Isaya 48 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 48:1-22

Israeli Mkaidi

148:1 Kum 6:13; Kut 23:13; Dan 8:12; Zek 8:3; Mwa 17:5; 29:35; Isa 19:18“Sikilizeni hili, ee nyumba ya Yakobo,

ninyi mnaoitwa kwa jina la Israeli,

na mnaotoka katika ukoo wa Yuda,

ninyi mnaoapa kwa jina la Bwana,

mnaomwomba Mungu wa Israeli,

lakini si katika kweli au kwa haki;

248:2 Neh 11:1; Rum 2:17; Mik 3:11; Isa 1:26; Mt 4:5; Isa 10:20; 47:4ninyi mnaojiita raiya wa mji mtakatifu,

na kumtegemea Mungu wa Israeli,

Bwana Mwenye Nguvu Zote ndilo jina lake:

348:3 Isa 40:21; 45:21; Yos 21:45; Isa 41:22; 17:14; 30:13Nilitoa unabii mambo ya kwanza tangu zamani,

kinywa changu kiliyatangaza na kuyafanya yajulikane;

kisha ghafula nikayatenda, nayo yakatokea.

448:4 Kum 9:27; 31:27; Mdo 5:21; Isa 9:9; Kut 32:9; Eze 3:9; Mdo 7:51Kwa kuwa nalijua jinsi ulivyokuwa mkaidi;

mishipa ya shingo yako ilikuwa chuma,

kipaji chako cha uso kilikuwa shaba.

548:5 Yer 44:15-18; Isa 42:9; 40:21Kwa hiyo nilikuambia mambo haya tangu zamani,

kabla hayajatokea nilikutangazia

ili usije ukasema,

‘Sanamu zangu zilifanya hayo;

kinyago changu cha mti na mungu wangu wa chuma aliyaamuru.’

648:6 Isa 41:22; Rum 16:25Umesikia mambo haya; yaangalie hayo yote.

Je, hutayakubali?

“Kuanzia sasa na kuendelea nitakueleza mambo mapya,

juu ya mambo yaliyofichika usiyoyajua.

748:7 Isa 65:18; 45:21; Kut 6:7Yameumbwa sasa, wala si tangu zamani;

hukupata kuyasikia kabla ya siku ya leo.

Hivyo huwezi kusema,

‘Naam, niliyajua hayo.’

848:8 Za 58:3; Kum 9:24; Isa 41:24; Mal 2:11-14; Isa 43:27Hujayasikia wala kuyaelewa,

tangu zamani sikio lako halikufunguka.

Ninafahamu vyema jinsi ulivyo mdanganyifu,

uliitwa mwasi tangu kuzaliwa kwako.

948:9 Yos 7:9; Ay 9:13; Za 78:38; 1Sam 12:22; Isa 37:35; 30:18Kwa ajili ya Jina langu mwenyewe

ninaichelewesha ghadhabu yangu,

kwa ajili ya sifa zangu nimeizuia isikupate,

ili nisije nikakukatilia mbali.

1048:10 Za 66:10Tazama, nimekusafisha, ingawa si kama fedha,

nimekujaribu katika tanuru ya mateso.

1148:11 1Sam 12:22; Law 18:21; Isa 42:8; Kum 32:26-27; Eze 20:9; Yer 14:7, 21Kwa ajili yangu mwenyewe,

kwa ajili yangu mwenyewe, nafanya hili.

Jinsi gani niliache Jina langu lichafuliwe?

Sitautoa utukufu wangu kwa mwingine.

Israeli Anawekwa Huru

1248:12 Isa 46:3; 41:4; Ufu 22:13; Isa 43:13; 42:6“Ee Yakobo, nisikilize mimi,

Israeli, ambaye nimekuita:

Mimi ndiye;

mimi ndimi mwanzo na mwisho.

1348:13 Ebr 1:10-12; Ay 9:8; Isa 34:16; 40:26; Kut 20:11; Isa 45:18Mkono wangu mwenyewe uliweka misingi ya dunia,

nao mkono wangu wa kuume umezitanda mbingu;

niziitapo, zote husimama pamoja.

1448:14 Isa 43:9; 46:10-11; 41:2, 22; Yer 50:45; Isa 21:9“Kusanyikeni, ninyi nyote, msikilize:

Ni ipi miongoni mwa hizo sanamu

ambayo imetabiri vitu hivi?

Watu wa Bwana waliochaguliwa na kuungana

watatimiza kusudi lake dhidi ya Babeli;

mkono wa Mungu utakuwa dhidi ya Wakaldayo.

1548:15 Amu 4:10; Isa 45:1Mimi, naam, Mimi, nimenena;

naam, nimemwita yeye.

Nitamleta,

naye atafanikiwa katika lile nililomtuma.

1648:16 Isa 45:19; Zek 2:8-11; Isa 33:13; 50:5-9; 11:2“Nikaribieni na msikilize hili:

“Tangu tangazo la kwanza sikusema kwa siri;

wakati litokeapo, nitakuwako hapo.”

Sasa Bwana Mwenyezi amenituma,

kwa Roho wake.

1748:17 Ay 19:25; Za 32:4; Isa 54:8; 47:4; 28:9; Yer 7:13; Isa 49:10Hili ndilo asemalo Bwana,

Mkombozi wako, yeye Aliye Mtakatifu wa Israeli:

“Mimi ni Bwana, Mungu wako,

nikufundishaye ili upate faida,

nikuongozaye katika njia ikupasayo kuiendea.

1848:18 Kum 5:29; Isa 42:23; Za 147:14; 45:8; Isa 54:13; 33:21; 45:5Laiti ungesikiliza kwa makini maagizo yangu,

amani yako ingekuwa kama mto,

haki yako kama mawimbi ya bahari.

1948:19 Mwa 22:17; Ay 5:25; Yer 35:19; Isa 43:5; 61:9; Mwa 12:2; Isa 56:5Wazao wako wangekuwa kama mchanga,

watoto wako kama chembe zake zisizohesabika;

kamwe jina lao lisingefutiliwa mbali,

wala kuangamizwa kutoka mbele zangu.”

2048:20 Zek 2:6-7; Ufu 18:4; Isa 12:6; Mik 4:10; Isa 52:11; Yer 48:6; 50:8Tokeni huko Babeli,

kimbieni kutoka kwa Wakaldayo!

Tangazeni hili kwa kelele za shangwe

na kulihubiri.

Lipelekeni mpaka miisho ya dunia;

semeni, “Bwana amemkomboa

mtumishi wake Yakobo.”

2148:21 Isa 41:17; 33:16; 30:25; Kut 17:6; Za 105:41; Hes 20:11Hawakuona kiu alipowaongoza kupita jangwani;

alifanya maji yatiririke kutoka kwenye mwamba kwa ajili yao;

akapasua mwamba

na maji yakatoka kwa nguvu.

2248:22 Isa 3:11; 57:21; Ay 3:26“Hakuna amani kwa waovu,” asema Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 48:1-22

Israeli ndi Nkhutukumve

1“Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,

inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,

ndinu a fuko la Yuda,

inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,

ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,

ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.

2Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika

ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,

amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:

3Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,

zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;

tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.

4Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve

wa nkhongo gwaa,

wa mutu wowuma.

5Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;

zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe

kuti unganene kuti,

‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,

kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’

6Inu munamva zinthu zimenezi.

Kodi inu simungazivomereze?

“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano

zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.

7Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;

munali musanazimve mpaka lero lino.

Choncho inu simunganene kuti,

‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’

8Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;

makutu anu sanali otsekuka.

Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti

chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.

9Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.

Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.

Sindidzakuwonongani kotheratu.

10Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;

ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.

11Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.

Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?

Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.

Kumasulidwa kwa Israeli

12“Tamvera Ine, iwe Yakobo,

Israeli, amene ndinakuyitana:

Mulungu uja Woyamba

ndi Wotsiriza ndine.

13Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,

dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.

Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba

ndi dziko lapansi.

14“Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:

Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?

Wokondedwa wa Yehova uja adzachita

zomwe Iye anakonzera Babuloni;

dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.

15Ine, Inetu, ndayankhula;

ndi kumuyitana

ndidzamubweretsa ndine

ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.

16“Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:

“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;

pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”

Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake

ndi kundituma.

17Yehova, Mpulumutsi wanu,

Woyerayo wa Israeli akuti,

“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,

ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.

18Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,

bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,

ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.

19Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,

ana ako akanachuluka ngati fumbi;

dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga

ndipo silikanafafanizidwa konse.”

20Tulukani mʼdziko la Babuloni!

Thawani dziko la Kaldeya!

Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo

ndipo muzilalikire

mpaka kumathero a dziko lapansi;

muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”

21Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;

anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;

anangʼamba thanthwelo ndipo

munatuluka madzi.

22“Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.