Isaya 6 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 6:1-13

Agizo Kwa Isaya

16:1 2Nya 26:22-23; Hes 12:8; Ufu 4:2; 1:13; 2Fal 15:7; Kut 24:10; Ufu 4:2; Yn 12:41; 1Fal 22:19Katika mwaka ule Mfalme Uzia alikufa, nilimwona Bwana ameketi katika kiti cha enzi, kilicho juu na kilichotukuzwa sana, nalo pindo la joho lake likajaza Hekalu. 26:2 Eze 1:5; 10:15; 1:11; Ufu 4:8Juu yake walikuwepo maserafi, kila mmoja alikuwa na mabawa sita: Kwa mabawa mawili walifunika nyuso zao, kwa mengine mawili walifunika miguu yao, na kwa mawili walikuwa wakiruka. 36:3 Ufu 4:8; Kut 16:7; 15:11; Hes 14:21; Isa 54:5; 11:9; Za 89:9; 72:19; 89:8; Mal 1:11Nao walikuwa wakiitana kila mmoja na mwenzake:

“Mtakatifu, Mtakatifu, Mtakatifu

ni Bwana Mwenye Nguvu Zote;

dunia yote imejaa utukufu wake.”

46:4 Kut 19:18; Eze 43:5; 44:4; Ufu 15:8Kwa sauti zao, miimo ya milango na vizingiti vilitikisika, nalo Hekalu likajaa moshi.

56:5 Isa 59:3; Yer 9:3-8; 51:57; Hes 17:12; Kum 5:26; Kut 6:12; 24:10; Isa 24:23; 5:8; Lk 5:8; Yer 5:3; 51:57; Ay 42:5Ndipo nikalia, “Ole wangu! Nimeangamia! Kwa kuwa mimi ni mtu mwenye midomo michafu, nami ninaishi katikati ya watu wenye midomo michafu, nayo macho yangu yamemwona Mfalme, Bwana Mwenye Nguvu Zote.”

66:6 Law 10:1; Eze 10:2Ndipo mmoja wa wale maserafi akaruka kunijia akiwa na kaa la moto linalowaka mkononi mwake, ambalo alikuwa amelichukua kwa koleo kutoka madhabahuni. 76:7 Dan 10:16; 12:3; 1Yn 1:7; Isa 45:25; Yer 1:9; Law 26:41Akanigusa nalo kinywa changu na kusema, “Tazama, hili limegusa midomo yako, uovu wako umeondolewa, nayo dhambi yako imesamehewa.”

86:8 Mdo 9:4; Ay 40:9; Yer 26:12-15; Mwa 1:26; 22:1; Kut 3:4Kisha nikasikia sauti ya Bwana ikisema, “Nimtume nani? Ni nani atakayekwenda kwa ajili yetu?”

Nami nikasema, “Mimi hapa. Nitume mimi!”

96:9 Mt 13:15; Lk 8:10; Mt 28:196:9 Amo 7:15; Yer 5:21; Eze 3:11; Mt 13:15; Lk 8:10Akasema, “Nenda ukawaambie watu hawa:

“ ‘Mtaendelea daima kusikiliza,

lakini kamwe hamtaelewa;

mtaendelea daima kutazama,

lakini kamwe hamtatambua.’

106:10 Kut 4:21; Kum 32:39; 29:4; Eze 12:2; Isa 44:18; Yn 12:40; Mk 4:12; 8:18Fanya mioyo ya watu hawa kuwa migumu,

fanya masikio yao yasisikie,

na upofushe macho yao.

Wasije wakaona kwa macho yao,

na wakasikiliza kwa masikio yao,

wakaelewa kwa mioyo yao,

nao wakageuka, nikawaponywa.”

116:11 Yer 4:13; Za 79:5; 79:1; Isa 24:10; Yer 35:17; Za 119:11; Law 26:31, 43Ndipo nikasema, “Hadi lini, Ee Bwana?”

Naye akanijibu:

“Hadi miji iwe imeachwa magofu

na bila wakazi,

hadi nyumba zitakapobaki bila watu,

na mashamba yatakapoharibiwa na kuangamizwa,

126:12 Kum 28:64; Yer 30:17; 4:29; Isa 5:5-9; 60:15; 62:4; 62:4hadi Bwana atakapokuwa amekwisha kumpeleka kila mmoja mbali sana,

na nchi itakapokuwa imeachwa kabisa.

136:13 Rum 11:5; Ay 14:7; 14:8; Isa 10:22; Kum 14:2; Law 27:30; Isa 5:6; 1:9Hata kama sehemu ya kumi ya watu watabaki katika nchi,

itaharibiwa tena.

Lakini kama vile mvinje na mwaloni

ibakizavyo visiki inapokatwa,

ndivyo mbegu takatifu

itakavyokuwa kisiki katika nchi.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 6:1-13

Masomphenya a Yesaya

1Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova. 2Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira. 3Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti

“Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse.

Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”

4Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.

5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”

6Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe. 7Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”

8Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?”

Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”

9Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa:

“ ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;

kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’

10Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;

uwagonthetse makutu,

ndipo uwatseke mʼmaso.

Mwina angaone ndi maso awo,

angamve ndi makutu awo,

angamvetse ndi mitima yawo,

kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”

11Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?”

Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti,

“Mpaka mizinda itasanduka mabwinja

nʼkusowa wokhalamo,

mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo,

mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,

12mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali,

dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.

13Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko,

nachonso chidzawonongedwa.

Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu

imasiyira chitsa pamene ayidula,

chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”