Isaya 51 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 51:1-23

Wokovu Wa Milele Kwa Sayuni

151:1 Isa 46:3; Kum 7:13; Mit 26:27; Kum 16:20; Za 94:15; Isa 63:8; Rum 9:30-31; Isa 17:10“Nisikilizeni, ninyi mnaofuatia haki

na mnaomtafuta Bwana:

Tazameni mwamba ambako mlichongwa,

na mahali pa kuvunjia mawe ambako mlichimbwa;

251:2 Mwa 17:6; Ebr 11:11; Mwa 12:2; Isa 29:22; Rum 4:16mwangalieni Abrahamu, baba yenu,

na Sara, ambaye aliwazaa.

Wakati nilipomwita alikuwa mmoja tu,

nami nikambariki na kumfanya kuwa wengi.

351:3 Isa 40:1; Mwa 13:10; Yer 16:9; Za 102:13; Isa 44:26; Za 51:18; Isa 61:4Hakika Bwana ataifariji Sayuni,

naye atayaangalia kwa huruma magofu yake yote;

atayafanya majangwa yake yawe kama Edeni,

nazo sehemu zake zisizolimika ziwe kama bustani ya Bwana.

Shangwe na furaha zitakuwako ndani yake,

shukrani na sauti za kuimba.

451:4 Kut 6:7; Isa 26:18; 42:4-6; Za 50:7; Isa 3:15; 63:8“Nisikilizeni, watu wangu;

nisikieni, taifa langu:

Sheria itatoka kwangu;

haki yangu itakuwa nuru kwa mataifa.

551:5 Isa 35:4; 46:13; Za 98:1; 85:9; Mwa 49:10; Isa 52:10Haki yangu inakaribia mbio,

wokovu wangu unakuja,

nao mkono wangu utaleta hukumu kwa mataifa.

Visiwa vitanitegemea

na kungojea mkono wangu kwa matumaini.

651:6 Za 37:20; Lk 21:33; Za 102:25-26; Ebr 1:10-12; Mt 24:35; Isa 54:10Inueni macho yenu mbinguni,

mkaitazame dunia chini;

mbingu zitatoweka kama moshi,

dunia itachakaa kama vazi,

na wakazi wake kufa kama mainzi.

Bali wokovu wangu utadumu milele,

haki yangu haitakoma kamwe.

751:7 Za 37:31; Mt 10:28; Mdo 5:41; Za 119:39; Lk 6:22; Isa 54:4; 50:7“Nisikieni, ninyi mnaojua lililo sawa,

ninyi watu ambao mna sheria yangu mioyoni mwenu:

Msiogope mashutumu ya wanadamu

wala msitiwe hofu na matukano yao.

851:8 Ay 13:28; Yak 5:2; Isa 14:11Kwa maana nondo atawala kama vazi,

nao funza atawatafuna kama sufu.

Lakini haki yangu itadumu milele,

wokovu wangu kwa vizazi vyote.”

951:9 Kut 32:7; Za 68:30; Ay 26:12; Eze 29:3; Amu 5:12; Mwa 18:14; Za 65:6; 74:13Amka, Amka! Jivike nguvu,

ewe mkono wa Bwana,

Amka, kama siku zilizopita,

kama vile vizazi vya zamani.

Si ni wewe uliyemkata Rahabu vipande vipande,

uliyemchoma yule joka?

1051:10 Zek 10:11; Kut 14:21; Ufu 16:12; Kut 15:5, 8, 13; Ay 36:30Si ni wewe uliyekausha bahari,

maji ya kilindi kikuu,

uliyefanya barabara katika vilindi vya bahari

ili waliokombolewa wapate kuvuka?

1151:11 Isa 35:9; 44:23; 48:20; Ufu 7:17; Yer 31:13; 30:19; Sef 3:17; Isa 30:19Wale waliolipiwa fidia na Bwana watarudi.

Wataingia Sayuni wakiimba;

furaha ya milele itakuwa taji juu ya vichwa vyao.

Furaha na shangwe zitawapata,

huzuni na kulia kwa uchungu kutatoweka.

1251:12 Za 118:6; 2Kor 1:3-4; 1Pet 1:24; Isa 15:6; 2Fal 1:15; Isa 2:22; 40:6-7“Mimi, naam mimi,

ndimi niwafarijie ninyi.

Ninyi ni nani hata kuwaogopa

wanadamu wanaokufa,

wanadamu ambao ni majani tu,

1351:13 Ay 8:13; 4:17; Isa 17:10; 7:4; Ay 20:7; Isa 45:11; 48:13; 9:4kwamba mnamsahau Bwana Muumba wenu,

aliyezitanda mbingu

na kuiweka misingi ya dunia,

kwamba mnaishi katika hofu siku zote

kwa sababu ya ghadhabu ya mdhalimu,

ambaye nia yake ni kuangamiza?

Iko wapi basi ghadhabu ya mdhalimu?

1451:14 Isa 49:10; Zek 9:11; Isa 42:7Wafungwa waliojikunyata kwa hofu

watawekwa huru karibuni;

hawatafia kwenye gereza lao,

wala hawatakosa chakula.

1551:15 Kut 14:21; Isa 43:16; Za 74:13; Yer 31:35; Za 93:3; Isa 13:4Kwa maana Mimi ndimi Bwana, Mungu wako,

ambaye huisukasuka bahari ili mawimbi yake yangurume:

Bwana Mwenye Nguvu Zote ndilo jina lake.

1651:16 Kut 4:12-15; 2Pet 3:13; Kum 18:18; 33:22; Zek 8:8; Eze 14:11; Yer 7:23; 24:7Nimeweka maneno yangu kinywani mwako

na kukufunika kwa uvuli wa mkono wangu:

Mimi niliyeweka mbingu mahali pake,

niliyeweka misingi ya dunia,

niwaambiaye Sayuni,

‘Ninyi ni watu wangu.’ ”

Kikombe Cha Ghadhabu Ya Bwana

1751:17 Amu 5:12; Ay 21:20; Ufu 16:19; Za 60:3; 16:5; Mt 20:22; Isa 42:25Amka, amka!

Simama, ee Yerusalemu,

wewe uliyekunywa kutoka mkono wa Bwana

kikombe cha ghadhabu yake,

wewe uliyekunywa mpaka kufikia machujo yake,

kikombe kile cha kunywea

kiwafanyacho watu kuyumbayumba.

1851:18 Ay 31:18; Za 88:18; Isa 49:21; 41:13Kati ya wana wote aliowazaa

hakuwepo hata mmoja wa kumwongoza,

kati ya wana wote aliowalea

hakuwepo hata mmoja wa kumshika mkono.

1951:19 Isa 40:2; 47:9; 49:13; Yer 14:12; 24:10Majanga haya mawili yamekuja juu yako:

ni nani awezaye kukufariji?

Maangamizi, uharibifu, njaa na upanga:

ni nani awezaye kukutuliza?

2051:20 Yer 14:16; Mao 2:19; Isa 5:25; Ay 18:10; Yer 44:6; Ay 40:11; Kum 28:20Wana wako wamezimia,

wamelala kwenye mwanzo wa kila barabara,

kama swala aliyenaswa kwenye wavu.

Wamejazwa na ghadhabu ya Bwana

na makaripio ya Mungu wako.

2151:21 Isa 14:32; 29:9; Mao 3:15Kwa hiyo sikiliza hili, wewe uliyeteswa,

uliyelewa, lakini si kwa mvinyo.

2251:22 Yer 50:34; Hab 2:16; Isa 49:25; Yer 25:15; Mt 20:2251:22 Yer 50:34; Hab 2:16; Isa 49:25; Yer 25:15; Mt 20:22Hili ndilo asemalo Bwana Mwenyezi wako,

Mungu wako, yeye ambaye huwatetea watu wake:

“Tazama, nimeondoa mkononi mwako

kikombe kilichokufanya uyumbayumbe;

kutoka kikombe hicho,

kikombe cha kunywa cha ghadhabu yangu,

kamwe hutakunywa tena.

2351:23 Yer 49:12; Zek 12:3; Yos 10:24; Isa 14:4; 49:26; Yer 25:15-17, 26; Mik 7:1051:23 Yer 49:12; Zek 12:3; Yos 10:24; Isa 14:4; 49:26; Yer 25:15-17, 26; Mik 7:10Nitakiweka mikononi mwa watesi wako,

wale waliokuambia,

‘Anguka kifudifudi

ili tuweze kutembea juu yako.’

Ukaufanya mgongo wako kama ardhi,

kama njia yao ya kupita.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 51:1-23

Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni

1“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso

ndiponso amene mumafunafuna Yehova:

Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa

ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;

2taganizani za Abrahamu, kholo lanu,

ndi Sara, amene anakubalani.

Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,

koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.

3Yehova adzatonthozadi Ziyoni,

ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;

Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,

malo ake owuma ngati munda wa Yehova.

Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda

ndi kundiyamika.

4“Mverani Ine, anthu anga:

tcherani khutu, inu mtundu wanga:

malangizo adzachokera kwa Ine;

cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.

5Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.

Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;

ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.

Mayiko akutali akundiyembekezera.

Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.

6Kwezani maso anu mlengalenga,

yangʼanani pansi pa dziko;

mlengalenga udzazimirira ngati utsi,

dziko lapansi lidzatha ngati chovala

ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.

Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,

chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.

7“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,

anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;

musaope kudzudzulidwa ndi anthu

kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.

8Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;

mbozi idzawadya ngati thonje.

Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,

chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”

9Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,

Inu Yehova;

dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,

monga nthawi ya mibado yakale.

Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,

amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?

10Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,

madzi ozama kwambiri aja?

Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,

kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?

11Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera

nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;

chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.

Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,

chisoni ndi kubuwula zidzathawa.

12Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.

Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?

Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.

13Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,

amene anayala za mlengalenga

ndi kuyika maziko a dziko lapansi.

Inu nthawi zonse mumaopsezedwa

chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani

amene angofuna kukuwonongani.

Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?

14Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;

sadzalowa mʼmanda awo,

kapena kusowa chakudya.

15Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.

Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu

ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.

Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,

ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,

ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”

Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu

17Dzambatuka, dzambatuka!

Imirira iwe Yerusalemu.

Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo

chimene Yehova anakupatsa.

Iwe amene unagugudiza

chikho chochititsa chizwezwe.

18Mwa ana onse amene anabereka,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;

mwa ana onse amene analera,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.

19Mavuto awiriwa akugwera iwe.

Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.

Ndani angakumvere chisoni?

Ndani angakutonthoze?

20Ana ako akomoka;

ali lambalamba pa msewu,

ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.

Ukali wa Yehova

ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.

21Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,

iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.

22Ambuye Yehova wanu,

Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,

“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako

chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;

sudzamwanso chikho

cha ukali wanga.

23Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,

amene ankakuwuza kuti,

‘gona pansi tikuyende pa msana.’

Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,

ngati msewu woti ayendepo.”