Isaya 66 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 66:1-24

Hukumu Na Matumaini

166:1 2Nya 6:18; Mt 23:22; Mdo 17:24; 1Fal 8:27; Mt 5:34-35; Za 2:4; 2Sam 7:7Hili ndilo asemalo Bwana,

“Mbingu ni kiti changu cha enzi,

nayo dunia ni mahali pa kuweka miguu yangu.

Iko wapi nyumba mtakayoijenga kwa ajili yangu?

Mahali pangu pa kupumzikia patakuwa wapi?

266:2 Isa 40:26; Mdo 17:24; Ezr 9:4; Mit 28:14; Mdo 7:50; Isa 57:15; Mt 5:3-4; Lk 18:13-14Je, mkono wangu haukufanya vitu hivi vyote,

hivyo vikapata kuwepo?”

asema Bwana.

“Mtu huyu ndiye ninayemthamini:

yeye ambaye ni mnyenyekevu

na mwenye roho yenye toba,

atetemekaye asikiapo neno langu.

366:3 Isa 1:11; Law 2:2; Isa 57:17; Kum 27:15; Eze 8:9-13Lakini yeyote atoaye dhabihu ya fahali

ni kama yeye auaye mtu,

na yeyote atoaye sadaka ya mwana-kondoo,

ni kama yule avunjaye shingo ya mbwa.

Yeyote atoaye sadaka ya nafaka,

ni kama yule aletaye damu ya nguruwe,

na yeyote afukizaye uvumba wa kumbukumbu,

ni kama yule aabuduye sanamu.

Wamejichagulia njia zao wenyewe,

nazo nafsi zao zinafurahia machukizo yao.

466:4 Mit 10:24; 1Sam 8:19; Mit 1:24; 2Fal 21:2-6; Isa 10:12; 41:28; 65:12Hivyo, mimi pia nitawachagulia mapigo makali,

nami nitaleta juu yao kile wanachokiogopa.

Kwa maana nilipoita, hakuna yeyote aliyejibu,

niliposema, hakuna yeyote aliyesikiliza.

Walifanya maovu machoni pangu

na kuchagua lile linalonichukiza.”

566:5 Za 38:20; Yn 15:18-21; Lk 13:17; Tit 2:13; Ezr 9:4; Isa 60:15; 44:9Sikieni neno la Bwana,

ninyi mtetemekao kwa neno lake:

“Ndugu zenu wanaowachukia ninyi

na kuwatenga ninyi kwa sababu ya Jina langu, wamesema,

Bwana na atukuzwe,

ili tupate kuona furaha yenu!’

Hata sasa wataaibika.

666:6 1Sam 2:10; Za 68:33; Law 26:28; Isa 65:6; Yoe 3:7Sikieni hizo ghasia kutoka mjini,

sikieni hizo kelele kutoka hekaluni!

Ni sauti ya Bwana ikiwalipa adui zake

yote wanayostahili.

766:7 Isa 54:1; Ufu 12:5“Kabla hajasikia utungu, alizaa;

kabla hajapata maumivu,

alizaa mtoto mwanaume.

866:8 Isa 64:4; Yer 18:13; Isa 49:20, 21Ni nani amepata kusikia jambo kama hili?

Ni nani amepata kuona mambo kama haya?

Je, nchi yaweza kuzaliwa kwa siku moja,

au taifa laweza kutokea mara?

Mara Sayuni alipoona utungu,

alizaa watoto wake.

966:9 Isa 37:3Je, nilete mwana hadi wakati wa kuzaliwa

na nisizalishe?” asema Bwana.

“Je, nifunge tumbo la uzazi

wakati mimi ndiye nizalishaye?”

asema Mungu wako.

1066:10 Kum 32:43; Rum 15:10; Za 26:8; Isa 25:9; 57:19; 61:2“Shangilieni pamoja na Yerusalemu na mfurahi kwa ajili yake,

ninyi nyote mnaompenda,

shangilieni kwa nguvu pamoja naye,

ninyi nyote mnaoomboleza juu yake.

1166:11 Hes 11:12; Isa 60:16; Mwa 49:25; Isa 25:6; Hes 25:1Kwa kuwa mtanyonya na kutosheka

katika faraja ya matiti yake;

mtakunywa sana,

na kuufurahia wingi wa mafuriko ya ustawi wake.”

1266:12 Isa 33:21; 48:18; Hes 11:12; Isa 60:4-5; Za 72:3; 119:165; Isa 9:6Kwa kuwa hili ndilo asemalo Bwana:

“Nitamwongezea amani kama mto,

nao utajiri wa mataifa kama kijito kifurikacho;

utanyonya na kuchukuliwa mikononi mwake

na kubembelezwa magotini pake.

1366:13 Isa 40:1; 2Kor 1:4; 1The 2:7; Isa 49:15Kama mama anavyomfariji mtoto wake,

ndivyo nitakavyokufariji wewe,

nawe utafarijiwa huko Yerusalemu.”

1466:14 Eze 37:1; Isa 10:5; 30:27; 25:9; Za 72:16; Isa 54:17; 41:20Wakati mtakapoona jambo hili, mioyo yenu itashangilia,

nanyi mtastawi kama majani;

mkono wa Bwana utajulikana kwa watumishi wake,

bali ghadhabu yake kali

itaonyeshwa kwa adui zake.

1566:15 2Fal 2:11; Za 68:17; Kum 28:20; Za 39:11; Isa 1:31; 42:25Tazama, Bwana anakuja na moto,

magari yake ya vita ni kama upepo wa kisulisuli,

atateremsha hasira yake kwa ghadhabu kali,

na karipio lake pamoja na miali ya moto.

1666:16 Amo 7:4; Eze 24:21; Isa 1:20; 30:30; 13:9-11; Yer 2:35; Eze 36:5; Isa 10:4Kwa maana kwa moto na kwa upanga wake

Bwana atatekeleza hukumu juu ya watu wote,

nao wengi watakuwa ni wale

waliouawa na Bwana.

1766:17 Isa 65:3; Za 37:20; Isa 1:28-29; Law 11:7, 29“Watu wote wanaojiweka wakfu na kujitakasa wenyewe ili kwenda bustanini, wakimfuata aliye katikati ya wale ambao hula nyama za nguruwe na panya pamoja na vitu vingine vilivyo machukizo, watafikia mwisho wao pamoja,” asema Bwana.

1866:18 Mit 24:2; Isa 65:2; 2:3; Zek 12:3; Kut 16:17; Isa 59:19“Nami, kwa sababu ya matendo yao na mawazo yao, niko karibu kuja na kukusanya mataifa yote na lugha zote, nao watakuja na kuuona utukufu wangu.

1966:19 Lk 2:34; Isa 11:10-11; Mt 24:30; Eze 27:10; 1Nya 16:24; Isa 24:15; Yer 46:9“Nitaweka ishara katikati yao, nami nitapeleka baadhi ya hao walionusurika kwa mataifa, hadi Tarshishi, kwa Puli66:19 Puli hapa inamaanisha Libya. na Waludi (wanaojulikana kama wapiga upinde), kwa Tubali na Uyunani, hadi visiwa vya mbali ambavyo havijasikia juu ya sifa zangu au kuuona utukufu wangu. Watatangaza utukufu wangu miongoni mwa mataifa. 2066:20 Isa 52:11; Rum 15:16; Yer 31:23; Eze 34:13; Kum 33:19; Yer 25:22Nao watawaleta ndugu zenu wote, kutoka mataifa yote, mpaka kwenye mlima wangu mtakatifu katika Yerusalemu kama sadaka kwa Bwana, juu ya farasi, katika magari ya vita na magari makubwa, juu ya nyumbu na ngamia,” asema Bwana. “Watawaleta, kama Waisraeli waletavyo sadaka zao za nafaka, katika Hekalu la Bwana, katika vyombo safi kwa kufuata desturi za ibada. 2166:21 Kut 19:6; 1Pet 2:5-9Nami nitachagua baadhi yao pia wawe makuhani na Walawi,” asema Bwana.

2266:22 2Pet 3:13; Isa 65:17; 1Pet 1:4-5; Isa 48:19; Ebr 12:26-27; Yn 10:27-29“Kama vile mbingu mpya na nchi mpya ninazozifanya zitakavyodumu mbele zangu,” asema Bwana, “ndivyo jina lenu na wazao wenu watakavyodumu. 2366:23 Eze 46:1-3; Ufu 15:4; Za 22:29; Zek 14:16; Isa 19:21; 44:5Kutoka Mwezi Mpya hata mwingine, na kutoka Sabato hadi nyingine, wanadamu wote watakuja na kusujudu mbele zangu,” asema Bwana. 2466:24 Isa 14:11; 1:31; Mt 25:41; Mk 9:48; Za 110:6; Isa 1:2“Nao watatoka nje na kuona maiti za wale walioniasi mimi. Funza wao hawatakufa, wala moto wao hautazimika, nao watakuwa kitu cha kuchukiza sana kwa wanadamu wote.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 66:1-24

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?”

Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

3Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

amaphanso munthu,

ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,

amaphanso galu.

Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya

amaperekanso magazi a nkhumba.

Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso

amapembedzanso fano.

Popeza iwo asankha njira zawozawo,

ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.

4Inenso ndawasankhira chilango chowawa

ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.

Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,

pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.

Anachita zoyipa pamaso panga

ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

5Imvani mawu a Yehova,

inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:

“Abale anu amene amakudani,

ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,

‘Yehova alemekezeke

kuti ife tione chimwemwe chanu!’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6Imvani mfuwu mu mzinda,

imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!

Limenelo ndi liwu la Yehova,

kulanga adani ake onse.

7“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

wachira kale;

asanayambe kumva ululu,

wabala kale mwana wamwamuna.

8Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

Ndani anazionapo zinthu zoterezi?

Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,

kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?

Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa

nthawi yomweyo anabereka ana ake.

9Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.

“Kodi ndingatseke mimba

pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,

kondwera nayeni kwambiri,

nonse amene mumamulira.

11Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri

wa mʼmawere

a chitonthozo chake.”

12Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,

ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,

kapena kumufungata pa miyendo yake.

13Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

moteronso Ine ndidzakusangalatsani;

ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

14Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira

ndi kuti ndimakwiyira adani anga.

15Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;

Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake

ndi malawi amoto.

16Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

ndi moto ndi lupanga,

Yehova adzapha anthu ambiri.

17Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”