa malupanga

ndi kunyezimira kwa mikondo!

Anthu ambiri ophedwa,

milumilu ya anthu akufa,

mitembo yosawerengeka,

anthu akupunthwa pa mitemboyo.

4Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere,

wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga,

amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake,

ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndikutsutsana nawe.

Ndidzakuvula chovala chako.

Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako

ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.

6Ndidzakuthira zonyansa,

ndidzakuchititsa manyazi

ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.

7Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati,

‘Ninive wasanduka bwinja,

adzamulira ndani?’

Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”

8Kodi ndiwe wopambana Tebesi,

mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo,

wozunguliridwa ndi madzi?

Mtsinjewo unali chitetezo chake,

madziwo anali linga lake.

9Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto,

Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.

10Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa

ndipo anapita ku ukapolo.

Ana ake anawaphwanyitsa pansi

mʼmisewu yonse ya mu mzindamo.

Anachita maere ogawana anthu ake otchuka,

ndipo anthu ake onse amphamvu

anamangidwa ndi maunyolo.

11Iwenso Ninive udzaledzera;

udzabisala

ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.

12Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu

yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha;

pamene agwedeza mitengoyo,

nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.

13Tayangʼana ankhondo ako,

onse ali ngati akazi!

Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako;

moto wapsereza mipiringidzo yake.

14Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu,

limbitsani chitetezo chanu!

Pondani dothi,

ikani mʼchikombole,

konzani khoma la njerwa!

15Kumeneko moto udzakupserezani;

lupanga lidzakukanthani

ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala.

Chulukanani ngati ziwala,

chulukanani ngati dzombe!

16Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu

mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga,

koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko

ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.

17Akalonga ako ali ngati dzombe,

akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe

limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira,

koma pamene dzuwa latuluka limawuluka,

ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.

18Iwe mfumu ya ku Asiriya,

abusa ako agona tulo;

anthu ako olemekezeka amwalira.

Anthu ako amwazikira ku mapiri

popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.

19Palibe chimene chingachize bala lako;

chilonda chako sichingapole.

Aliyense amene amamva za iwe

amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako,

kodi alipo amene sanazilawepo

nkhanza zako zosatha?