1 Wakorintho 13 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

1 Wakorintho 13:1-13

Karama Ya Upendo

113:1 Mk 16:17; 1Kor 13:8Hata kama nitasema kwa lugha za wanadamu na za malaika, kama sina upendo, nimekuwa kengele inayolialia au toazi livumalo. 213:2 Efe 4:11; Mdo 11:27; 1Kor 14:2; 2Kor 8:7; 1Kor 12:9; Mt 17:20; 21:21Ningekuwa na karama ya unabii na kujua siri zote na maarifa yote, hata kama nina imani kiasi cha kuweza kuhamisha milima, kama sina upendo, mimi si kitu. 313:3 Lk 19:8; Mdo 2:45; Dan 3:28Kama nikitoa mali yote niliyo nayo na kama nikijitolea mwili wangu uchomwe moto, kama sina upendo, hainifaidi kitu.

413:4 1The 5:14; 1Kor 5:2Upendo huvumilia, upendo hufadhili, upendo hauoni wivu, hauna majivuno, hauna kiburi. 513:5 1Kor 10:24; Mt 5:22; Ay 14:16-17; Mit 10:12; 7:19; 1Pet 4:8Haukosi kuwa na adabu, hautafuti mambo yake, haukasiriki upesi, hauweki kumbukumbu ya mabaya. 613:6 2The 2:12; 2Yn 4; 1:3-4Upendo haufurahii mabaya bali hufurahi pamoja na kweli. 713:7 1Kor 13:8, 13; Mit 10:12; 1Kor 9:12; Rum 15:1Upendo huvumilia yote, huamini yote, hutumaini yote, hustahimili yote.

813:8 1Kor 13:2; 1Pet 4:8Upendo haushindwi kamwe. Lakini ukiwepo unabii, utakoma; zikiwepo lugha, zitakoma; yakiwepo maarifa, yatapita. 913:9 1Kor 8:2Kwa maana tunafahamu kwa sehemu na tunatoa unabii kwa sehemu. 1013:10 Flp 3:12Lakini ukamilifu ukija, yale yasiyo kamili hutoweka. 1113:11 Za 131:2Nilipokuwa mtoto, nilisema kama mtoto, niliwaza kama mtoto, nilifikiri kama mtoto. Nilipokuwa mtu mzima niliacha mambo ya kitoto. 1213:12 Ay 26:14; 36:26; Mwa 32:30; Ay 19:26; 1Yn 3:2; 1Kor 8:2; 8:3; Gal 4:9Kwa maana sasa tunaona taswira kama kwa kioo, lakini wakati huo tutaona wazi. Sasa nafahamu kwa sehemu, wakati huo nitafahamu kikamilifu, kama vile mimi ninavyofahamika kikamilifu.

1313:13 Rum 5:2-5; Gal 5:5-6; Efe 4:25; Kol 1:4-5; 1The 1:3; Ebr 6:10-12; Mt 22:37-40; 1Kor 16:14; Gal 5:6; 1Yn 4:7-12, 16Basi sasa, yanadumu mambo haya matatu: Imani, tumaini na upendo. Lakini lililo kuu miongoni mwa haya matatu ni upendo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 13:1-13

Kupambana kwa Chikondi

1Ngakhale nditamayankhula mʼmalilime a anthu ndi a angelo, koma ngati ndilibe chikondi, ndili ngati chinganga chaphokoso kapena ngati chitsulo chosokosera. 2Ngati ndili ndi mphatso ya uneneri, nʼkumazindikira zinsinsi ndi kudziwa zonse, ndipo ngati ndili ndi chikhulupiriro chosuntha mapiri, koma wopanda chikondi, ine sindili kanthu. 3Ngati ndipereka zanga zonse kwa osauka ndi kupereka thupi langa kuti alitenthe, koma ngati ndilibe chikondi, ine sindipindula kanthu.

4Chikondi nʼcholeza mtima, chikondi nʼchokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira. 5Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa. 6Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi. 7Chimatchinjiriza nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira nthawi zonse.

8Chikondi ndi chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha. 9Pakuti timadziwa zinthu pangʼono chabe ndipo timanenera pangʼono chabe. 10Koma changwiro chikadzaoneka ndipo chopereweracho chidzatha. 11Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya. 12Pakuti tsopano tiona zinthu mosaoneka bwino ngati mʼgalasi loonera; kenaka tidzaziona maso ndi maso. Tsopano ndidziwa mosakwanira koma kenaka ndidzadziwa mokwanira, monga mmene Mulungu akundidziwira ine.

13Ndipo tsopano zatsala zinthu zitatu: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.