Ezekieli 19 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ezekieli 19:1-14

Maombolezo Kwa Ajili Ya Wakuu Wa Israeli

119:1 Yer 7:29; 2Nya 24:6; Eze 26:17; Yer 9:10, 20; Eze 27:32; 28:12“Wewe fanya maombolezo kuhusu wakuu wa Israeli 219:2 Hes 23:24; Mwa 49:9na useme:

“ ‘Tazama jinsi gani mama yako alivyokuwa simba jike

miongoni mwa simba!

Alilala katikati ya wana simba

na kulisha watoto wake.

319:3 Eze 19:6; 2Fal 23:31, 32Alimlea mmoja wa watoto wake,

naye akawa simba mwenye nguvu.

Akajifunza kurarua mawindo

naye akala watu.

419:4 2Nya 36:4; Mao 4:20; Ay 41:2; 2Fal 23:33-34Mataifa wakasikia habari zake,

naye akanaswa katika shimo lao.

Wakamwongoza kwa ndoana

mpaka nchi ya Misri.

519:5 2Fal 23:34; Mwa 49:9“ ‘Mama yake alipongoja na kuona tumaini lake halitimiziki,

nayo matarajio yake yametoweka,

akamchukua mwanawe mwingine

na kumfanya simba mwenye nguvu.

619:6 Yer 22:13; 2Nya 36:9; 2Fal 24:9Alizungukazunguka miongoni mwa simba,

kwa kuwa sasa alikuwa simba mwenye nguvu.

Akajifunza kurarua mawindo

naye akala watu.

719:7 Eze 29:10; 30:12Akabomoa ngome zao

na kuiharibu miji yao.

Nchi na wote waliokuwa ndani yake

wakatiwa hofu kwa kunguruma kwake.

819:8 2Fal 24:2, 11; Mao 4:20; Eze 12:13; 2Fal 24:11Kisha mataifa wakaja dhidi yake

kutoka sehemu zilizomzunguka.

Wakatanda nyavu zao kwa ajili yake,

naye akanaswa katika shimo lao.

919:9 2Fal 25:7; 24:15; 2Nya 36:6; 2Fal 19:28; Zek 11:3Kwa kutumia ndoana wakamvutia kwenye tundu

na kumleta mpaka kwa mfalme wa Babeli.

Wakamtia gerezani, hivyo kunguruma kwake

hakukusikika tena

katika milima ya Israeli.

1019:10 Za 80:8-11; Eze 15:2; Yer 17:8; Mwa 49:22“ ‘Mama yako alikuwa kama mzabibu

katika shamba lako la mizabibu

uliopandwa kando ya maji,

ukiwa unazaa sana na wenye matawi mengi

kwa sababu ya wingi wa maji.

1119:11 Eze 31:3; Dan 4:11Matawi yake yalikuwa na nguvu,

yaliyofaa kuwa fimbo ya enzi ya mtawala.

Ulikuwa mrefu kupita miti mingine

katikati ya matawi manene;

ulionekana kwa urahisi

kwa ajili ya urefu wake

na wingi wa matawi yake.

1219:12 Kum 29:28; Eze 17:10; Hos 13:15; Isa 27:11; Eze 28:17; Mwa 41:6Lakini ulingʼolewa kwa hasira kali

na kutupwa chini.

Upepo wa mashariki uliufanya usinyae,

matunda yake yakapukutika,

matawi yake yenye nguvu yakanyauka

na moto ukayateketeza.

1319:13 Eze 20:35; Hos 2:14; 2:3Sasa umepandwa jangwani

katika nchi kame na ya kiu.

1419:14 Amu 9:15; Eze 20:47; 15:4Moto ulienea kuanzia katika mmojawapo ya matawi yake makubwa

na kuteketeza matunda yake.

Hakuna tawi lenye nguvu lililobaki juu yake

lifaalo kuwa fimbo ya enzi ya mtawala.’

Hili ndilo ombolezo, na litumike kama ombolezo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 19:1-14

Nyimbo ya Maliro a Akalonga a Israeli

1“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli. 2Uzinena kuti,

“ ‘Amayi ako anali ndani?

Anali ngati mkango waukazi!

Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna;

unkalera ana ake pakati pa misona.

3Unalera mmodzi mwa ana ake,

ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu.

Unaphunzira kugwira nyama,

ndipo unayamba kudya anthu.

4Anthu amitundu anamva za mkangowo,

ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo.

Iwo anawukoka ndi ngowe

kupita nawo ku dziko la Igupto.

5“ ‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera,

amayiwo anatenganso mwana wina

namusandutsa mkango wamphamvu.

6Unkayendayenda pakati pa mikango inzake,

pakuti tsopano unali mkango wamphamvu.

Unaphunzira kugwira nyama

ndipo unayamba kudya anthu.

7Unagwetsa malinga awo,

ndikuwononga mizinda yawo.

Onse a mʼdzikomo

anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.

8Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira,

inabwera kudzalimbana nawo.

Anawutchera ukonde wawo,

ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.

9Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga.

Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni

ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende

ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso

ku mapiri a Israeli.

10“ ‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa

wodzalidwa mʼmbali mwa madzi.

Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri

chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.

11Nthambi zake zinali zolimba,

zoyenera kupangira ndodo yaufumu.

Unatalika nusomphoka pakati pa

zomera zina.

Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake,

ndi nthambi zake zambiri.

12Koma unazulidwa mwaukali

ndipo unagwetsedwa pansi.

Unawuma ndi mphepo ya kummawa,

zipatso zake zinayoyoka;

nthambi zake zolimba zinafota

ndipo moto unapsereza mtengo wonse.

13Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu,

dziko lowuma ndi lopanda madzi.

14Moto unatulukanso mu mtengomo

ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake.

Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo

yoyenera kupangira ndodo yaufumu.

Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’ ”