Mithali 13 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Mithali 13:1-25

Mema Ya Muda Mfupi Na Yale Ya Kudumu

113:1 1Sam 2:25; Mit 10:1; 12:1; 15:5Mwana mwenye hekima husikia mafundisho ya babaye,

bali mwenye dharau hasikilizi maonyo.

213:2 Mit 12:14Kutoka tunda la midomo yake mtu hufurahia mambo mema,

bali wasio waaminifu wanatamani sana jeuri.

313:3 Za 12:2; Yak 3:2; Mit 10:6; Ay 1:22Yeye alindaye midomo yake hulinda nafsi yake,

bali yeye asemaye kwa haraka ataangamia.

413:4 Mit 21:25-26Mvivu hutamani sana na hapati kitu,

bali nafsi ya mwenye bidii

hutoshelezwa kikamilifu.

513:5 Kol 3:9; Rum 12:9Mwenye haki huchukia uongo,

bali waovu huleta aibu na fedheha.

613:6 Mit 11:3-5; Yer 44:5Haki humlinda mtu mwadilifu,

bali uovu humwangusha mwenye dhambi.

713:7 2Kor 6:10Mtu mmoja hujifanya tajiri, kumbe hana chochote;

mwingine hujifanya maskini, kumbe ana utajiri mwingi.

813:8 Mit 15:16Utajiri wa mtu waweza kukomboa maisha yake,

bali mtu maskini hasikii kitisho.

913:9 Ay 18:5; Mit 4:18-19Nuru ya mwenye haki hungʼaa sana,

bali taa ya mwovu itazimwa.

1013:10 Amu 19:30; Mit 9:9Kiburi huzalisha magomvi tu,

bali hekima hupatikana kwa wale wanaozingatia ushauri.

1113:11 Mit 10:2; 9:9; 20:21Fedha isiyo ya halali hupungua,

bali yeye akusanyaye fedha kidogo kidogo huongezeka.

1213:12 Mit 10:11Kilichotarajiwa kikikawia kuja moyo huugua,

bali tumaini lililotimizwa ni mti wa uzima.

1313:13 Hes 15:31; Kut 9:20; Mit 16:20; 2Nya 36:16Yeye anayedharau mafundisho anajiletea maangamizi,

bali yeye anayeheshimu agizo hupewa tuzo.

1413:14 Mit 10:11; 14:27Mafundisho ya mwenye busara ni chemchemi ya uzima,

ili kumwepusha mtu na mitego ya mauti.

15Ufahamu mzuri hupata upendeleo,

bali njia ya asiye mwaminifu ni ngumu.

1613:16 Es 5:11; Mit 12:23Kila mwenye busara hutenda kwa maarifa,

bali mpumbavu hudhihirisha upumbavu wake.

1713:17 Mit 10:26; 25:13Mjumbe mwovu huanguka kwenye taabu,

bali mjumbe mwaminifu huleta uponyaji.

1813:18 Mit 15:31-32; Za 141:5Yeye anayedharau maonyo hupata umaskini na aibu,

bali yeye anayekubali maonyo huheshimiwa.

1913:19 Mit 10:11Tarajio lililotimizwa ni tamu kwa nafsi,

bali wapumbavu huchukia sana kuacha ubaya.

2013:20 2Nya 10:8Yeye atembeaye na mwenye hekima atapata hekima,

bali rafiki wa mpumbavu hupata madhara.

2113:21 Za 32:10; Mit 19:17; 11:12Balaa humwandama mtenda dhambi,

bali mafanikio ni thawabu kwa mwenye haki.

2213:22 Es 8:2; Mhu 2:26Mtu mwema huwaachia wana wa wanawe urithi,

bali mali ya wenye dhambi imehifadhiwa

kwa ajili ya wenye haki.

2313:23 Mit 12:11Shamba la mtu maskini laweza kuzalisha chakula kingi,

bali dhuluma hukifutilia mbali.

2413:24 Mit 29:15-17; Efe 6:4Yeye aizuiaye fimbo yake hampendi mwanawe,

bali yeye ampendaye

huwa mwangalifu kumwadibisha.

2513:25 Za 34:10; Mit 10:3Mwenye haki hula mpaka akaridhisha moyo wake,

bali tumbo la mwovu hutaabika kwa njaa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 13:1-25

1Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,

koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.

2Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,

koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.

3Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,

koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.

4Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,

koma munthu wakhama adzalemera.

5Munthu wolungama amadana ndi zabodza,

koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.

6Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,

koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.

7Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;

munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.

8Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,

koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.

9Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,

koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.

10Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,

koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.

11Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono

koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.

12Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,

koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.

13Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,

koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.

14Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;

amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.

15Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,

koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.

16Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,

koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.

17Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,

koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.

18Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,

koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.

19Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,

koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.

20Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;

koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.

21Choyipa chitsata mwini,

koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.

22Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,

koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.

23Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,

koma anthu opanda chilungamo amachilanda.

24Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,

koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.

25Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,

koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.