Mithali 28 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 28:1-28

128:1 2Fal 7:7; Law 26:17; Za 53:5Mtu mwovu hukimbia ingawa hakuna yeyote anayemfukuza,

bali wenye haki ni wajasiri kama simba.

2Wakati nchi inapokuwa na uasi, inakuwa na viongozi wengi,

bali mwenye ufahamu na maarifa hudumisha utaratibu.

328:3 Mt 18:28Mtu maskini amwoneaye yeye aliye maskini zaidi

ni kama mvua ya dhoruba isiyosaza mazao.

428:4 1Fal 18:18; Mt 3:7; Efe 5:11; 1Tim 5:20Wale waiachao sheria huwasifu waovu,

bali wale waishikao sheria huwapinga.

528:5 Yn 7:17; 1Kor 2:15Watu wabaya hawaelewi haki,

bali wale wamtafutao Bwana wanaielewa kikamilifu.

628:6 Mit 19:1Afadhali maskini ambaye mwenendo wake hauna lawama

kuliko tajiri ambaye njia zake ni potovu.

728:7 Mit 23:19-21Yeye ashikaye sheria ni mwana mwenye ufahamu,

bali rafiki wa walafi humwaibisha baba yake.

828:8 Ay 27:16-17; Eze 18:8; Kut 18:21; Mit 13:22; Lk 14:12-14Yeye aongezaye utajiri wake kwa riba kubwa mno

hukusanya kwa ajili ya mwingine,

ambaye atawahurumia maskini.

928:9 Za 66:18; Zek 7:11; Isa 1:13; 2Tim 4:3Kama mtu yeyote akikataa kusikia sheria,

hata maombi yake ni chukizo.

1028:10 Za 34:9; 57:6; Mk 10:30; Mit 26:27; Rum 8:32Yeye ambaye humwongoza mwenye haki kwenye mapito mabaya,

ataanguka kwenye mtego wake mwenyewe,

bali wasio na lawama watapokea urithi mwema.

11Mtu tajiri anaweza kuwa na hekima machoni pake mwenyewe,

bali mtu maskini mwenye ufahamu atamfichua.

1228:12 2Fal 11:20; Ay 24:4; Mit 11:10Mwenye haki ashindapo, kuna furaha kubwa,

bali waovu watawalapo, watu hujificha.

1328:13 1Yn 1:8-10; 2Sam 12:13; Ay 31:33; Dan 4:27Yeye afichaye dhambi zake hatafanikiwa,

bali yeyote aziungamaye na kuziacha hupata rehema.

1428:14 Za 16:8; Mit 23:17; Rum 2:5; 11:20Amebarikiwa mtu ambaye siku zote humcha Bwana,

bali yeye afanyaye moyo wake kuwa mgumu

huangukia kwenye taabu.

15Kama simba angurumaye au dubu ashambuliaye,

ndivyo alivyo mtu mwovu atawalaye wanyonge.

16Mtawala dhalimu hana akili,

bali yeye achukiaye mapato ya udhalimu

atafurahia maisha marefu.

1728:17 Mwa 9:6; 1Sam 30:17Mtu mwenye kusumbuliwa na hatia ya kuua

atakuwa mtoro mpaka kufa;

mtu yeyote na asimsaidie.

1828:18 Es 6:13; Mit 10:9Yeye ambaye mwenendo wake hauna lawama

hulindwa salama,

bali yeye ambaye njia zake ni potovu

ataanguka ghafula.

1928:19 Mit 12:11Yeye alimaye shamba lake atakuwa na chakula tele,

bali yule afuataye mambo ya upuzi atakuwa na umaskini wa kumtosha.

2028:20 Mit 13:11; 20:21; 23:4, 22; 1Tim 6:9Mtu mwaminifu atabarikiwa sana,

bali yeye atamaniye kupata utajiri kwa haraka

hataacha kuadhibiwa.

2128:21 Eze 13:19; Za 94:21; Mit 18:5Kuonyesha upendeleo si vizuri,

hata hivyo mtu atafanya kosa kwa kipande cha mkate.

2228:22 Mit 28:20Mtu mchoyo ana tamaa ya kupata utajiri,

naye hana habari kuwa umaskini unamngojea.

2328:23 Mit 27:5, 6Yeye amkemeaye mtu mwishoni hupata kibali zaidi,

kuliko mwenye maneno ya kusifu isivyostahili.

2428:24 Mit 18:9; 19:26Yeye amwibiaye babaye au mamaye

na kusema, “Si kosa,”

yeye ni mwenzi wa yule aharibuye.

2528:25 1Tim 6:6; Mit 29:25Mtu mwenye tamaa huchochea fitina,

bali yule amtegemeaye Bwana atafanikiwa.

2628:26 Za 4:5; Mit 3:5Yeye ajitumainiaye mwenyewe ni mpumbavu,

bali yeye atembeaye katika hekima hulindwa salama.

2728:27 Kum 15:7; Mit 19:17; 22:9Yeye ampaye maskini

hatapungukiwa na kitu chochote,

bali yeye awafumbiaye maskini macho

hupata laana nyingi.

2828:28 Mit 28:12; Ay 20:19Wakati waovu watawalapo,

watu huenda mafichoni,

bali waovu wanapoangamia,

wenye haki hufanikiwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 28:1-28

1Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,

koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

2Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,

koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake

ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

4Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,

koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,

koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

6Munthu wosauka wa makhalidwe abwino

aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

7Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,

koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

8Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka

amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wokana kumvera malamulo

ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa

adzagwera mu msampha wake womwe,

koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;

koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,

koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,

koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa

ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza

koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu

adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;

wina aliyense asamuthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa

koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,

koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21Kukondera si kwabwino,

ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera

koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake

mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24Amene amabera abambo ake kapena amayi ake

namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”

ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25Munthu wadyera amayambitsa mikangano,

koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,

koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,

koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,

koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.