Isaya 17 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 17:1-14

Neno Dhidi Ya Dameski

117:1 Yer 49:23; Mdo 9:2; Kum 13:16; Zek 9:1; Mwa 14:15; Isa 25:2Neno kuhusu Dameski:

“Tazama, Dameski haitakuwa tena mji

bali itakuwa lundo la magofu.

217:2 Yer 7:33; Mik 4:4; Isa 5:17; 2Fal 10:33; Isa 7:21; 27:10; Eze 25:5; Law 26:6Miji ya Aroeri itaachwa

na itaachiwa mifugo ambayo italala huko,

bila yeyote wa kuyaogopesha.

317:3 Isa 7:8, 16; 21:16; Hos 9:11; Isa 8:4; Hos 10:14; Isa 25:2, 12Mji wenye ngome utatoweka kutoka Efraimu,

nao uweza wa ufalme kutoka Dameski;

mabaki ya Aramu yatakuwa

kama utukufu wa Waisraeli,”

asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

417:4 Isa 2:11; 10:16“Katika siku ile utukufu wa Yakobo utafifia,

unono wa mwili wake utadhoofika.

517:5 Yoe 3:13; Mt 13:30; Ufu 14:15-19; Isa 33:4; Yer 51:33; Ay 24:24; Yos 17:1517:5 Yos 17:15; 1Nya 11:15Itakuwa kama mvunaji akusanyavyo nafaka

na kuvuna nafaka kwa mikono yake,

kama wakati mtu aokotapo masazo ya masuke

katika Bonde la Warefai.

617:6 Kum 4:24; Isa 10:19; 27:12; 24:3Hata hivyo baadhi ya masazo yatabaki,

kama vile mti wa mzeituni unavyopigwa,

kukiachwa zeituni mbili au tatu juu ya matawi kileleni,

nne au tano katika matawi yazaayo sana,”

asema Bwana, Mungu wa Israeli.

717:7 Isa 9:13; 12:6; Zek 12:10; Mik 7:7; Isa 2:12; 10:20; Za 95:6Katika siku ile watu watamwangalia Muumba wao,

na kuelekeza macho yao kwa yule Aliye Mtakatifu wa Israeli.

817:8 2Nya 32:19; Ufu 9:20; 2Fal 17:10Hawataziangalia tena madhabahu,

kazi za mikono yao,

nao hawataheshimu nguzo za Ashera,17:8 Ashera hapa maana yake ni mungu mke aliyekuwa akiabudiwa pamoja na Baali.

na madhabahu za kufukizia uvumba zilizofanywa kwa mikono yao.

917:9 Isa 7:19Katika siku ile miji yao iliyo imara, ambayo waliihama kwa sababu ya Waisraeli, itakuwa kama mahali palipoachwa pa vichaka na magugu. Nayo yote itakuwa ukiwa.

1017:10 Eze 22:12; Hos 8:14; Za 68:19; Kum 6:12; Yer 2:32; Za 50:22Mmemsahau Mungu Mwokozi wenu,

hamkumkumbuka Mwamba aliye ngome yenu.

Kwa hiyo, hata ingawa mlipandikiza mimea iliyo mizuri sana

na kuotesha mizabibu ya kigeni,

1117:11 Za 90:6; Ay 4:8; Kum 28:39; Yer 10:19; 30:12; Law 26:30hata kama siku ile unapoipandikiza, unaifanya iote

na asubuhi ile ile unayoipanda, unaifanya ichipue,

hata hivyo mavuno yatakuwa kama si kitu

katika siku ile ya ugonjwa na maumivu yasiyoponyeka.

1217:12 Yer 6:23; Lk 21:25; Isa 41:11; Za 18:4; 46:6; Isa 8:7-9Lo! Ghadhabu ya mataifa mengi,

wanaghadhibika kama bahari iliyochafuka!

Lo! Makelele ya mataifa

wanavuma kama ngurumo za maji mengi!

1317:13 Kum 28:20; Isa 13:14; Ay 13:25; Dan 2:35; Za 65:7; 46:3; Ay 21:18Ingawa mataifa yanavuma kama ngurumo za maji yanayofanya mawimbi,

wakati anapoyakemea yanakimbia mbali,

yanafukuzwa mbele ya upepo kama makapi juu ya milima,

kama jani livingirishwapo na dhoruba.

1417:14 2Fal 19:35; Amu 5:31; Isa 29:5; 30:13; 33:18; 54:14Wakati wa jioni, hofu ya ghafula!

Kabla ya asubuhi, wametoweka!

Hili ndilo fungu la wale wanaotupora,

fungu la wale wanaotunyangʼanya mali zetu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.