Isaya 14 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Isaya 14:1-32

Yuda Kufanywa Upya

114:1 Isa 54:7-8; Zek 10:6; Mwa 18:19; Eze 47:22; Efe 2:12-19; Kut 12:43; Eze 47:22; Zek 8:22-23; Isa 11:10; Yer 3:18; Zek 2:12Bwana atamhurumia Yakobo,

atamchagua Israeli tena,

na kuwakalisha katika nchi yao wenyewe.

Wageni wataungana nao

na kujiunga na nyumba ya Yakobo.

214:2 Isa 11:12; 26:15; 49:7; 49:23; 54:3; 60:9; Sef 3:19; Zek 2:9; Za 49:14Mataifa watawachukua

na kuwaleta mahali pao wenyewe.

Nayo nyumba ya Israeli itamiliki mataifa

kama watumishi na wajakazi katika nchi ya Bwana.

Watawafanya watekaji wao kuwa mateka,

na kutawala juu ya wale waliowaonea.

314:3 Isa 11:10-12; Ay 3:17; Kut 1:14Katika siku Bwana atakapokuondolea mateso, udhia na utumwa wa kikatili, 414:4 Hab 2:6; Mik 2:4; Isa 13:19; 9:4utaichukua dhihaka hii dhidi ya mfalme wa Babeli:

Tazama jinsi mtesi alivyofikia mwisho!

Tazama jinsi ghadhabu yake kali ilivyokoma!

514:5 Isa 10:15; Za 125:3; 110:2Bwana amevunja fimbo ya mwovu,

fimbo ya utawala ya watawala,

614:6 2Fal 15:29; Isa 10:14; Za 47:3; Isa 47:6ambayo kwa hasira waliyapiga mataifa

kwa mapigo yasiyo na kikomo,

nao kwa ghadhabu kali waliwatiisha mataifa

kwa jeuri pasipo huruma.

714:7 Za 126:1-3; Hes 6:26; Yer 50:34; Zek 1:11Nchi zote ziko kwenye mapumziko na kwenye amani,

wanabubujika kwa kuimba.

814:8 1Nya 16:33; Za 65:13; Eze 31:16; 2Fal 19:23; Isa 37:24Hata misunobari na mierezi ya Lebanoni

inashangilia mbele yako na kusema,

“Basi kwa sababu umeangushwa chini,

hakuna mkata miti atakayekuja kutukata.”

914:9 Mit 30:16; Eze 32:21; Ay 26:5; Zek 10:3; Ay 3:14Kuzimu kote kumetaharuki

kukulaki unapokuja,

kunaamsha roho za waliokufa ili kukupokea,

wote waliokuwa viongozi katika ulimwengu,

kunawafanya wainuke kwenye viti vyao vya kifalme:

wale wote waliokuwa wafalme juu ya mataifa.

1014:10 Eze 26:20; 32:21Wote wataitikia,

watakuambia,

“Wewe pia umekuwa dhaifu, kama sisi tulivyo;

wewe umekuwa kama sisi.”

1114:11 Ay 7:5; 24:20; Hes 16:30; Mit 30:16; Isa 5:12; Eze 26:13; Amo 6:5; Ay 21:26Majivuno yako yote yameshushwa mpaka kuzimu,

pamoja na kelele ya vinubi vyako,

mafunza yametanda chini yako,

na minyoo imekufunika.

1214:12 Isa 34:4; 2Pet 1:19; Ufu 2:28; Lk 10:18; Eze 26:17; Ufu 2:28Tazama jinsi ulivyoanguka kutoka mbinguni,

ewe nyota ya asubuhi, mwana wa mapambazuko!

Umetupwa chini duniani,

wewe uliyepata kuangusha mataifa!

1314:13 Mt 11:23; Eze 28:2; 2The 2:4; Dan 8:10; 5:23; Isa 37:24Ulisema moyoni mwako,

“Nitapanda juu hadi mbinguni,

nitakiinua kiti changu cha enzi

juu ya nyota za Mungu,

nitaketi nimetawazwa

juu ya mlima wa kusanyiko,

kwenye vimo vya juu sana vya Mlima Mtakatifu.

1414:14 Hes 24:16; 2The 2:4; Ay 20:6; Isa 47:8; Yer 50:29; Dan 11:38; Isa 10:13Nitapaa juu kupita mawingu,

nitajifanya kama Yeye Aliye Juu Sana.”

1514:15 Mt 11:23; Lk 10:15; Mdo 12:23; Isa 13:6; 47:11; Ay 21:13; Eze 31:16Lakini umeshushwa chini hadi kuzimu,

hadi kwenye vina vya shimo.

1614:16 Yer 50:23; Ufu 18:18; Isa 2:19; 13:13; Yoe 3:16Wale wanaokuona wanakukazia macho,

wanatafakari hatima yako:

“Je, huyu ndiye yule aliyetikisa dunia

na kufanya falme zitetemeke,

1714:17 Isa 15:6; Za 52:7; 2Fal 15:29; Kut 7:14; Yer 50:33; Ufu 18:18yule aliyeifanya dunia kuwa jangwa,

aliyeipindua miji yake,

na ambaye hakuwaachia mateka wake

waende nyumbani?”

1814:18 Ay 21:32Wafalme wote wa mataifa wamelala kwa heshima

kila mmoja katika kaburi lake.

1914:19 Isa 22:16-18; Yer 36:30; Isa 34:3; 13:15; Yer 8:1; 41:7-9Lakini wewe umetupwa nje ya kaburi lako

kama tawi lililokataliwa,

umefunikwa na waliouawa

pamoja na wale waliochomwa kwa upanga,

wale washukao mpaka

kwenye mawe ya shimo.

Kama mzoga uliokanyagwa chini ya nyayo,

2014:20 Ay 18:19; Kum 32:16; Za 21:10; 1Fal 21:19Hutajumuika nao kwenye mazishi,

kwa kuwa umeharibu nchi yako

na kuwaua watu wako.

Mzao wa mwovu

hatatajwa tena kamwe.

2114:21 Mwa 9:25; Kut 20:5; Hes 16:27; Law 26:39Andaa mahali pa kuwachinjia wanawe

kwa ajili ya dhambi za baba zao,

wasije wakainuka ili kuirithi nchi

na kuijaza dunia kwa miji yao.

2214:22 2Sam 18:18; 1Fal 14:10; Za 94:16; Ay 18:17-19; Isa 13:18; Za 109:13Bwana Mwenye Nguvu Zote asema,

“Nitainuka dhidi yao,

nitalikatilia mbali jina lake kutoka Babeli pamoja na watu wake walionusurika,

watoto wake na wazao wake,”

asema Bwana.

2314:23 Law 11:16-18; Sef 2:14; Isa 34:11-15; Yer 25:12; 50:3; 51:62“Nitaifanya kuwa mahali pa bundi,

na kuwa nchi ya matope;

nitaifagia kwa ufagio wa maangamizi,”

asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

Unabii Dhidi Ya Ashuru

2414:24 Isa 62:8; Eze 12:25; Mdo 4:28; Isa 45:23; 23:8-9; Dan 4:35; Isa 46:10-11Bwana Mwenye Nguvu Zote ameapa,

“Hakika, kama vile nilivyopanga, ndivyo itakavyokuwa,

nami kama nilivyokusudia, ndivyo itakavyosimama.

2514:25 Isa 37:36-37; 10:27; 9:4Nitamponda Mwashuru katika nchi yangu,

juu ya milima yangu nitawakanyagia chini.

Nira yake itaondolewa kutoka kwa watu wangu,

nao mzigo wake utaondolewa kutoka mabegani mwao.”

2614:26 Kut 15:12; Ay 30:21; Isa 23:9Huu ndio mpango uliokusudiwa kwa ajili ya ulimwengu wote,

huu ni mkono ulionyooshwa juu ya mataifa yote.

2714:27 2Nya 20:6; Ay 40:8; Dan 4:35; Yer 49:20; Kut 14:21Kwa kuwa Bwana Mwenye Nguvu Zote amekusudia,

ni nani awezaye kumzuia?

Mkono wake umenyooshwa,

ni nani awezaye kuurudisha?

Unabii Dhidi Ya Wafilisti

28Neno hili lilikuja mwaka ule Mfalme Ahazi alipofariki:

2914:29 Yos 13:3; Isa 11:8; Kum 8:15; 2Nya 26:6Msifurahi, enyi Wafilisti wote,

kwamba fimbo iliyowapiga imevunjika;

kutoka mzizi wa huyo nyoka

atachipuka nyoka mwenye sumu kali,

uzao wake utakuwa joka lirukalo,

lenye sumu kali.

3014:30 Isa 3:15; 25:4; 7:21-22; 8:21; 9:20; Sef 2:5Maskini kuliko maskini wote watapata malisho,

nao wahitaji watalala salama.

Lakini mzizi wako nitauangamiza kwa njaa,

nayo njaa itawaua walionusurika.

3114:31 Isa 3:26; Yer 47:2; Eze 32:30; Isa 13:6; 41:25; Mwa 10:14; Yer 13:20; 46:20-24Piga yowe, ee lango! Bweka, ee mji!

Yeyukeni, enyi Wafilisti wote!

Wingu la moshi linakuja toka kaskazini,

wala hakuna atakayechelewa katika safu zake.

3214:32 Za 51:18; Isa 37:9; Yak 2:5; Za 87:2; Isa 28:16; 44:28; 4:6Ni jibu gani litakalotolewa

kwa wajumbe wa taifa hilo?

Bwana ameifanya imara Sayuni,

nako ndani yake watu wake walioonewa watapata kimbilio.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 14:1-32

1Yehova adzachitira chifundo Yakobo;

adzasankhanso Israeli

ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo.

Alendo adzabwera kudzakhala nawo

ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.

2Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli

ku dziko lawo.

Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja

kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova.

Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo.

Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.

3Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani, 4mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti,

Wopsinja uja watha!

Ukali wake uja watha!

5Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa,

Iye waphwanya ndodo ya olamulira.

6Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali

powamenya kosalekeza,

Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali

ndikuwazunza kosalekeza.

7Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere;

ndipo akuyimba mokondwa.

8Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni

ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti,

“Chigwetsedwere chako pansi,

palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”

9Ku manda kwatekeseka

kuti akulandire ukamabwera;

mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri

a dziko lapansi, yadzutsidwa.

Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu

ayimiritsidwa pa mipando yawo.

10Onse adzayankha;

adzanena kwa iwe kuti,

“Iwenso watheratu mphamvu ngati ife;

Iwe wafanana ndi ife.”

11Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda,

pamodzi ndi nyimbo za azeze ako;

mphutsi zayalana pogona pako

ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi.

12Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba,

iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha!

Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi,

Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!

13Mu mtima mwako unkanena kuti,

“Ndidzakwera mpaka kumwamba;

ndidzakhazika mpando wanga waufumu

pamwamba pa nyenyezi za Mulungu;

ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako,

pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.

14Ndidzakwera pamwamba pa mitambo;

ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”

15Koma watsitsidwa mʼmanda

pansi penipeni pa dzenje.

16Anthu akufa adzakupenyetsetsa

nadzamalingalira za iwe nʼkumati,

“Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi

ndi kunjenjemeretsa maufumu,

17munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu,

amene anagwetsa mizinda yake

ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”

18Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu

aliyense mʼmanda akeake.

19Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako,

ngati nthambi yowola ndi yonyansa.

Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa;

amene anabayidwa ndi lupanga,

anatsikira mʼdzenje lamiyala

ngati mtembo woponderezedwa.

20Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu,

chifukwa unawononga dziko lako

ndi kupha anthu ako.

Zidzukulu za anthu oyipa

sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.

21Konzani malo woti muphere ana ake aamuna

chifukwa cha machimo a makolo awo;

kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi

ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.

22Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni.

Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo.

Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,”

akutero Yehova.

23“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu

ndiponso dambo lamatope;

ndidzawusesa ndi tsache lowononga,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Za Kulangidwa kwa Asiriya

24Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti,

“Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho,

ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.

25Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa;

ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga;

ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga,

ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”

26Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi,

ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.

27Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse?

Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?

Za Kulangidwa kwa Afilisti

28Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:

29Musakondwere inu Afilisti nonse

kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa;

chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri,

ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.

30Osaukitsitsa adzapeza chakudya

ndipo amphawi adzakhala mwamtendere.

Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala,

ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.

31Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda!

Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse!

Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto,

ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.

32Kodi tidzawayankha chiyani

amithenga a ku Filisitiya?

“Yehova wakhazikitsa Ziyoni,

ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”