Hesabu 34 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Hesabu 34:1-29

Mipaka Ya Kanaani

1Bwana akamwambia Mose, 234:2 Hes 33:51; Mwa 17:8; Kum 1:7-8; Yos 23:4; Za 78:54-55; 105:11; Eze 47:15“Waamuru Waisraeli na uwaambie: ‘Mtakapoingia nchi ya Kanaani, nchi ambayo itagawanywa kwenu kama urithi itakuwa na mipaka ifuatayo:

334:3 Hes 15:21; Yos 15:1-3; Mwa 14:3; Eze 47:13; Mwa 14:3; Yos 3:16“ ‘Upande wenu wa kusini utajumuisha sehemu ya Jangwa la Sini kufuata mpaka wa Edomu. Upande wa mashariki mpaka wenu wa kusini utaanzia mwisho wa Bahari ya Chumvi,34:3 Yaani Bahari Mfu. 434:4 Yos 15:3; Amu 1:36; Hes 32:8; Yos 15:4katiza kusini mwa Pito la Akrabimu, endelea mpaka Sini na kwenda kusini ya Kadesh-Barnea. Kisha mpaka huo utaenda hadi Hasar-Adari hadi Azmoni, 534:5 Mwa 15:18; 1Fal 8:65; Isa 27:12mahali ambapo utapinda, na kuunganika na Kijito cha Misri na kumalizikia kwenye Bahari ya Kati.34:5 Yaani Mediterania.

634:6 Yos 1:4; 9:1; 15:12; 23:4; Eze 47:10; 48:28; 47:9-20“ ‘Mpaka wenu wa magharibi utakuwa Bahari ya Kati. Huu utakuwa mpaka wenu upande wa magharibi.

734:7 Eze 47:15-17; Hes 20:22“ ‘Kwa mpaka wenu wa kaskazini, wekeni alama kuanzia Bahari ya Kati hadi mlima Hori, 834:8 Hes 13:21; Yos 13:5; 2Sam 8:9; 2Fal 18:25; Isa 10:9; Yer 39:5; Eze 47:15-20na kutoka mlima Hori hadi Pito la Hamathi. Kisha mpaka utaenda hadi Sedadi, 934:9 Eze 47:17kuendelea hadi Zifroni, na kuishia Hasar-Enani. Huu utakuwa mpaka wenu upande wa kaskazini.

1034:10 Yos 15:5“ ‘Kwa mpaka wenu wa mashariki, wekeni alama kuanzia Hasar-Enani hadi Shefamu. 1134:11 2Fal 23:33; 25:6; Yer 39:5; 52:9; Yos 15:32; 21:16; 1Nya 4:32; Kum 3:17; Yos 11:2; 13:27Mpaka utaelekea kusini kuanzia Shefamu hadi Ribla upande wa mashariki wa Aini, na kuendelea kwenye miteremko mashariki mwa Bahari ya Kinerethi.34:11 Yaani Bahari ya Galilaya. 12Kisha mpaka utashuka kuelekea Mto Yordani na kuishia katika Bahari ya Chumvi.

“ ‘Hii itakuwa nchi yenu, ikiwa na mipaka yake kila upande.’ ”

1334:13 Law 16:8; Yos 18:10; Mik 2:5; Yos 13:6; 14:1-5; Isa 49:8Mose akawaamuru Waisraeli: “Gawanyeni nchi hii kwa kura kama urithi. Bwana ameagiza kwamba itolewe kwa yale makabila tisa na nusu, 1434:14 Hes 32:19; Kum 33:21; Yos 14:3kwa sababu jamaa ya kabila la Reubeni, kabila la Gadi, na nusu ya kabila la Manase wamekwishapokea urithi wao. 15Haya makabila mawili na nusu wamekwishapokea urithi wao upande wa mashariki wa Yordani ngʼambo ya Yeriko, kuelekea mawio ya jua.”

16Bwana akamwambia Mose, 1734:17 Hes 11:28; Kum 1:38; Kut 6:23-25“Haya ndiyo majina ya watu ambao watakusaidia kugawanya nchi kama urithi: Eleazari kuhani na Yoshua mwana wa Nuni. 1834:18 Hes 1:4; Yos 14:1Tena uteue kiongozi mmoja kutoka kila kabila kusaidia kuigawanya nchi. 1934:19 Hes 26:65; Mwa 29:35; Kum 33:7; Za 60:7; 108:8; Hes 13:6, 30; Kum 1:36Haya ndiyo majina yao:

“Kalebu mwana wa Yefune,

kutoka kabila la Yuda;

2034:20 Mwa 29:33; 49:5; Eze 48:24Shemueli mwana wa Amihudi,

kutoka kabila la Simeoni;

2134:21 Mwa 49:27; Amu 5:14; Za 68:27Elidadi mwana wa Kisloni,

kutoka kabila la Benyamini;

22Buki mwana wa Yogli,

kiongozi kutoka kabila la Dani;

2334:23 Hes 1:34; Mwa 48:8-22; Kum 33:13; Mwa 49:22; Za 80:1Hanieli mwana wa Efodi,

kiongozi kutoka kabila la Manase mwana wa Yosefu;

2434:24 Hes 1:32Kemueli mwana wa Shiftani,

kiongozi kutoka kabila la Efraimu mwana wa Yosefu;

2534:25 Mwa 30:20Elisafani mwana wa Parnaki,

kiongozi kutoka kabila la Zabuloni;

26Paltieli mwana wa Azani,

kiongozi kutoka kabila la Isakari;

2734:27 Hes 1:40Ahihudi mwana wa Shelomi,

kiongozi kutoka kabila la Asheri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

kiongozi kutoka kabila la Naftali.”

2934:29 Kum 32:8; Mdo 17:26Hawa ndio watu ambao Bwana aliamuru wagawanye urithi kwa Waisraeli katika nchi ya Kanaani.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 34:1-29

Malire a Dziko la Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:

3“ ‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere. 4Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni, 5kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.

6“ ‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.

7“ ‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori 8ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi, 9ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.

10“ ‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu. 11Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti. 12Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere.

“ ‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’ ”

13Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka, 14chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo. 15Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni. 18Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo. 19Mayina awo ndi awa:

Kalebe mwana wa Yefune,

wochokera ku fuko la Yuda,

20Semueli mwana wa Amihudi,

wochokera ku fuko la Simeoni;

21Elidadi mwana wa Kisiloni,

wochokera ku fuko la Benjamini;

22Buki mwana wa Yogili,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;

23Hanieli mwana wa Efodi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;

24Kemueli mwana wa Sifitani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.

25Elizafani mwana wa Parinaki,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;

26Palitieli mwana wa Azani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,

27Ahihudi mwana wa Selomi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”

29Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.