Ezekieli 21 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ezekieli 21:1-32

Babeli, Upanga Wa Mungu Wa Hukumu

121:1 Eze 20:1Neno la Bwana likanijia kusema: 221:2 Yer 11:12; Eze 20:46; Amo 7:16; Eze 9:6; 13:17“Mwanadamu, uelekeze uso wako juu ya Yerusalemu na uhubiri dhidi ya mahali patakatifu. Tabiri dhidi ya nchi ya Israeli 321:3 Yer 21:13; 47:6-7; Ay 9:22; Isa 27:1; Eze 14:21uiambie: ‘Hili ndilo Bwana asemalo: Mimi niko kinyume nawe. Nitautoa upanga wangu kwenye ala yake na kumkatilia mbali mwenye haki na mwovu. 421:4 Eze 20:47; Law 26:25; Yer 25:27Kwa sababu nitamkatilia mbali mwenye haki na mwovu, upanga wangu utakuwa wazi dhidi ya kila mmoja kuanzia kusini mpaka kaskazini. 521:5 Eze 20:47-48; Isa 45:23; 34:5Ndipo watu wote watajua ya kuwa Mimi Bwana nimeutoa upanga wangu kwenye ala yake, nao hautarudi humo tena.’

621:6 Isa 22:4; Yer 30:6; Eze 9:4“Kwa hiyo lia kwa uchungu, mwanadamu! Lia kwa uchungu mbele yao kwa moyo uliopondeka na kwa huzuni nyingi. 721:7 Yer 47:3; Eze 7:17; Ay 23:2; Yos 7:5; Eze 22:14; Za 6:2; Ay 11:16Nao watakapokuuliza, ‘Kwa nini unalia kwa uchungu?’ Utasema hivi, ‘Kwa sababu ya habari zinazokuja. Kila moyo utayeyuka na kila mkono utalegea, kila roho itazimia na kila goti litalegea kama maji.’ Habari hizo zinakuja! Hakika zitatokea, asema Bwana Mwenyezi.”

8Neno la Bwana likanijia, kusema: 921:9 Kum 32:41“Mwanadamu, tabiri na useme, ‘Hili ndilo Bwana asemalo:

“ ‘Upanga, upanga,

ulionolewa na kusuguliwa:

1021:10 Za 105:5-6; Isa 34:5-6; Kum 32:41umenolewa kwa ajili ya mauaji,

umesuguliwa ili ungʼae

kama umeme wa radi!

“ ‘Je, tuifurahie fimbo ya utawala ya mwanangu Yuda? Upanga unaidharau kila fimbo ya namna hiyo.

1121:11 Yer 46:4“ ‘Upanga umewekwa tayari ili kusuguliwa,

ili upate kushikwa mkononi,

umenolewa na kusuguliwa,

umewekwa tayari kwa mkono wa muuaji.

1221:12 Yer 31:19Piga kelele na uomboleze, ee mwanadamu,

kwa kuwa upanga u dhidi ya watu wangu;

u dhidi ya wakuu wote wa Israeli.

Wametolewa wauawe kwa upanga

pamoja na watu wangu.

Kwa hiyo pigapiga kifua chako.

1321:13 Ay 9:23; 2Kor 8:2“ ‘Kwa maana upanga huu umejaribiwa na kuhakikishwa, itakuwaje basi fimbo ya ufalme ya Yuda inayoudharau kama haitakuwepo tena, bali itakuwa imeondolewa kabisa? asema Bwana Mwenyezi.’

1421:14 Hes 24:10; Eze 6:11; 30:24; 8:12“Hivyo basi, mwanadamu, tabiri

na ukapige makofi.

Upanga wako na upige mara mbili,

naam, hata mara tatu.

Ni upanga wa kuchinja,

upanga wa mauaji makuu,

ukiwashambulia kutoka kila upande.

1521:15 2Sam 17:10; Za 22:14Ili mioyo ipate kuyeyuka

na wanaouawa wawe wengi,

nimeweka upanga wa kuchinja

kwenye malango yao yote.

Lo! Umetengenezwa

umetemete kama umeme wa radi,

umeshikwa kwa ajili ya kuua.

1621:16 Eze 14:17Ee upanga, kata upande wa kuume,

kisha upande wa kushoto,

mahali popote makali yako

yatakapoelekezwa.

1721:17 Eze 22:13; 5:13; 14:17; 16:42Mimi nami nitapiga makofi,

nayo ghadhabu yangu itapungua.

Mimi Bwana nimesema.”

18Neno la Bwana likanijia kusema: 1921:19 Eze 14:21; 32:11; Yer 31:21“Mwanadamu, weka alama njia mbili ambazo upanga wa mfalme wa Babeli utapitia, njia hizo zikianzia katika nchi hiyo hiyo. Weka kibao pale ambapo njia zinagawanyika kuelekea mjini. 2021:20 Yer 49:2; Amo 1:14; Kum 3:11Weka alama njia moja kwa ajili ya upanga upate kuja dhidi ya Raba ya Waamoni na nyingine upate kuja dhidi ya Yuda na Yerusalemu iliyozungushiwa ngome. 2121:21 Mit 16:33; Hes 20:7; 23:23; Zek 10:2Kwa kuwa mfalme wa Babeli sasa amesimama katika njia panda, katika makutano ya njia mbili, akipiga ramli: anapiga kura kwa kutumia mishale, anataka shauri kwa sanamu zake, anachunguza maini ya wanyama. 2221:22 2Fal 25:1; Eze 4:2; Yer 51:14; 4:16; 32:24; Eze 26:9Upande wake wa kuume inakuja kura ya Yerusalemu, ambapo ataweka vyombo vya kuvunjia boma, ili kuamrisha mauaji, kupiga ukelele wa vita, kuweka vyombo vya kuvunjia boma kwenye malango, kuweka jeshi kuzunguka na kufanya uzingiraji. 2321:23 Hes 5:15; Eze 17:19Itakuwa kama kupiga ramli kwa uongo kwa wale watu ambao wameapa kumtii yeye. Lakini mfalme wa Babeli atawakumbusha juu ya uovu wao na kuwachukua mateka.

24“Kwa hiyo hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo: ‘Kwa sababu enyi watu mmekumbusha uovu wenu kwa kuasi waziwazi, mkidhihirisha dhambi zenu katika yale yote mfanyayo, kwa kuwa mmefanya jambo hili, mtachukuliwa mateka.

2521:25 Eze 35:5; Mwa 13:13; Eze 22:4“ ‘Ee mtawala kafiri na mwovu wa Israeli, ambaye siku yako imewadia, ambaye wakati wako wa adhabu umefikia kilele chake, 2621:26 Isa 28:5; Yer 13:18; Isa 40:4; Mt 23:12; Za 75:7hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo: Vua kilemba, ondoa taji. Kwa kuwa mambo hayatakuwa kama yalivyokuwa. Aliye mnyonge atakwezwa na aliyekwezwa atashushwa. 2721:27 Mwa 49:10; Za 2:6; Hag 2:21-22; Yer 23:5-6; Eze 37:24Mahame! Mahame! Nitaufanya mji kuwa mahame! Hautajengwa upya mpaka aje yule ambaye ndiye mwenye haki nao; yeye ndiye nitakayempa.’

2821:28 Mwa 19:38; Sef 3:8; Yer 12:12“Nawe, mwanadamu, tabiri na useme, ‘Hili ndilo Bwana Mwenyezi asemalo kuhusu Waamoni na matukano yao.

“ ‘Upanga, upanga,

umefutwa kwa ajili ya kuua,

umesuguliwa ili kuangamiza

na unametameta kama umeme wa radi!

2921:29 Eze 22:28; 35:5; Yer 27:9Wakati wakitoa maono ya uongo kwa ajili yako,

wanapobashiri uongo kwa ajili yako,

wanakuweka wewe kwenye shingo za watu wapotovu,

wale walio waovu,

wale ambao siku yao imewadia,

wakati wa adhabu yao ya mwisho.

3021:30 Yer 47:6; Eze 16:3Urudishe upanga kwenye ala yake!

Katika mahali ulipoumbiwa,

katika nchi ya baba zako,

huko nitakuhukumu.

3121:31 Za 79:6; Eze 22:20-21; Yer 51:20-23; Za 18:15; Isa 11:4; Eze 16:39Nitamwaga ghadhabu yangu juu yako

na kupuliza moto wa hasira yangu dhidi yako;

nitakutia mikononi mwa watu wakatili,

watu stadi katika kuangamiza.

3221:32 Eze 20:47-48; 25:10; Mal 4:1Mtakuwa kuni za kuwashia moto,

damu yenu itamwagwa katika nchi yenu,

wala hamtakumbukwa tena;

kwa maana Mimi Bwana nimesema.’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 21:1-32

Babuloni, Lupanga la Mulungu

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu. 3Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe. 4Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto. 5Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’

6“Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu. 7Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”

8Yehova anandiyankhulanso kuti, 9“Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti,

“Izi ndi zimene Yehova akunena:

Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.

10Lanoledwa kuti likaphe,

lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi!

“ ‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.

11“ ‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe,

ndi kuti linyamulidwe,

lanoledwa ndi kupukutidwa,

kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.

12Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu,

pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga;

zidzagweranso akalonga onse a Israeli.

Adzaphedwa ndi lupanga

pamodzi ndi anthu anga.

Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.

13“ ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’

14“Tsono mwana wa munthu, nenera

ndipo uwombe mʼmanja.

Lupanga likanthe kawiri

ngakhale katatu.

Limenelo ndilo lupanga lophera anthu.

Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa

limene likuwazungulira.

15Ndawayikira pa zipata zawo zonse

lupanga laphuliphuli

kuti ataye mtima

ndiponso kuti anthu ambiri agwe.

Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi

ndi kuti azilisolola kuphera anthu.

16Iwe lupanga, ipha anthu kumanja,

kenaka kumanzere,

kulikonse kumene msonga yako yaloza.

17Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga,

ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga

Ine Yehova ndayankhula.”

18Yehova anandiyankhulanso kuti, 19“Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda. 20Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa. 21Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe. 22Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo. 23Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.

24“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.

25“ ‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni, 26Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa. 27Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’

28“Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Lupanga, lupanga,

alisolola kuti liphe anthu,

alipukuta kuti liwononge

ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.

29Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza.

Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso.

Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa

amene tsiku lawo lafika,

ndiye kuti nthawi

ya kulangidwa kwawo komaliza.

30“ ‘Bwezerani lupanga mʼchimake.

Ku malo kumene inu munabadwira,

mʼdziko la makolo anu,

ndidzakuweruzani.

31Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu,

ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani.

Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza;

anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.

32Mudzakhala ngati nkhuni pa moto.

Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe.

Simudzakumbukiridwanso

pakuti Ine Yehova ndayankhula.’ ”