Ezekieli 18 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ezekieli 18:1-32

Roho Itendayo Dhambi Itakufa

1Neno la Bwana likanijia kusema: 218:2 Isa 3:15; Mao 5:7; Ay 21:19; Yer 31:29“Je, ninyi watu mna maana gani kutumia mithali hii inayohusu nchi ya Israeli:

“ ‘Baba wamekula zabibu zenye chachu,

nayo meno ya watoto yametiwa ganzi’?

318:3 Za 49:4“Hakika kama niishivyo, asema Bwana Mwenyezi, hamtatumia tena mithali hii katika Israeli. 418:4 Mwa 18:32; Rum 6:23; Ebr 12:9; 2Fal 14:6; Mit 13:21; Kut 17:14; Ay 21:20; Isa 42:5; Eze 33:8Kwa kuwa kila roho ni mali yangu, kama vile ilivyo roho ya baba, vivyo hivyo roho ya mtoto ni mali yangu. Roho itendayo dhambi ndiyo itakayokufa.

5“Mtu aweza kuwa ni mwenye haki

atendaye yaliyo haki na sawa.

618:6 Eze 6:2; 22:9; Kum 4:19; Amo 5:26; Ebr 13:4; Eze 6:13; Law 15:24Hakula katika mahali pa ibada za miungu

kwenye milima

wala hakuziinulia macho sanamu

za nyumba ya Israeli.

Hakumtia unajisi mke wa jirani yake,

wala hakukutana kimwili na mwanamke

wakati wa siku zake za hedhi.

718:7 Yak 5:4; Kut 22:26; Kum 24:12; 24:12; 15:11; Lk 3:11; Kut 20:15; Ay 22:7Hamwonei mtu yeyote,

bali hurudisha kilichowekwa rehani kwake.

Hanyangʼanyi, bali huwapa wenye njaa chakula chake

na huwapa nguo walio uchi.

818:8 Zek 8:16; Kut 18:21; Kum 23:19-20; Yer 22:3; Kut 22:25; Law 25:35-37Hakopeshi kwa riba

wala hajipatii faida ya ziada.

Huuzuia mkono wake usifanye mabaya,

naye huhukumu kwa haki kati ya mtu na mtu.

918:9 Hab 2:4; Law 18:5; Amo 5:4; Law 19:37; Eze 11:12; 20:11Huzifuata amri zangu

na kuzishika sheria zangu kwa uaminifu.

Huyo mtu ni mwenye haki;

hakika ataishi,

asema Bwana Mwenyezi.

1018:10 Kut 21:12; Eze 22:6“Aweza kuwa ana mwana jeuri, amwagaye damu au atendaye mojawapo ya mambo haya 1118:11 Kut 22:22; Ay 24:9; Isa 54:9; 59:6-7; Hab 2:6; Kut 22:17; Eze 16:49(ingawa baba yake hakufanya mojawapo ya haya):

“Hula katika mahali pa ibada za miungu kwenye milima.

Humtia unajisi mke wa jirani yake.

1218:12 Kut 22:22; 22:27; Ay 24:9; Amo 4:1; 2Fal 21:11Huwaonea maskini na wahitaji.

Hunyangʼanyana.

Harudishi kile kilichowekwa rehani kwake.

Huziinulia sanamu macho.

Hufanya mambo ya machukizo.

1318:13 Kut 22:25; Law 20:9; Hos 12:14; Eze 33:4-5Hukopesha kwa riba na kutafuta faida ya ziada.

Je, mtu wa namna hii ataishi? Hapana, hataishi! Kwa sababu amefanya mambo haya yote ya machukizo, hakika atauawa na damu yake itakuwa juu ya kichwa chake mwenyewe.

1418:14 2Nya 34:21; Mit 23:24“Lakini yawezekana mwana huyo ana mwana aonaye dhambi hizi zote anazofanya baba yake, naye ingawa anaziona, yeye hafanyi mabaya kama haya:

1518:15 Eze 22:9; Za 24:4“Hakula katika mahali pa ibada za miungu

kwenye milima,

wala hainulii macho sanamu

za nyumba ya Israeli.

Hakumtia unajisi

mke wa jirani yake.

1618:16 Kut 22:27; Ay 22:7; Mit 22:9; Za 41:1; Eze 16:49; Isa 7:10Hakumwonea mtu yeyote

wala hakutaka rehani kwa ajili ya mkopo.

Hanyangʼanyi,

bali huwapa wenye njaa chakula chake

na huwapa nguo walio uchi.

1718:17 Za 1:2Huuzuia mkono wake usitende dhambi,

hakopeshi kwa riba

wala hajipatii faida ya ziada.

Huzishika amri zangu

na kuzifuata sheria zangu.

Hatakufa kwa ajili ya dhambi za baba yake; hakika ataishi. 1818:18 Eze 3:18Lakini baba yake atakufa kwa ajili ya dhambi yake mwenyewe, kwa sababu alitoza bei isiyo halali kwa nguvu, akamnyangʼanya ndugu yake na kufanya yaliyo mabaya miongoni mwa watu wake.

1918:19 Kut 20:5; Kum 5:9; Yer 15:4; Zek 1:3-6“Lakini mnauliza, ‘Kwa nini mwana asiadhibiwe kwa uovu wa baba yake?’ Kwa vile mwana ametenda yaliyo haki na sawa na amekuwa mwangalifu kuzishika amri zangu zote, hakika ataishi. 2018:20 Kum 24:16; Rum 2:9; Isa 3:10; Hes 15:31; 1Fal 8:32; 2Fal 14:6; Eze 7:27; Mt 16:27Roho itendayo dhambi ndiyo itakayokufa. Mwana hataadhibiwa kwa ajili ya makosa ya baba yake, wala baba hataadhibiwa kwa ajili ya makosa ya mwanawe. Haki ya mtu mwenye haki itahesabiwa juu yake na uovu wa mtu mwovu utalipizwa juu yake.

2118:21 Eze 13:22; 33:12-19; Yer 18:8; Mwa 26:5“Lakini mtu mwovu akiacha dhambi zake zote alizozitenda na kushika amri zangu zote na kufanya lililo haki na sawa, hakika ataishi, hatakufa. 2218:22 Dan 4:27; Mik 7:19; Mit 18:20-24; Isa 43:25Hakuna kosa lolote alilotenda litakalokumbukwa juu yake. Kwa ajili ya mambo ya haki aliyoyatenda, ataishi. 2318:23 Mao 3:33; 2Pet 3:9; 1Tim 2:4; Za 147:11; Ay 37:23; Eze 16:6; Mik 7:18Je, mimi ninafurahia kifo cha mtu mwovu? Asema Bwana Mwenyezi. Je, si mimi ninafurahi wanapogeuka kutoka njia zao mbaya na kuishi?

2418:24 Ay 35:8; 2Pet 2:20-22; Ebr 10:38; Yer 34:6; Eze 15:8; 1Sam 15:11; 2Nya 24:17-20“Lakini kama mtu mwenye haki akiacha haki yake na kutenda dhambi na kufanya mambo ya machukizo ambayo mtu mwovu hufanya, Je, ataishi? Hakuna hata mojawapo ya matendo ya haki aliyotenda litakalokumbukwa. Kwa sababu ya kukosa uaminifu kwake anayo hatia na kwa sababu ya dhambi alizozitenda, atakufa.

2518:25 Sef 3:5; Mal 3:1-17; Mwa 18:25; Yer 2:29; Eze 33:17; Mal 2:17“Lakini mnasema, ‘Njia ya Bwana si ya haki.’ Sikia, ee nyumba ya Israeli: Njia yangu siyo iliyo ya haki? Je, si njia zenu ndizo ambazo si za haki? 2618:26 Eze 18:24Kama mtu mwenye haki akiacha haki yake na kutenda dhambi, atakufa kwa ajili ya dhambi yake, kwa sababu ya dhambi alizotenda, atakufa. 2718:27 Isa 1:18; Eze 13:22Lakini mtu mwovu akigeuka kutoka maovu aliyoyatenda na kufanya yaliyo haki na sawa, ataokoa maisha yake. 2818:28 Eze 18:14; Isa 55:7Kwa kuwa anayafikiria na kugeuka kutoka makosa yake yote aliyoyatenda na kuyaacha, hakika ataishi, hatakufa. 29Lakini nyumba ya Israeli inasema, ‘Njia za Bwana si haki.’ Je, njia zangu si za haki, ee nyumba ya Israeli? Je, si njia zenu ndizo ambazo si za haki?”

3018:30 Yer 35:15; Eze 7:13; Mt 3:2; Hos 12:6; 1Pet 1:17; Isa 27“Kwa hiyo, ee nyumba ya Israeli, nitawahukumu, kila mmoja sawasawa na njia zake, asema Bwana Mwenyezi. Tubuni! Geukeni kutoka makosa yenu yote, ndipo dhambi haitakuwa anguko lenu. 3118:31 Za 51:10; Isa 1:16-17; Eze 36:26; Efe 4:22; Amu 6:8; Yer 27:13; Eze 11:19Tupilieni mbali makosa yenu yote mliyoyatenda, nanyi mpate moyo mpya na roho mpya. Kwa nini mfe, ee nyumba ya Israeli? 3218:32 2Nya 7:14; Ay 37:23; Eze 33:11; Ay 22:23; Isa 55:7; Mal 3:7; Eze 16:6Kwa maana sifurahii kifo cha mtu awaye yote afaye katika uovu, asema Bwana Mwenyezi. Tubuni basi, mkaishi!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 18:1-32

Munthu Wochimwa Adzafa

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti:

“ ‘Nkhuyu zodya akulu zimapota

ndi ana omwe?’ ”

3“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli. 4Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.

5“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama

amene amachita zolungama ndi zolondola.

6Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo

kapena kupembedza mafano a Aisraeli.

Iye sayipitsa mkazi wa mnzake

kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.

7Iye sapondereza munthu wina aliyense,

koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake.

Iye salanda zinthu za osauka,

koma amapereka chakudya kwa anthu anjala,

ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.

8Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira,

kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu.

Amadziletsa kuchita zoyipa

ndipo sakondera poweruza milandu.

9Iye amatsatira malangizo anga,

ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika.

Munthu ameneyo ndi wolungama;

iye adzakhala ndithu ndi moyo,

akutero Ambuye Yehova.

10“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere. 11Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo.

“Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo.

Amayipitsa mkazi wa mnzake.

12Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa.

Amalanda zinthu za osauka.

Sabweza chikole cha munthu wa ngongole.

Iye amatembenukira ku mafano

nachita zonyansa.

13Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu.

Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.

14“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.

15“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo.

Sapembedza mafano a ku Israeli.

Sayipitsa mkazi wa mnzake.

16Sapondereza munthu wina aliyense.

Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka.

Salanda zinthu za munthu.

Amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.

17Amadziletsa kuchita zoyipa.

Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja.

Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga.

Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu. 18Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.

19“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse. 20Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.

21“ ‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi. 22Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo. 23Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.

24“ ‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.

25“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama? 26Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo. 27Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake. 28Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa. 29Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?

30“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo. 31Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli? 32Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”