Kutoka 23 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Kutoka 23:1-33

Sheria Za Haki Na Rehema

123:1 Mwa 36:7; Mt 19:18; Lk 3:14; Kut 20:16; Kum 5:20; 19:16-21; Za 27:12; 35:11; Mit 19:5; Mdo 6:11“Usieneze habari za uongo. Usimsaidie mtu mwovu kwa kuwa shahidi mwenye nia ya kudhuru wengine.

223:2 Law 19:15, 33; Kum 1:17; 27:19; 1Sam 8:3; Kum 24:17; 16:19; Ay 31:34“Usifuate umati wa watu katika kutenda mabaya. Unapotoa ushahidi kwenye mashtaka, usipotoshe haki ukijumuika na umati wa watu, 323:3 Rum 12:20; Law 6:2-3; 19:11; Kum 22:1-2nawe usimpendelee mtu maskini katika mashtaka yake.

4“Kama ukikutana na maksai au punda wa adui yako anapotea, hakikisha umemrudisha kwake. 523:5 Kum 22:4Ukiona punda wa mtu anayekuchukia ameanguka na mzigo wake, usimwache hapo alipoangukia; hakikisha kuwa umemsaidia.

623:6 Kum 23:16; Mit 22:22“Usiwanyime haki watu wako walio maskini katika mashtaka yao. 723:7 Kut 20:16; Efe 4:24-25; Mt 27:4; Mwa 18:23; Kut 34:7; Kum 19:18; 25:1Ujiepushe na mashtaka ya uongo, wala usimuue mtu asiye na hatia au mtu mwaminifu, kwa maana sitamhesabia hana hatia yeye aliye na hatia.

823:8 Kut 18:21; Law 9:15; Kum 10:17; 27:25; Ay 15:34; 36:18; Za 26:10; Mit 6:35; 15:27; 17:8; Isa 1:23; 5:23; Mik 3:11; 7:3“Usipokee rushwa, kwa kuwa rushwa hupofusha wale waonao, na kupinda maneno ya wenye haki.

923:9 Kut 22:21; Law 19:33-34; Eze 22:7“Usimwonee mgeni; ninyi wenyewe mnajua jinsi mgeni anavyojisikia, kwa sababu mlikuwa wageni Misri.

Sheria Za Sabato

10“Kwa muda wa miaka sita mtapanda mashamba yenu na kuvuna mazao, 1123:11 Law 25:1-7; Neh 10:31lakini katika mwaka wa saba usiilime ardhi wala kuitumia, ili watu walio maskini miongoni mwenu waweze kupata chakula kutoka kwenye hayo mashamba, nao wanyama pori wapate chakula kwa yale mabaki watakayobakiza. Utafanya hivyo katika shamba lako la mizabibu na la mizeituni.

1223:12 Kut 20:9; Lk 13:14; Mwa 2:2-3“Kwa siku sita fanya kazi zako, lakini siku ya saba usifanye kazi, ili maksai wako na punda wako wapate kupumzika, naye mtumwa aliyezaliwa nyumbani mwako, pamoja na mgeni, wapate kustarehe.

1323:13 Kum 4:9, 23; 1Tim 4:16; Kum 12:3; Yos 23:7; Za 16:4; Zek 13:2; Kum 18:20; Hos 2:17“Uzingatie kutenda kila kitu nilichokuambia. Usiombe kwa majina ya miungu mingine, wala usiyaruhusu kusikika kinywani mwako.

Sikukuu Tatu Za Mwaka

(Kutoka 34:18-26; Kumbukumbu 16:1-17)

1423:14 Kut 12:14; 34:23-24; Kum 16:16; 1Fal 9:25; 2Nya 8:13; Eze 46:9“Mara tatu kwa mwaka utanifanyia sikukuu.

1523:15 Kut 12:17; Mt 26:17; Lk 22:1; Mdo 12:3; Kut 12:2; 22:29“Utaadhimisha Sikukuu ya Mikate Isiyotiwa Chachu; kwa siku saba utakula mikate isiyotiwa chachu kama nilivyokuagiza. Fanya jambo hili kwa wakati uliopangwa katika mwezi wa Abibu, ndio mwezi wa nne, kwa sababu katika mwezi huo ulitoka Misri.

“Mtu yeyote asije mbele yangu mikono mitupu.

1623:16 Law 23:15-21; Hes 28:26; Kum 16:9; 2Nya 8:13; Kut 22:29; 34:22; Law 23:34, 42; Kum 16:16; 31:10; Ezr 3:4; Neh 8:14; Zek 14:16; Yer 40:10; Kum 16:13“Utaadhimisha Sikukuu ya Mavuno kwa malimbuko ya mazao yako uliyopanda katika shamba lako.

“Utaadhimisha Sikukuu ya Kukusanya mavuno mwishoni mwa mwaka, unapokusanya mavuno yako toka shambani.

17“Mara tatu kwa mwaka wanaume wote watakuja mbele za Bwana Mwenyezi.

1823:18 Kut 34:25; Law 2:11; Kut 12:8“Msitoe damu ya dhabihu kwangu pamoja na kitu chochote kilicho na chachu.

“Mafuta ya mnyama wa sadaka ya sikukuu yangu yasibakizwe mpaka asubuhi.

19“Utaleta malimbuko bora ya ardhi yako katika nyumba ya Bwana Mungu wako.

“Usimchemshe mwana-mbuzi katika maziwa ya mama yake.

Malaika Wa Mungu Kuandaa Njia

2023:20 Mwa 16:7; Kut 15:17; 32:34“Tazama, ninamtuma malaika akutangulie mbele yako akulinde njiani na kukuleta mpaka mahali nilipoandaa. 2123:21 Kum 18:19; Yer 13:15; Kum 29:20; 2Fal 24:4; Mao 1:17; Hes 17:10; Kum 9:7; 31:27; Yos 24:19; Za 25:7; 78:8, 40; 106:33; 107; 11; 1Yn 5:16; Kut 3:15Mtamtii na kusikiliza kile anachokisema. Usiasi dhidi yake; hatakusamehe uasi wako, kwa maana Jina langu limo ndani yake. 2223:22 Kut 15:26; Mwa 12:3; Isa 41:11; Yer 30:20Kama ukitii kweli kweli kile asemacho na kufanya yote nisemayo, nitakuwa adui wa adui zako, na nitawapinga wale wakupingao. 2323:23 Hes 13:29; 21:21; Yos 3:10; 24:8-10; 24:8-11; Ezr 9:1Malaika wangu atatangulia mbele yako na kukuleta katika nchi ya Waamori, Wahiti, Waperizi, Wakanaani, Wahivi na Wayebusi, nami nitawafutilia mbali. 2423:24 Kut 20:5; Law 18:3; 20:23; Kum 9:4; 12:30-31; Yer 10:2; Kut 34:13; Hes 33:52; Kum 7:5; 12:3; Amu 2:2; 2Fal 18:4; 23:14; Kum 16:22; 1Fal 14:23; 3:2; 10:26; 17:20; 2Nya 14:2-3; Isa 27:9Usiisujudie miungu yao, au kuiabudu, wala kufuata desturi yao. Utayabomoa kabisa na kuvunjavunja mawe yao ya ibada vipande vipande. 2523:25 Mt 4:10; Law 26:3-13; Kum 7:12-15; 28:1-14; Kut 15:26Utamwabudu Bwana Mungu wako, na baraka zake zitakuwa juu ya vyakula vyako na maji yako. Nami nitaondoa maradhi miongoni mwako, 2623:26 Law 26:3-4; Kum 7:14; 28:4; Mal 3:11; Mwa 15:15; Kum 4:1, 40; 21:12na hakuna atakayeharibu mimba wala atakayekuwa tasa katika nchi yako. Nami nitakupa maisha makamilifu.

2723:27 Mwa 35:5; Kut 15:14; 14:24; Kum 7:23; 2Sam 22:41; Za 18:40; 21:12“Nitapeleka utisho wangu mbele yako na kufadhaisha kila taifa utakalolifikia. Nitafanya adui zako wote wakupe kisogo na kukimbia. 2823:28 Kum 7:20; Yos 24:12; Kut 33:2; 34:11, 24; Hes 13:29; Kum 4:38; 11:23; 18:12; Yos 3:10; 24:11; Za 78:55Nitatanguliza manyigu mbele yako kuwafukuza Wahivi, Wakanaani na Wahiti waondoke njiani mwako. 2923:29 Kum 7:22Lakini sitawafukuza kwa mara moja, kwa sababu nchi itabaki ukiwa na wanyama pori watakuwa wengi mno kwako. 3023:30 Yos 23:5Nitawafukuza kidogo kidogo mbele yako, mpaka uwe umeongezeka kiasi cha kutosha kuimiliki nchi.

3123:31 Mwa 2:14; Kum 34:2; Ezr 4:20; Kum 7:24; 9:3; Yos 21:44; 24:12-18; Za 80:8“Nitaweka mipaka ya nchi yako kuanzia Bahari ya Shamu hadi Bahari ya Wafilisti, na kuanzia jangwani hadi Mto Frati. Nitawatia watu wanaoishi katika nchi hizo mikononi mwako, nawe utawafukuza watoke mbele yako. 3223:32 Mwa 26:28; Kut 34:12; Kum 7:2; Yos 9:7; Amu 2:2; 1Sam 11:1; 1Fal 15:19; 20:34; Eze 17:13Usifanye agano lolote nao wala na miungu yao. 3323:33 Kut 10:7; Za 106:36Usiwaache waishi katika nchi yako, la sivyo watakusababisha utende dhambi dhidi yangu, kwa sababu ibada ya miungu yao hakika itakuwa mtego kwako.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 23:1-33

Malamulo a Zachilungamo ndi Zachifundo

1“Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.

2“Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri. 3Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.

4“Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo. 5Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.

6“Usakhotetse milandu ya anthu osauka. 7Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.

8“Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.

9“Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.

Malamulo a Nthawi Zopuma

10“Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi. 11Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.

12“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.

13“Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.

Masiku Atatu Akulu a Chikondwerero

14“Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.

15“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto.

“Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.

16“Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda.

“Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.

17“Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.

18“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti.

“Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.

19“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu.

“Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.

Kutsogolera kwa Mngelo wa Mulungu

20“Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza. 21Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa. 22Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu. 23Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo. 24Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo. 25Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu. 26Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.

27“Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani. 28Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu. 29Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani. 30Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.

31“Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa. 32Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo. 33Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”