Ayubu 36 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 36:1-33

Elihu Atukuza Wema Wa Mungu

1Elihu akaendelea kusema:

2“Nivumilie kidogo zaidi nami nitakuonyesha

kwamba yako mengi zaidi ya kusemwa kwa ajili ya Mungu.

336:3 Ay 4:17; 8:3Ninayapata maarifa yangu kutoka mbali,

nami nitamhesabia haki Muumba wangu.

436:4 Ay 6:28; 13:6; 37:5, 16, 23; 32:17Uwe na hakika kwamba maneno yangu si ya uongo;

mmoja aliye mkamilifu katika maarifa yuko pamoja na wewe.

536:5 Za 31:22; 69:33; Hes 23:19; Rum 11:29“Mungu ni mwenye nguvu, lakini hamdharau mwanadamu;

ni mwenye nguvu, naye ni thabiti katika shauri lake.

636:6 Ay 8:22; 4:10Hawaachi waovu waendelee kuishi,

bali huwapa walioteswa haki yao.

736:7 Za 34:15; 113:8; Mt 6:18; Isa 22:23Yeye haondoi macho yake kwa wenye haki;

huwaketisha penye viti vya enzi pamoja na wafalme

na kuwatukuza milele.

836:8 2Sam 3:34; 2Fal 23:33Lakini ikiwa watu wamefungwa kwenye minyororo,

wakiwa wameshikiliwa na kamba za mateso,

936:9 Ay 15:25huwaonyesha yale waliyoyatenda,

kwamba wametenda dhambi kwa majivuno.

1036:10 Ay 33:16; 2Fal 17:13; Ay 5:17Huwafanya wao kusikia maonyo,

na huwaagiza kutubu uovu wao.

1136:11 Kut 28:1; Hag 1:12; Isa 1; 19Kama wakitii na kumtumikia,

wataishi siku zao zilizobaki katika mafanikio,

na miaka yao katika utoshelevu.

1236:12 Law 26:38; Ay 15:22; 4:21; Efe 4:18Lakini wasiposikiliza,

wataangamia kwa upanga,

nao watakufa pasipo maarifa.

1336:13 Ay 15:12; Rum 2:5; Ay 5:2; 4:17; Amo 4:11“Wasiomcha Mungu moyoni mwao huficha chuki;

hata anapowafunga, hawamwombi msaada.

1436:14 Kum 23:17Wanakufa wangali vijana,

miongoni mwa wanaume hanithi wa mahali pa kuabudia miungu.

1536:15 Ay 5:15; 2Kor 12:10; Ay 33:16; 34:33Bali wao wanaoteseka huwaokoa katika mateso yao,

na kuzungumza nao katika dhiki zao.

1636:16 Hos 2:14; Za 23:5; 78:19“Yeye anakubembeleza utoke katika mataya ya dhiki,

ili kukuweka mahali palipo na nafasi mbali na kizuizi,

hadi kwenye meza yako ya faraja iliyojaa vyakula vizuri.

1736:17 Ay 20:29; 22:11Lakini sasa umelemewa na hukumu kwa ajili ya uovu;

hukumu na haki vimekukamata.

1836:18 Kut 23:8; Amo 5:12; Ay 34:33Uwe mwangalifu ili yeyote asikushawishi kwa utajiri;

usipotoshwe kwa fungu kubwa la rushwa.

1936:19 Za 49:6; Yer 9:23Je, utajiri wako hata nguvu zako nyingi

vinaweza kukusaidia usiingie kwenye dhiki?

2036:20 Ay 34:20-25Usiutamani usiku uje,

ili uwaburute watu mbali na nyumba zao.

2136:21 Ay 34:33; Za 66:18; Ebr 11:25Jihadhari usigeukie uovu,

ambao unaupenda zaidi kuliko mateso.

2236:22 Isa 40:13; Rum 11:34“Mungu ametukuzwa katika nguvu zake.

Ni nani aliye mwalimu kama yeye?

2336:23 Ay 34:10, 13; Rum 11:33; Mwa 18:25; Kum 32:4Ni nani aliyemwelekeza katika njia zake,

au kumwambia, ‘Wewe umetenda yasiyo sawa’?

2436:24 1Nya 16:24; Za 35:27; 59:16; Ufu 15:3Kumbuka kuzitukuza kazi zake,

ambazo watu wamezisifu katika wimbo.

2536:25 Rum 1:20Wanadamu wote wameiona;

watu wanaikazia macho kwa mbali.

2636:26 1Kor 13:12; Mwa 21:33; Ebr 1:12Tazama jinsi Mungu alivyo mkuu,

kupita ufahamu wetu!

Hesabu ya miaka yake haitafutiki.

2736:27 2Sam 1:21; Za 147:8“Yeye huvuta juu matone ya maji,

ayachujayo kama mvua kutoka kwenye vijito;

2836:28 Ay 22:11; Mt 5:45mawingu huangusha chini maji yake,

nayo mvua nyingi huwanyeshea wanadamu.

2936:29 Mit 8:28; Isa 40:22Ni nani ajuaye jinsi ayatandazavyo mawingu,

jinsi angurumavyo kutoka hemani mwake.

3036:30 Kut 19:16; Yer 10:13; Hab 3:11; Isa 51:10; Za 18:12, 14; 97:4Tazama jinsi anavyotandaza umeme wa radi kumzunguka,

naye huvifunika vilindi vya bahari.

3136:31 1Fal 17:1; Amo 4:7-8; Isa 30:23; Mdo 14:17Hivi ndivyo atawalavyo mataifa,

na kuwapa chakula kwa wingi.

3236:32 Ay 28:24; Za 18:14Huujaza mkono wake kwa umeme wa radi,

na kuuagiza kulenga shabaha yake.

33Ngurumo zake hutangaza dhoruba inayokuja;

hata mifugo hujulisha kukaribia kwake.36:33 Au: hutangaza kuja kwake.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 36:1-33

1Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:

2“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani

kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.

3Nzeru zanga ndimazitenga kutali;

ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.

4Ndithudi mawu anga si abodza;

wanzeru zangwiro ali ndi inu.

5“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;

Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.

6Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo

koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.

7Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;

amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu

ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.

8Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,

ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,

9Iye amawafotokozera zomwe anachita,

kuti iwo anachimwa modzikuza.

10Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake

ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.

11Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,

adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere,

adzatsiriza zaka zawo mosangalala.

12Koma ngati samvera,

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo adzafa osadziwa kanthu.

13“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;

akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.

14Amafa akanali achinyamata,

pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.

15Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;

Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.

16“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,

kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani,

kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.

17Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;

chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.

18Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;

musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.

19Kodi chuma chanu

kapena mphamvu zanu zonse

zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?

20Musalakalake kuti usiku ubwere,

pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.

21Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,

chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.

22“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.

Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?

23Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,

kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’

24Kumbukirani kutamanda ntchito zake

zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.

25Anthu onse amaziona ntchitozo;

anthuwo amaziona ali kutali.

26Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe!

Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.

27“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo,

timene timasungunuka nʼkukhala mvula;

28mitambo imagwetsa mvulayo

ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.

29Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera,

momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?

30Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse,

zimafika ngakhale pansi pa nyanja.

31Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu

ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.

32Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani,

ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.

33Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho;

ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.