2 Samweli 7 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

2 Samweli 7:1-29

Ahadi Ya Mungu Kwa Daudi

(1 Nyakati 17:1-15)

17:1 1Nya 22:18; 17:1; 2Sam 6:3; Dan 4:29-30Baada ya mfalme kuingia rasmi katika jumba lake la kifalme, naye Bwana akiwa amemstarehesha pande zote mbali na adui zake, 27:2 2Sam 12:1; 1Fal 1:8, 22; 1Nya 29:29; 2Nya 9:29; 2Sam 5:11; 1Fal 3:1; 7:1-7; 9:1; 2Nya 8:1; Yer 22:14; Hag 1:4; Kut 26:1; Za 132:3; Mdo 7:45-46; Kut 40:21akamwambia nabii Nathani, “Mimi hapa, ninaishi katika jumba la kifalme la mierezi, wakati Sanduku la Mungu limebaki katika hema.”

37:3 1Sam 10:7; Za 132:1-5; 1Fal 8:17; 1Nya 22:7; 28:2Nathani akamjibu mfalme, “Lolote ulilo nalo moyoni, endelea ukalifanye, kwa maana Bwana yu pamoja nawe.”

4Usiku ule neno la Bwana likamjia Nathani, kusema:

57:5 1Fal 8:19; 1Nya 22:8; 1Fal 5:3-5; 1Nya 28:3“Nenda ukamwambie mtumishi wangu Daudi, ‘Hili ndilo asemalo Bwana: Je, ewe ndiwe wa kunijengea mimi nyumba ili nikae ndani yake? 67:6 Mdo 7:45; Kut 40:18, 34; Yos 18:1; 1Fal 8:16Sijakaa ndani ya nyumba tangu siku niliyowaleta Waisraeli kutoka Misri hadi leo. Nimekuwa nikitembea kutoka mahali pamoja hadi mahali pengine ndani ya hema kama makao yangu. 77:7 Kum 23:14; 2Sam 5:2; 1Fal 8:27; Isa 66:1; Law 26:11; Za 78:72; Eze 34:2, 15, 23; Mt 2:6; Mdo 20:28; 1Pet 5:2Popote nilipotembea pamoja na Waisraeli wote, je, nimewahi kumwambia kiongozi wao yeyote niliyemwamuru kuwachunga watu wangu Israeli, “Kwa nini hujanijengea nyumba ya mierezi?” ’

87:8 1Sam 16:11; 1Nya 21:17; Za 74:1; Amo 7:15; Isa 9:16; 16:1; 2Sam 6:21; Za 78:70-72; 2Kor 6:18“Sasa basi, mwambie mtumishi wangu Daudi, ‘Hili ndilo asemalo Bwana Mwenye Nguvu Zote: Nilikutoa wewe kutoka machungani na kutoka kuandama kundi la kondoo na mbuzi ili kuwaongoza watu wangu Israeli. 97:9 1Sam 18:14; 2Sam 5:10; Za 18:37-42; Kut 11:3; Mwa 12:2; 1Nya 17:8; Lk 1:52Nimekuwa pamoja nawe popote ulipokwenda, nami nimekuondolea mbali adui zako wote mbele yako. Basi nitalifanya jina lako kuwa kuu kama majina ya watu walio wakuu sana duniani. 107:10 Kut 15:17; Isa 5:1-7; 2Fal 21:8; 2Nya 33:8; Za 89:22-23; 147:14; Isa 54:14; 60:18; Za 44:2; 80:8; Yer 24:6; Amo 9:15Nami nitawapatia watu wangu Israeli mahali niwapande humo ili kwamba wawe na nyumbani kwao wenyewe wasisumbuliwe tena. Watu waovu hawatawaonea tena, kama walivyofanya mwanzoni, 117:11 Amu 2:16; 1Sam 12:9-11; 1Fal 2:24; 1Sam 25:28; Za 89:35-37; Lk 1:32-33; Mdo 13:22-23; 2Tim 2:8; Kut 1:21; Isa 7:2na kama walivyofanya tangu mwanzo wakati nilipowaweka viongozi juu ya watu wangu Israeli. Pia nitawapa raha mbele ya adui zenu wote.

“ ‘Bwana akuambia kwamba Bwana mwenyewe atakujengea nyumba. 127:12 Mwa 15:15; 1Fal 2:1; Mdo 13:36; 1Fal 8:20; Za 132:11-12; Yer 30:21; 33:15; 2Nya 23:3Siku zako zitakapokwisha nawe ulale pamoja na baba zako, nitainua mzao wako aingie mahali pako, ambaye atatoka viunoni mwako, nami nitauimarisha ufalme wake. 137:13 Kum 12:5; 1Fal 5:5; 6:12; 8:19, 29; Kum 16:11; 2Fal 21:4, 7; Mit 25:5; Dan 7:27; Mwa 9; 16; 2Sam 22:51; 1Fal 2:4, 45; 1Nya 22; 10; 28:6; 2Nya 6:16; 7:18; 13:5; 21:7; Za 89:3-4; Isa 9:7; 16:5; Yer 17:25; 33:17-21Yeye ndiye atakayejenga nyumba kwa ajili ya Jina langu, nami nitaimarisha kiti cha enzi cha ufalme wake milele. 147:14 Za 2:7; 89:26; Yer 3:19; Mt 3:17; Yn 1:49; 2Kor 6:18; Ebr 1:5; Ufu 21:7; Kum 8:5; 1Fal 11:34; 1Nya 22:10; Ebr 12:7; Za 89:30-33; Mit 13:24Nitakuwa baba yake, naye atakuwa mwanangu. Atakapokosea nitamwadhibu kwa fimbo ya wanadamu, kwa adhabu ya kupigwa na wanadamu. 157:15 1Fal 2:4; 6:12; 8:25; 9:5; 11:13; 2Fal 19:34; 2Nya 6:16; 7:18; 21:7; Za 89:34; Yer 33; 17; 1Sam 13:13; 15:28; 16:14; 7:16; Za 89:36-37; Lk 1:33; Za 9:7; 93:2; 103:19Lakini upendo wangu kamwe hautaondolewa kwake, kama nilivyouondoa kwa Sauli, niliyemwondoa atoke mbele yako. 16Nyumba yako na ufalme wako utadumu milele mbele zangu, kiti chako cha enzi kitafanywa imara milele.’ ”

17Nathani akamwarifu Daudi maneno yote ya maono haya.

Maombi Ya Daudi

(1 Nyakati 17:16-27)

187:18 Kut 3:11; 1Sam 18:18Ndipo Mfalme Daudi akaingia ndani, akaketi mbele za Bwana, akasema:

“Ee Bwana Mwenyezi, mimi ni nani, na jamaa yangu ni nini, hata umenileta mpaka hapa nilipo? 197:19 Isa 55:8-9Naam, kana kwamba hili halitoshi machoni pako, Ee Bwana Mwenyezi, wewe umenena pia kuhusu siku zijazo za nyumba ya mtumishi wako. Je, hii ndiyo njia yako ya kawaida ya kushughulika na mwanadamu, Ee Bwana Mwenyezi?

207:20 Isa 38:15; Yn 21:17; 1Sam 16:7; Mwa 18:19; Za 139:1“Je, Daudi aweza kukuambia nini zaidi? Kwa maana unamjua mtumishi wako, Ee Bwana Mwenyezi. 217:21 Efe 4:32Kwa ajili ya neno lako na kwa mapenzi yako, umefanya jambo hili kubwa na kulifanya lijulikane na lifahamike kwa mtumishi wako.

227:22 Za 48:1; 77; 13; 86:10; Yer 10:6; Kum 3:24; Kut 9:14; 8:10; 20:4; 10:2; Amu 6:13; 1Nya 16:25; 2Nya 2:5; Kum 4:35; Isa 45:5“Tazama jinsi ulivyo mkuu, Ee Bwana Mwenyezi! Hakuna mwingine kama wewe, wala hakuna Mungu ila wewe, kama vile tulivyosikia kwa masikio yetu wenyewe, 237:23 Kum 4:32-38; 33:29; 1Sam 12:22; Hes 6:27; Kum 10:21; 7:7-8; 9:29; 15:15; Za 147:20; Neh 1:10Naye ni nani aliye kama watu wako Israeli, taifa pekee duniani ambalo Mungu alitoka kwenda kulikomboa kwa ajili yake mwenyewe, na kujifanyia jina mwenyewe, kwa kufanya maajabu makubwa na ya kutisha kwa kuwafukuza mataifa na miungu yao mbele ya watu wako, ambao uliwakomboa kutoka Misri? 247:24 Kum 26:18; Kut 6:6-7; Za 48:14Umeimarisha watu wako Israeli hasa kama watu wako mwenyewe milele, nawe, Ee Bwana, umekuwa Mungu wao.

257:25 Hes 23:19; 2Nya 1:9“Basi sasa, Bwana, ukaitimize ahadi uliyosema kuhusu mtumishi wako na nyumba yake milele. Fanya kama ulivyoahidi, 267:26 Kut 6:3; Neh 9:5; Za 72:19; 96:8; Mt 6:9; 1Sam 25:28ili kwamba jina lako litukuke milele. Ndipo watu watasema, ‘Bwana Mwenye Nguvu Zote ni Mungu juu ya Israeli!’ Nayo nyumba ya mtumishi wako Daudi itakuwa imara mbele zako.

27“Ee Bwana Mwenye Nguvu Zote, Mungu wa Israeli, umelifunua hili kwa mtumishi wako, ukisema, ‘Nitakujengea nyumba.’ Hivyo mtumishi wako amepata ujasiri kukuletea dua hii. 287:28 Kut 34:6; Yn 17:17Ee Bwana Mwenyezi, wewe ndiwe Mungu! Maneno yako ndiyo kweli, nawe umemwahidi mtumishi wako mambo haya mazuri. 297:29 Hes 6:23-27Sasa naomba uwe radhi kuibariki nyumba ya mtumishi wako, ili idumu mbele zako milele, kwa maana wewe, Ee Bwana Mwenyezi, umesema, na kwa baraka zako nyumba ya mtumishi wako itaendelea kubarikiwa milele.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 7:1-29

Lonjezo la Mulungu kwa Davide

1Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira, 2mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”

3Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”

4Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,

5“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo? 6Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti. 7Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’ ”

8“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli. 9Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi. 10Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja, 11monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse.

“ ‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako: 12Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake. 13Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. 14Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu. 15Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu. 16Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’ ”

17Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.

Pemphero la Davide

18Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati:

“Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?” 19Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?

20Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu. 21Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.

22Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu. 23Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto? 24Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.

25“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera, 26kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.

27“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere. 28Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu. 29Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”