Maombolezo Kwa Ajili Ya Misri
1Neno la Bwana likanijia kusema: 230:2 Isa 13:6; Yak 5:1“Mwanadamu, toa unabii na useme: ‘Hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo:
“ ‘Ombolezeni ninyi na mseme,
“Ole wa siku ile!”
330:3 Oba 1:15; Yoe 2:11; Eze 32:7; 34:12; 7:7; Yoe 1:15Kwa kuwa siku ile imekaribia,
siku ya Bwana imekaribia,
siku ya mawingu,
siku ya maangamizi kwa mataifa.
430:4 Eze 29:19; Yer 50:15; 25:19; Dan 11:43; Mwa 10:6; Eze 29:10Upanga utakuja dhidi ya Misri,
nayo maumivu makuu yataijia Ethiopia.
Mauaji yatakapoangukia Misri,
utajiri wake utachukuliwa
na misingi yake itabomolewa.
530:5 Eze 27:10; Yer 25:20; 2Nya 9:14; Nah 3:9Kushi30:5 Kushi ndiyo Ethiopia. na Putu, Ludi na Arabia yote, Libya30:5 Libya ndiyo Kubu. na watu wa nchi ya Agano watauawa kwa upanga pamoja na Misri.
630:6 Eze 29:10“ ‘Hili ndilo Bwana asemalo:
“ ‘Wale walioungana na Misri wataanguka
na kiburi cha nguvu zake kitashindwa.
Kutoka Migdoli hadi Aswani,
watauawa ndani yake kwa upanga,
asema Bwana Mwenyezi.
730:7 Eze 29:12“ ‘Hizo nchi zitakua ukiwa
miongoni mwa nchi zilizo ukiwa,
nayo miji yao itakuwa magofu
miongoni mwa miji iliyo magofu.
830:8 Yer 49:27; Eze 39:6; Nah 1:6; Eze 29:9Ndipo watakapojua kwamba mimi ndimi Bwana,
nitakapoiwasha Misri moto
na wote wamsaidiao watapondwa.
930:9 Kum 31:6; Mt 10:28; Eze 24:3; 44:630:9 Mwa 10:6; Isa 18:1-2; 23:5; Eze 32:9-10; Sef 2:12“ ‘Siku hiyo wajumbe watatoka kwangu kwa merikebu, ili kuwatia hofu Ethiopia, wakiwa katika hali yao ya kuridhika. Maumivu makali yatawapata siku ya maangamizi ya Misri, kwa kuwa hakika itakuja.
1030:10 Yer 39:1; Eze 29:19“ ‘Hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo:
“ ‘Nitakomesha makundi ya wajeuri ya Misri
kwa mkono wa Nebukadneza mfalme wa Babeli.
1130:11 Eze 28:7; 29:19Yeye na jeshi lake, taifa lililo katili kuliko mataifa yote,
litaletwa ili kuangamiza nchi.
Watafuta panga zao dhidi ya Misri
na kuijaza nchi kwa waliouawa.
1230:12 Isa 19:6; Yer 46:8; Eze 29:9; 19:7Nitakausha vijito vya Naili
na nitaiuza nchi kwa watu waovu,
kwa mkono wa wageni,
nitaifanya nchi ukiwa na kila kitu
kilichomo ndani yake.
Mimi Bwana nimenena haya.
1330:13 Yer 43:12; Isa 19:13; Eze 6:6; Zek 10:11“ ‘Hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo:
“ ‘Nitaangamiza sanamu
na kukomesha vinyago katika Memfisi30:13 Kiebrania ni Nofu.
Hapatakuwepo tena na mkuu katika nchi ya Misri,
nami nitaeneza hofu katika nchi nzima.
1430:14 Eze 29:14; Hes 13:22; Za 78:12; Yer 46:25Nitaifanya Pathrosi30:14 Pathrosi ni Misri ya Juu. kuwa ukiwa
na kuitia moto Soani,
nami nitaipiga kwa adhabu Thebesi30:14 Thebesi kwa Kiebrania ni No (au No-Amoni), mji katika Misri.
15Nitaimwaga ghadhabu yangu juu ya Pelusiumu,30:15 Kiebrania ni Sini.
ngome ya Misri,
nami nitakatilia mbali
makundi ya wajeuri wa Thebesi.
1630:16 Yos 7:15; Isa 19:13Nitaitia moto nchi ya Misri;
Pelusiumu itagaagaa kwa maumivu makuu.
Thebesi itachukuliwa na tufani,
Memfisi itakuwa katika taabu daima.
1730:17 Mwa 41:45Wanaume vijana wa Oni30:17 Yaani Heliopoli (Mji wa Jua). na wa Pi-Besethi30:17 Yaani Bubasti.
wataanguka kwa upanga
nayo hiyo miji itatekwa.
1830:18 Law 26:13; Isa 9:4; Yer 2:16; 43:7Huko Tahpanhesi mchana utatiwa giza
nitakapovunja kongwa la Misri;
hapo kiburi cha nguvu zake kitakoma.
Atafunikwa na mawingu
na vijiji vyake vitatekwa.
1930:19 Eze 28:22Kwa hiyo nitaipiga Misri kwa adhabu,
nao watajua kuwa Mimi ndimi Bwana.’ ”
2030:20 Eze 26:1; 29:17; 32:1Katika mwaka wa kumi na moja, mwezi wa kwanza, siku ya saba, neno la Bwana likanijia kusema: 2130:21 Yer 48:25; 44:30; 30:13; 46:11“Mwanadamu, nimevunja mkono wa Farao mfalme wa Misri. Haukufungwa ili upone au kuwekewa kipande cha ubao ili upate nguvu za kuweza kuchukua upanga. 2230:22 Mwa 15:18; Yer 46:25; Za 37:17; Zek 11:17Kwa hiyo hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo: Mimi ni kinyume na Farao mfalme wa Misri. Nitavunja mikono yake yote miwili, ule mkono ulio mzima pia na ule uliovunjika na kuufanya upanga uanguke toka mkononi mwake. 2330:23 Eze 29:12Nitawatawanya Wamisri miongoni mwa mataifa na kuwafukuza huku na huko katika nchi zote. 2430:24 Zek 10:6-12; 12:5; Eze 21:14; Sef 2:12; Yer 51:52Nitaitia nguvu mikono ya mfalme wa Babeli na kuutia upanga wangu mkononi mwake, lakini nitavunja mikono ya Farao, naye atalia kwa huzuni mbele yake kama mtu aliyetiwa jeraha la kumfisha. 2530:25 Kut 7:5; Za 9:16; 59:13; 1Nya 21:12; Isa 10:5; Eze 29:19Nitaitia nguvu mikono ya mfalme wa Babeli, lakini mikono ya Farao italegea. Ndipo watakapojua kwamba Mimi ndimi Bwana, nitakapoutia upanga wangu mkononi mwa mfalme wa Babeli, naye ataunyoosha dhidi ya Misri. 2630:26 Eze 29:12Nitawatawanya Wamisri miongoni mwa mataifa na kuwafukuza huku na huko katika nchi mbalimbali. Ndipo watakapojua kwamba Mimi ndimi Bwana.”
Za Kulangidwa kwa Igupto
1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,
‘Kalanga, tsiku lafika!’
3Pakuti tsiku layandikira,
tsiku la Yehova lili pafupi,
tsiku la mitambo yakuda,
tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto
ndipo mavuto adzafika pa Kusi.
Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,
chuma chake chidzatengedwa
ndipo maziko ake adzagumuka.
5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:
“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa
ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.
Adzaphedwa ndi lupanga
kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”
ndikutero Ine Ambuye Yehova.
7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja
kupambana mabwinja ena onse opasuka,
ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka
kupambana mizinda ina yonse.
8Nditatha kutentha Igupto
ndi kupha onse omuthandiza,
pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni
kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja
adzabwera kudzawononga dzikolo.
Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto
ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo
ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.
Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo
pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.
Ine Yehova ndayankhula.
13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Ndidzawononga mafano
ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.
Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,
ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,
ndi kutentha mzinda wa Zowani.
Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,
linga lolimba la Igupto,
ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;
Peluziumu adzazunzika ndi ululu.
Malinga a Thebesi adzagumuka,
ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti
adzaphedwa ndi lupanga
ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima
pamene ndidzathyola goli la Igupto;
motero kunyada kwake kudzatha.
Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,
ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,
ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”
Farao Watha Mphamvu
20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”