Ayubu 29 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 29:1-25

Ayubu Anamaliza Utetezi Wake

129:1 Za 18:28; Ay 13:12Ayubu akaendelea na hoja yake, akasema:

229:2 Yer 1:12; 44:27“Tazama jinsi ninavyoitamani miezi iliyopita,

zile siku ambazo Mungu alikuwa akinilinda,

329:3 Ay 11:17; 12:25wakati taa yake iliniangazia kichwani changu,

na kwa mwanga wake Mungu nikapita katikati ya giza!

429:4 Za 25:14; Mit 3:32Natamani siku zile nilizokuwa katika ustawi wangu,

wakati urafiki wa Mungu wa ndani ulipoibariki nyumba yangu,

529:5 Za 127:3-5; 128:3; Rum 4:1wakati Mwenyezi alikuwa pamoja nami,

nao watoto wangu walikuwa wamenizunguka,

629:6 Ay 20:17; Za 81:16; Mwa 49:20; Kum 32:13wakati njia yangu ilikuwa imenyweshewa siagi,

nao mwamba ukanimiminia vijito vya mafuta ya zeituni.

729:7 Ay 5:4; 31:21; Yer 20:2; 38:7“Wakati nilipokwenda kwenye lango la mji

na kuketi katika kiwanja,

829:8 1Tim 5:1; Law 19:32vijana waliniona wakakaa kando,

nao wazee walioketi wakasimama;

929:9 Amu 16:19; Mit 30:32wakuu wakaacha kuzungumza

na kuziba vinywa vyao kwa mikono yao;

1029:10 Za 137:6wenye vyeo wakanyamazishwa,

nazo ndimi zao zikagandamana na makaakaa ya vinywa vyao.

1129:11 Ay 4:4; Ebr 11:4Yeyote aliyenisikia alinena mema juu yangu,

nao walioniona walinisifu,

1229:12 Kum 24:17; Ay 31:17-21; Za 72:12; Mit 21:13kwa sababu nilimwokoa maskini aliyeomba msaada,

naye yatima aliyekuwa hana wa kumsaidia.

1329:13 Ay 31:20; 22:9; Kum 10:18Mtu aliyekuwa karibu kufa alinibariki,

nami niliufanya moyo wa mjane kuimba.

1429:14 2Sam 8:15; Rum 13:14; Efe 6:14Niliivaa haki kama vazi langu;

uadilifu ulikuwa joho langu na kilemba changu.

1529:15 Hes 10:31Nilikuwa macho ya kipofu

na miguu kwa kiwete.

1629:16 Ay 24:4; Mit 29:7Nilikuwa baba kwa mhitaji;

nilimtetea mgeni.

1729:17 Ay 24:9; 4:10, 11; Za 3:7Niliyavunja meno makali ya waovu,

na kuwapokonya wahanga kwenye meno yao.

1829:18 Za 62:2; Mit 3:1-2“Nikafikiri, ‘Nitafia katika nyumba yangu mwenyewe,

nazo siku zangu zitakuwa nyingi kama chembechembe za mchanga.

1929:19 Hes 24:6; Yer 17:8Mizizi yangu itafika mpaka kwenye maji,

nao umande utakaa juu ya matawi yangu usiku kucha.

2029:20 Za 18:34; Isa 38:12; Mwa 49:24Utukufu wangu utabakia kuwa mpya ndani yangu,

upinde wangu daima utaendelea kuwa mpya mkononi mwangu.’

2129:21 Ay 29:21“Watu walinisikiliza kwa tumaini,

wakingojea ushauri wangu kwa utulivu.

2229:22 Kum 32:2Baada ya mimi kuzungumza, hawakusema zaidi;

maneno yangu yaliingia masikioni mwao kwa makini.

23Waliningojea kama manyunyu ya mvua

na kuyapokea maneno yangu

kama ardhi inyonyavyo mvua ya vuli.

24Walipokata tamaa niliwaonyesha uso wa furaha;

nuru ya uso wangu ilikuwa ya thamani kwao.

2529:25 Ay 31:31; 4:4Niliwachagulia njia na kukaa kama mkuu wao;

niliishi kama mfalme katikati ya majeshi yake;

nikawa kama yeye anayewafariji waombolezaji.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 29:1-25

1Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

2“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi,

masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,

3pamene nyale yake inkandiwunikira

ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!

4Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri,

pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,

5nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane,

ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,

6pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka,

ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.

7“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda

ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,

8anyamata amati akandiona ankapatuka

ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;

9atsogoleri ankakhala chete

ndipo ankagwira pakamwa pawo;

10anthu otchuka ankangoti duu,

ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.

11Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga,

ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,

12chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo,

ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.

13Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa;

ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.

14Chilungamo chinali ngati chovala changa;

chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.

15Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya;

ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.

16Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi;

ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.

17Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa

ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.

18“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga,

masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.

19Mizu yanga idzatambalalira ku madzi,

ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.

20Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine,

ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’

21“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi,

ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.

22Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso;

mawu anga ankawagwira mtima.

23Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula

ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.

24Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira;

kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.

25Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu;

ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo;

ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”