Isaya 16 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 16:1-14

Hali Ya Kukata Tamaa Ya Moabu

116:1 Isa 10:32; Amu 1:36; 2Fal 14:7; 2Nya 32:23; 2Fal 3:4; Oba 1:3Pelekeni wana-kondoo kama ushuru

kwa mtawala wa nchi,

Kutoka Sela, kupitia jangwani,

hadi mlima wa Binti Sayuni.

216:2 Mit 27:8; Hes 21:13-14; Yer 48:40; Hes 21:29Kama ndege wanaopapatika

waliofukuzwa kutoka kwenye kiota,

ndivyo walivyo wanawake wa Moabu

kwenye vivuko vya Arnoni.

316:3 1Fal 18:4“Tupeni shauri,

toeni uamuzi.

Wakati wa adhuhuri,

fanyeni kivuli chenu kama usiku.

Waficheni watoro,

msisaliti wakimbizi.

416:4 Isa 55:7; 9:4; 2:2-4Waacheni watoro wa Moabu wakae pamoja nanyi;

kuweni mahali pao pa salama ili kuepuka mharabu.”

Mtesi atafikia mwisho na maangamizi yatakoma,

aletaye vita atatoweka kutoka nchi.

516:5 1Sam 13:14; Mik 4:7; Isa 7:2; Dan 7:14; Mit 20:28; Isa 9:7; Lk 1:32Kwa upendo kiti cha enzi kitaimarishwa,

kwa uaminifu mtu ataketi juu yake,

yeye atokaye nyumba ya Daudi:

yeye ambaye katika kuhukumu hutafuta haki,

na huhimiza njia ya haki.

616:6 Eze 25:8; Yer 25:21; Law 26:19; Ay 20:6; Sef 2:8; Yer 49:16; Amo 2:1Tumesikia juu ya kiburi cha Moabu:

kiburi chake cha kujivuna na udanganyifu,

kiburi chake na ufidhuli wake,

lakini majivuno yake si kitu.

716:7 1Nya 16:3; 2Fal 3:25; Yer 48:20; 49:3; Isa 13:6Kwa hiyo Wamoabu wanaomboleza,

wanaiombolezea Moabu kwa pamoja.

Wanaomboleza na kuhuzunika

kwa ajili ya watu wa Kir-Haresethi.

816:8 Ay 8:16; Hes 21:32; 21:25; Isa 15:6; 5:2; Ay 8:16; Za 80:11Mashamba ya Heshboni yananyauka,

pia na mizabibu ya Sibma.

Watawala wa mataifa

wamekanyaga mizabibu iliyo mizuri sana,

ambayo ilipata kufika Yazeri

na kuenea kuelekea jangwani.

Machipukizi yake yalienea

yakafika hadi baharini.

916:9 Isa 15:3; Eze 27:31; Yer 40:12; Ay 7:3; Hes 32:3; Ezr 3:13Hivyo ninalia kama Yazeri aliavyo,

kwa ajili ya mizabibu ya Sibma.

Ee Heshboni, ee Eleale,

ninakulowesha kwa machozi!

Kelele za furaha kwa ajili ya tunda lako lililoiva

na kwa ajili ya mavuno zimekomeshwa.

1016:10 Isa 24:7-8; Amu 9:27; Ay 24:11; Yer 25:30; Isa 5:2Furaha na shangwe zimeondolewa

kutoka mashamba ya matunda;

hakuna yeyote aimbaye wala apazaye sauti

katika mashamba ya mizabibu;

hakuna yeyote akanyagaye zabibu shinikizoni,

kwa kuwa nimekomesha makelele.

1116:11 Isa 15:5; Hos 11:8; Flp 2:1; Ay 30:31; Isa 63:15Moyo wangu unaomboleza kwa ajili ya Moabu kama kinubi,

nafsi yangu yote kwa ajili ya Kir-Haresethi.

1216:12 Za 115:4-7; 1Kor 8:4; Hes 22:4; Isa 15:2; 1Fal 11:7; 18:29Wakati Moabu anapojitokeza mahali pake pa juu,

anajichosha mwenyewe tu;

anapokwenda mahali pake pa kuabudia miungu ili kuomba,

haitamfaidi lolote.

13Hili ndilo neno ambalo Bwana ameshasema kuhusu Moabu. 1416:14 Isa 25:10; Yer 48:42; Kum 15:18; 13:16; Isa 20:3; 37:30; Law 19:13Lakini sasa Bwana anasema: “Katika miaka mitatu, kama vile mtumishi aliyefungwa na mkataba angeihesabu, fahari ya Moabu na watu wake wengi watadharauliwa, nao walionusurika watakuwa wachache sana, tena wanyonge.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 16:1-14

1Anthu a ku Mowabu

atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa,

kuchokera ku Sela kudutsa chipululu

mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.

2Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku

akazimwaza mʼchisa,

momwemonso akazi a ku Mowabu

akuyendayenda ku madooko a Arinoni.

3Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti,

“Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite.

Inu mutiteteze kwa adani anthu.

Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo.

Mutibise,

musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.

4Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu;

mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.”

Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso,

kuwononga kudzaleka;

waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.

5Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi;

mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika.

Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo

ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.

6Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri.

Kunyada kwawo

ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo,

zonse ndi zopanda phindu.

7Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri;

iwo akulirira dziko lawo.

Akubuma momvetsa chisoni

chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.

8Minda ya ku Hesiboni yauma,

minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga.

Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda

minda ya mpesa wabwino,

imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri,

mpaka kutambalalira ku chipululu.

Mizu yake inakafika

mpaka ku tsidya la nyanja.

9Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri,

chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima.

Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali,

ndikukunyowetsani ndi misozi!

Mwalephera kupeza zokolola,

chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.

10Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso;

palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa;

palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa,

pakuti ndathetsa kufuwula.

11Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu,

mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.

12Ngakhale anthu a ku Mowabu

apite ku malo awo achipembedzo

koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe

chifukwa sizidzatheka.

13Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu. 14Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”