Isaya 42 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 42:1-25

Mtumishi Wa Bwana

142:1 Isa 49:3-6; 14:1; Yn 3:34; Lk 9:35; Mwa 49:10; Mt 3:16-17; 20:28“Huyu hapa mtumishi wangu, ninayemtegemeza,

mteule wangu, ambaye ninapendezwa naye;

nitaweka Roho yangu juu yake,

naye ataleta haki kwa mataifa.

242:2 Za 8:1-4Hatapaza sauti wala kupiga kelele,

wala hataiinua sauti yake barabarani.

342:3 Za 72:2; Mt 12:17-21; Za 96:13; Isa 36:6; Ay 30:24; 13:25Mwanzi uliopondeka hatauvunja,

na utambi unaofuka moshi hatauzima.

Kwa uaminifu ataleta haki,

442:4 Mwa 49:10; Ebr 12:2; Rum 8:22-25; Kut 34:29; Isa 51:4; 11:11hatazimia roho wala kukata tamaa,

mpaka atakaposimamisha haki juu ya dunia.

Visiwa vitaweka tumaini lao katika sheria yake.”

542:5 Za 24:2; Mdo 17:24-25; Isa 44:24; 48:13; Za 102:25Hili ndilo asemalo Mungu, Bwana,

yeye aliyeziumba mbingu na kuzitanda,

aliyeitandaza dunia na vyote vitokavyo humo,

awapaye watu wake pumzi,

na uzima kwa wale waendao humo:

642:6 Kut 31:2; Amu 4:10; Yer 23:6; Mdo 13:47; Dan 9:7; Isa 26:18; Lk 22:20“Mimi, Bwana, nimekuita katika haki;

nitakushika mkono wako.

Nitakulinda na kukufanya

kuwa Agano kwa ajili ya watu

na nuru kwa Mataifa,

742:7 Zek 9:11; 2:7; 2Tim 2:26; Lk 4:19; Mt 11:5; Isa 32:3; 51:14; Za 146:8kuwafungua macho wale wasioona,

kuwaacha huru kutoka kifungoni waliofungwa jela,

na kuwafungua kutoka gerezani

wale wanaokaa gizani.

842:8 Kut 3:14-15; 6:3; Isa 48:11; Za 81:10; Ebr 2:14-15; Kut 8:10; Isa 46:9“Mimi ndimi Bwana; hilo ndilo Jina langu!

Sitampa mwingine utukufu wangu

wala sanamu sifa zangu.

942:9 Isa 41:22; 40:21; Eze 2:4Tazama, mambo ya kwanza yametokea,

nami natangaza mambo mapya;

kabla hayajatokea

nawatangazia habari zake.”

Wimbo Wa Kumsifu Bwana

1042:10 Za 98:1; Kum 30:4; Za 96:11; 1Fal 10:9; 1Nya 16:32; Za 48:10; Isa 11:11Mwimbieni Bwana wimbo mpya,

sifa zake toka miisho ya dunia,

ninyi mshukao chini baharini,

na vyote vilivyomo ndani yake,

enyi visiwa na wote wakaao ndani yake.

1142:11 Mwa 25:13; Isa 32:16; 52:7; Nah 1:15; Isa 60:7; Amu 1:36Jangwa na miji yake na vipaze sauti zao;

makao anamoishi Kedari na yashangilie.

Watu wa Sela waimbe kwa furaha,

na wapige kelele kutoka vilele vya milima.

1242:12 Isa 24:15; 1Nya 16:24; 1Pet 2:9; Za 26:7; 66:2Wampe Bwana utukufu,

na kutangaza sifa zake katika visiwa.

1342:13 Isa 9:6; Yos 6:5; Yoe 3:16; Isa 66:14; 26:11; Kut 14:14; Hos 11:10Bwana ataenda kama mtu mwenye nguvu,

kama shujaa atachochea shauku yake,

kwa kelele ataamsha kilio cha vita,

naye atashinda adui zake.

1442:14 Es 4:14; Yer 4:31; Mwa 43:31; Lk 18:7“Kwa muda mrefu nimenyamaza kimya,

nimekaa kimya na kujizuia.

Lakini sasa, kama mwanamke wakati wa kujifungua,

ninapiga kelele, ninatweta na kushusha pumzi.

1542:15 Eze 38:20; Za 107:33; Isa 11:15; 50:2; Nah 1:4-6Nitaharibu milima na vilima

na kukausha mimea yako yote;

nitafanya mito kuwa visiwa

na kukausha mabwawa.

1642:16 Kum 4:31; Ebr 13:5; Yer 31:8-9; Isa 26:7; 29:24; 57:18; Mdo 26:18; Ebr 13:5Nitawaongoza vipofu kwenye njia ambayo hawajaijua,

kwenye mapito wasiyoyazoea nitawaongoza;

nitafanya giza kuwa nuru mbele yao,

na kufanya mahali palipoparuza kuwa laini.

Haya ndiyo mambo nitakayofanya;

mimi sitawaacha.

1742:17 Kut 32:4; Za 97:7; Isa 1:26Lakini wale wanaotumaini sanamu,

wanaoviambia vinyago, ‘Ninyi ndio miungu yetu,’

watarudishwa nyuma kwa aibu kubwa.

Israeli Kipofu Na Kiziwi

18“Sikieni, enyi viziwi;

tazameni, enyi vipofu, mpate kuona!

1942:19 Isa 43:8; Eze 12:2; Isa 41:8-9; Hag 1:13; Isa 26:3Ni nani aliye kipofu isipokuwa mtumishi wangu,

na kiziwi kama mjumbe ninayemtuma?

Ni nani aliye kipofu kama yeye aliyejitoa kwangu,

aliye kipofu kama mtumishi wa Bwana?

2042:20 Isa 6:9-10; Yer 5:21; Rum 2:21; Yer 6:10; Isa 48:21; 41:17Mmeona vitu vingi, lakini hamkuzingatia;

masikio yenu yako wazi, lakini hamsikii chochote.”

2142:21 2Kor 3:7; Isa 43:25Ilimpendeza Bwana

kwa ajili ya haki yake

kufanya sheria yake kuwa kuu na tukufu.

2242:22 Isa 24:18-22; Lk 19:41-44; Amu 6:4; 2Fal 24:13; Isa 5:29; Za 66:11; Yos 22:5; Isa 1:14; 30:11Lakini hili ni taifa lililoibwa na kutekwa nyara,

wote wamenaswa katika mashimo,

au wamefichwa katika magereza.

Wamekuwa nyara,

wala hapana yeyote awaokoaye.

Wamefanywa mateka,

wala hapana yeyote asemaye, “Warudishe.”

2342:23 Kum 32:29; Za 81:13; Isa 47:7; 48:18; 57:11Ni nani miongoni mwenu atakayesikiliza hili,

au atakayezingatia kwa makini katika wakati ujao?

2442:24 2Fal 17:6; Isa 43:28; 10:5-6Ni nani aliyemtoa Yakobo kuwa mateka,

na Israeli kwa wateka nyara?

Je, hakuwa yeye, Bwana,

ambaye tumetenda dhambi dhidi yake?

Kwa kuwa hawakufuata njia zake,

hawakutii sheria zake.

2542:25 Hos 7:9; Nah 1:6; 2Fal 22:13; Ay 40:11; Eze 7:19; 2Fal 25:9; Isa 29:13Hivyo akawamwagia hasira yake inayowaka,

ukali wa vita.

Iliwazunguka kwa miali ya moto, lakini hata hivyo hawakuelewa;

iliwateketeza, lakini hawakuyatia moyoni.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 42:1-25

Mtumiki wa Yehova

1“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza,

amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye.

Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo,

ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.

2Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu,

kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.

3Bango lophwanyika sadzalithyola,

ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa.

Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;

4sadzafowoka kapena kukhumudwa

mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi,

ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”

5Yehova Mulungu

amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika,

amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka,

amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo,

ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,

6“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama;

ndikugwira dzanja ndipo

ndidzakuteteza.

Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu

ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.

7Udzatsekula maso a anthu osaona,

udzamasula anthu a mʼndende

ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.

8“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo!

Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense

kapena matamando anga kwa mafano.

9Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi,

ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano;

zinthuzo zisanaonekere

Ine ndakudziwitsani.”

Nyimbo Yotamanda Yehova

10Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi,

inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo.

Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.

11Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo;

midzi ya Akedara ikondwere.

Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe;

afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.

12Atamande Yehova

ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.

13Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu,

adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo;

akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo

ndipo adzagonjetsa adani ake.

14Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali,

ndakhala ndili phee osachita kanthu.

Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira,

ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.

15Ndidzawononga mapiri ndi zitunda

ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse;

ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba

ndipo ndidzawumitsa maiwe.

16Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe,

ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo;

ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala

ndipo ndidzasalaza malo osalala.

Zimenezi ndizo ndidzachite;

sindidzawataya.

17Koma onse amene amadalira mafano

amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’

ndidzawachititsa manyazi kotheratu.

Aisraeli Alephera Kuphunzira

18“Imvani, agonthi inu;

yangʼanani osaona inu, kuti muone! 19Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi?

Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma?

Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano,

kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?

20Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale;

makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”

21Chinamukomera Yehova

chifukwa cha chilungamo chake,

kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.

22Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo,

onsewa anawakola mʼmaenje

kapena akuwabisa mʼndende.

Tsono asanduka chofunkha

popanda wina wowapulumutsa

kapena kunena kuti,

“Abwezeni kwawo.”

23Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi

kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?

24Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha,

ndi Israeli kwa anthu akuba?

Kodi si Yehova,

amene ife tamuchimwirayu?

Pakuti sanathe kutsatira njira zake;

ndipo sanamvere malangizo ake.

25Motero anawakwiyira kwambiri,

nawavutitsa ndi nkhondo.

Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse;

motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.