Kutoka 22 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Kutoka 22:1-31

Ulinzi Wa Mali

122:1 Law 6:1-7; 2Sam 12:6; Mit 6:31; Lk 19:8“Kama mtu akiiba maksai au kondoo na kumchinja au kumuuza, ni lazima alipe ngʼombe watano badala ya maksai mmoja na kondoo wanne badala ya kondoo mmoja.

222:2 Ay 24:16; Yer 2:34; Hos 7:1; Mt 6:19-20; 24:43; Hes 35:27; Kut 20:15; Law 19:11; Kum 5:19; Lk 18:20; Rum 13:9; Efe 4:28; 1Pet 4:15“Kama mwizi akishikwa anavunja nyumba akapigwa hata akafa, aliyemuua hana hatia ya kumwaga damu; 322:3 Kut 21:2; Mt 18:25lakini jambo hilo likitokea wakati jua limechomoza, huyo mtu atakuwa na hatia ya kumwaga damu.

“Mwizi huyo sharti alipe, lakini kama hana kitu, lazima auzwe ili alipe kwa ajili ya wizi wake.

422:4 1Sam 12:5; Mwa 43:12; Kut 21:16; Mit 6:31“Kama mnyama aliyeibwa akikutwa hai mikononi mwake, ikiwa ni maksai au punda au kondoo, lazima alipe mara mbili.

5“Kama mtu akichunga mifugo yake katika shamba au shamba la mizabibu, na akawaachia wajilishe katika shamba la mtu mwingine, ni lazima alipe vitu bora kutoka kwenye shamba lake mwenyewe au kutoka shamba lake la mizabibu.

622:6 Amu 15:5“Kama moto ukiwaka na kuenea kwenye vichaka vya miiba na kuteketeza miganda ya nafaka au nafaka ambayo haijavunwa, au kuteketeza shamba lote, mtu yule aliyewasha moto lazima alipe.

722:7 Law 6:2; Mwa 43:12“Kama mtu akimpa jirani yake fedha au mali nyingine amtunzie, na kama vikiibwa kutoka nyumba ya huyo jirani, kama mwizi atashikwa, lazima alipe mara mbili. 822:8 Kut 21:6; Kum 17:8-9Lakini mwizi asipopatikana, mwenye nyumba atafika mbele ya waamuzi ili kuthibitisha kuwa hakuchukua mali ya mwenzake. 922:9 Kum 25:1Pakiwepo jambo lolote la mali isiyo halali, ikiwa ni maksai, punda, kondoo, mavazi, ama mali yoyote iliyopotea ambayo fulani atasema, ‘Hii ni mali yangu,’ pande zote mbili wataleta mashauri yao mbele ya waamuzi. Yule ambaye waamuzi watamwona kuwa na hatia atamlipa jirani yake mara mbili.

10“Kama mtu akimpa jirani yake punda, ngʼombe, kondoo au mnyama mwingine yeyote amtunzie, akifa au akijeruhiwa au akichukuliwa wakati haonekani na mtu yeyote, 1122:11 Law 6:3; 1Fal 8:31; 2Nya 6:22; Ebr 6:16jambo hili kati yao wawili litaamuliwa kwa kuapa kiapo mbele za Bwana, kwamba huyo jirani hakuhusika na wizi wa mali ya jirani yake. Mwenye mali itampasa akubali jambo hili, na hakuna malipo yatakayohitajika. 12Lakini kama mnyama aliibwa kwa jirani, itampasa amlipe mwenye mnyama. 1322:13 Mwa 31:39Kama ameraruliwa na mnyama pori, ataleta mabaki ya mnyama kama ushahidi, naye hatadaiwa kulipa mnyama aliyeraruliwa.

14“Kama mtu akimwazima mnyama kutoka kwa jirani yake, na kama akiumia au akafa na mwenye mnyama hayupo, lazima amlipe huyo mnyama. 1522:15 Law 19:13; Ay 17:5Lakini mwenye mnyama akiwa angalipo na mnyama wake, mwazimaji hatalazimika kumlipa. Kama mnyama alikuwa amekodishwa, fedha iliyolipwa kwa kukodisha inatosha kwa kufidia hasara.

Uwajibikaji Wa Kijamii

1622:16 Kum 22:28; Mwa 34:12“Kama mtu akimshawishi bikira ambaye hajaposwa na akilala naye, lazima alipe mahari, kisha atamwoa msichana huyo. 17Baba wa msichana akikataa katakata kumpa huyo mtu huyo msichana wake, bado ni lazima huyo mtu atalipa mahari kama inavyostahili malipo ya ubikira.

1822:18 Kut 7:11; Law 19:26, 31; 20:27; Kum 18:17; 1Sam 28:3; 2Nya 33:6; Isa 57:3“Usiruhusu mwanamke mchawi aishi.

1922:19 Law 18:23; 20:15; Kum 27:21“Mtu yeyote aziniye na mnyama lazima auawe.

2022:20 Kut 20:23; 22:21“Mtu awaye yote anayemtolea mungu mwingine dhabihu isipokuwa Bwana, lazima aangamizwe.

21“Usimtendee mgeni vibaya au kumwonea, kwa kuwa nanyi mlikuwa wageni huko Misri.

2222:22 Kum 10:18; 24:6, 10-17; Ay 22:6-9; 24:3; 21; Za 68:5; 146:9; Mit 23:10; Isa 1:17; Yer 7:5-6; 21:12; 22:3; Eze 18:5-12; Zek 7:9-10; Mal 3:5; Yak 1:27“Usimdhulumu mjane wala yatima. 2322:23 Lk 18:7; Kum 10:18; 15:9; 24:15; Ay 34:28; 35:9; Za 10:14-17; 12:5; 18:6; Yak 5:4Kama ukifanya hivyo nao wakinililia, hakika nitasikia kilio chao. 2422:24 Za 10:9; 69:24; Mao 5:3Hasira yangu itawaka, nami nitawaua kwa upanga, wake zenu watakuwa wajane na watoto wenu watakuwa yatima.

2522:25 Law 25:35-37; Kum 15:7-11; 23:20; Neh 5:7-10; Za 15:5; Eze 18:8“Kama ukimkopesha mmojawapo wa watu wangu fedha ambaye ni mhitaji, usiwe kama mtu mkopesha fedha; usimtoze riba. 2622:26 Mit 20:16; Eze 33:15; Amo 2:8Kama ukichukua vazi la jirani kama rehani, ulirudishe kwake kabla jua kuzama, 2722:27 Kum 24:13, 17; Ay 22:6; 24:7; 29:11; 31:19-20; Eze 18:12, 16; Kut 34:6; Kum 4:31; 2Nya 30:9; Neh 9:17; Za 99:8; 103:8; 116:5; 145:8; Yoe 2:13; Yon 4:2kwa kuwa vazi lake ndilo pekee alilo nalo la kumfunika mwili wake. Ni nini kingine atajifunika nacho? Atakaponililia, nitasikia, kwa kuwa nina huruma.

2822:28 Kut 20:7; 2Sam 16:5, 9; 1Sam 19:21; 1Fal 21:10; 2Fal 2:23; Za 102; 8; Mhu 10:20; Mdo 23:5“Usimkufuru Mungu au kumlaani mtawala wa watu wako.

2922:29 Kut 23:15-19; 34:20-26; Law 19:24; 23:10; Hes 18:13; 28:26; Kum 18:4; 26:2, 10; 1Sam 6:3; Neh 10:35; Mit 3:9; Mal 3:10; Kut 13:2; Hes 8:16-17; Lk 2:23“Usiache kutoa sadaka kutoka ghala lako au mapipa yako.

“Lazima unipe mzaliwa wa kwanza wa wana wako. 3022:30 Kut 34:19; Kum 15:19; Law 12:3; 22:27; Mwa 17:12Ufanye vivyo hivyo kwa ngʼombe wako na kwa kondoo wako. Waache wakae na mama zao kwa siku saba, lakini siku ya nane unipe.

3122:31 Kut 19:6; Law 19:2; 22:31; Ezr 9:2; Law 7:24; 17:15; 22:8; Kum 14:21; Eze 4:14; 44:31“Ninyi mtakuwa watu wangu watakatifu. Kwa hiyo msile nyama ya mnyama aliyeraruliwa na wanyama pori; mtupieni mbwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 22:1-31

Za Kuteteza Katundu

1“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.

2“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe. 3Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha.

“Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.

4“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.

5“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.

6“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.

7“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho. 8Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo. 9Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.

10“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona, 11ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu. 12Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo. 13Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.

14“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira. 15Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.

Malamulo a Kakhalidwe ka Anthu

16“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake. 17Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.

18“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.

19“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.

20“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.

21“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.

22“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye. 23Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo. 24Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.

25“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja. 26Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe 27chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.

28“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.

29“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka.

“Mundipatse ana anu achisamba aamuna. 30Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.

31“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”