Ayubu 27 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ayubu 27:1-23

Hotuba Ya Mwisho Ya Ayubu

Ayubu Anadumisha Uadilifu Wake

127:1 Ay 29:1Ndipo Ayubu akaendelea na hoja yake, akasema:

227:2 Ay 9:18; 34:5; Isa 45:9; 1Sam 1:10“Hakika kama Mungu aishivyo, aliyeninyima haki yangu,

Mwenyezi ambaye amenifanya

nionje uchungu wa nafsi,

327:3 Mwa 2:7; Za 144:4kwa muda wote nitakaokuwa na uhai ndani yangu,

nayo pumzi ya Mungu ikiwa puani mwangu,

427:4 Ay 6:28; 12:16; 16:17midomo yangu haitanena uovu,

wala ulimi wangu hautatamka udanganyifu.

527:5 Ay 2:9; 10:7; 32:2Sitakubaliana nanyi kabisa kuwa mko sahihi;

hadi nife, sitakana uadilifu wangu.

627:6 Ay 29:14; Za 119:121; Isa 59:17; 61:10; Rum 2:15Nitadumisha haki yangu wala sitaiacha;

dhamiri yangu haitanisuta muda wote ninaoishi.

7“Watesi wangu wawe kama waovu,

nao adui zangu wawe kama wasio haki!

827:8 Ay 8:13; Hes 16:22; Lk 12:20; Mt 16:26Kwa maana mtu asiyemcha Mungu

analo tegemeo gani anapokatiliwa mbali,

Mungu anapouondoa uhai wake?

927:9 Zek 7:13; Mik 3:4; 1Sam 8:18Je, Mungu husikiliza kilio chake,

shida zimjiapo?

1027:10 Ay 22:26Je, anaweza kumfurahia Mwenyezi?

Je, atamwita Mungu nyakati zote?

1127:11 Ay 36:23; 27:13“Nitawafundisha juu ya uweza wa Mungu;

njia za Mwenyezi sitazificha.

12Ninyi nyote mmeona hili wenyewe.

Ni ya nini basi mazungumzo haya yasiyo na maana?

1327:13 Ay 15:20; 16:19“Hili ndilo fungu ambalo Mungu humpa mtu mwovu,

urithi ule mtu mdhalimu anapokea kutoka kwa Mwenyezi:

1427:14 Mao 2:22; Es 9:10; Hos 9:13; Ay 20:10; 2Fal 10:6-10Hata kama watoto wake watakuwa wengi kiasi gani,

fungu lao ni kuuawa kwa upanga;

wazao wake hawatakuwa kamwe

na chakula cha kuwatosha.

1527:15 Za 78:64Tauni itawazika wale watakaonusurika miongoni mwao,

nao wajane wao hawatawaombolezea.

1627:16 Zek 9:3Ajapokusanya fedha nyingi kama mavumbi,

na mavazi kama malundo ya udongo wa mfinyanzi,

1727:17 Mit 13:22; Mhu 2:26yale yote mtu mwovu aliyojiwekea akiba, mwenye haki atayavaa,

naye asiye na hatia ataigawanya fedha yake.

1827:18 Ay 8:14; Isa 1:8; 24:20; Mao 2:6Nyumba aijengayo ni kama utando wa buibui,

kama kibanda alichotengeneza mlinzi.

1927:19 Ay 3:13; Hes 20:26Yeye hulala akiwa tajiri, lakini ndiyo mara ya mwisho;

afunguapo macho yake, yote yametoweka.

2027:20 Ay 15:21; 20:8Vitisho humjia kama mafuriko;

dhoruba humkumba ghafula usiku.

2127:21 Ay 38:24; Yer 13:24; Ay 30:22; 7:10; Yer 22:22Upepo mkali wa mashariki humchukua, naye hutoweka;

humzoa kutoka mahali pake.

2227:22 Yer 13:14; Eze 5:11; Ay 11:20Humvurumisha bila huruma,

huku akikimbia kasi kukwepa nguvu zake.

2327:23 Ay 7:10; 18:18Upepo humpigia makofi kwa dharau,

na kumfukuza atoke mahali pake.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 27:1-23

1Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

2“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,

Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,

3nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,

mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,

4pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,

lilime langa silidzayankhula zachinyengo.

5Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;

mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.

6Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;

chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.

7“Mdani wanga akhale ngati woyipa,

wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!

8Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,

pamene Mulungu achotsa moyo wake?

9Kodi Mulungu amamva kulira kwake

pamene zovuta zamugwera?

10Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?

Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?

11“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo

sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.

12Inu mwadzionera nokha zonsezi.

Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?

13“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,

cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.

14Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo

zidzukulu zake zidzasowa zakudya.

15Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,

ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.

16Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,

ndi kukundika zovala ngati mchenga,

17zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,

ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.

18Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,

ili ngati msasa umene mlonda amamanga.

19Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;

akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.

20Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;

mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.

21Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo

imamuchotsa pamalo pake.

22Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,

pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.

23Mphepoyo imamuwomba ndithu

ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”