ዘዳግም 32 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ዘዳግም 32:1-52

1ሰማያት ሆይ፤ አድምጡ፤ እኔም እናገራለሁ፤

ምድር ሆይ፤ አንቺም የአፌን ቃል ስሚ።

2ትምህርቴ እንደ ዝናብ ትውረድ፤

ቃሌም እንደ ጤዛ ይንጠባጠብ፤

በቡቃያ ሣር ላይ እንደ ካፊያ፣

ለጋ ተክልም ላይ እንደ ከባድ ዝናብ ይውረድ።

3እኔ የእግዚአብሔርን (ያህዌ) ስም ዐውጃለሁ፤

የአምላካችንን (ኤሎሂም) ታላቅነት አወድሱ!

4እርሱ ዐለት፣ ሥራውም ፍጹም ነው፤

መንገዱም ሁሉ ትክክል ነው፤

የማይሳሳት ታማኝ አምላክ፣

ቀጥተኛና ጻድቅ አምላክም እርሱ ነው።

5በእርሱ ላይ ክፋት ፈጽመዋል፤ ከነውራቸው የተነሣ ከእንግዲህ ልጆቹ አይደሉም፤

ወልጋዳና ጠማማ ትውልዶች ናቸው32፥5 ወይም የተጣመሙት እነርሱ እንጂ የእርሱ ልጆች አይደሉም

6አንተ ተላላና ጥበብ የጐደለህ ሕዝብ፣

ለእግዚአብሔር (ለያህዌ) የምትመልስለት በዚህ መንገድ ነውን?

አባትህ ፈጣሪህ32፥6 ወይም ያወጣህ አባትህ።

የሠራህና ያበጀህ እርሱ አይደለምን?

7የጥንቱን ዘመን አስታውስ፤

አባትህን ጠይቅ፤ ይነግርሃልም፤

ሽማግሌዎችህንም ጠይቅ፤ ያስረዱሃል።

8ልዑል ለአሕዛብ ርስታቸውን በሰጠ ጊዜ፣

የሰውንም ዘር በለያየ ጊዜ፣

በእስራኤል ልጆች32፥8 የማሶሬቱ ቅጅ፣ የሙት ባሕር ጥቅልል እንዲሁም የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም፣ የእግዚአብሔር ልጆች ይላሉ። ቍጥር ልክ፣

የአሕዛብን ርስት ድንበር ለየ፤

9የእግዚአብሔር (ያህዌ) ድርሻ የገዛ ሕዝቡ፣

ያዕቆብ የተለየ ርስቱ ነውና።

10እርሱን በምድረ በዳ፣

ባዶና ጭው ባለ በረሓ ውስጥ አገኘው፤

ጋሻ ሆነው፤ ተጠነቀቀለትም፤

እንደ ዐይኑ ብሌን ጠበቀው።

11ንስር ጐጆዋን በትና፣

በጫጩቶቿም ላይ እንደምትረብብ፣

እነርሱን ለመያዝ ክንፎቿን እንደምትዘረጋ፣

በክንፎቿም እንደምትሸከማቸው፣

12እግዚአብሔር (ያህዌ) ብቻ መራው፤

ምንም ባዕድ አምላክ አብሮት አልነበረም።

13በምድር ከፍታ ላይ አወጣው፤

የዕርሻንም ፍሬ መገበው፤

ከዐለት ድንጋይ ማር አበላው፤

ከባልጩትም ድንጋይ ዘይት መገበው።

14የላሙንና የበጉን መንጋ ቅቤና ወተት፣

የሰቡትን በጎችና ፍየሎች፣

የባሳንን ምርጥ አውራ በግ፣

መልካም የሆነውንም ስንዴ፣

ማለፊያውንም የወይን ጠጅ።

15ይሹሩን32፥15 ይሹሩን ማለት ቅን ወይም ትክክለኛ ማለት ሲሆን፣ ይኸውም እስራኤልን የሚያሳይ ነው። ወፈረ፤ ረገጠ፤

ጠገበ፤ ሰውነቱ ደነደነ፤ ለሰለሰ፤

የፈጠረውንም አምላክ (ኤሎሂም) ተወ፤

መጠጊያ ዐለት የሆነውን አዳኙንም ናቀ።

16በባዕዳን አማልክታቸው አስቀኑት፤

በአጸያፊ ጣዖቶቻቸውም አስቈጡት።

17አምላክ ላልሆኑ አጋንንት፦

ላላወቋቸው አማልክት፣

ከጊዜ በኋላ ለተነሡ አማልክት፣

አባቶቻችሁ ላልፈሯቸው አማልክት ሠዉ።

18አባት የሆነህን ዐለት ከዳኸው፤

የወለደህን አምላክ ረሳኸው።

19እግዚአብሔር (ያህዌ) ይህን አይቶ ናቃቸው፤

በወንድና በሴት ልጆቹ ተቈጥቷልና።

20እርሱም፣ “ፊቴን ከእነርሱ እሰውራለሁ፤

መጨረሻቸው ምን እንደሚሆንም አያለሁ” አለ፤

ጠማማ ትውልድ፣

የማይታመኑም ልጆች ናቸውና።

21አምላክ ባልሆነው አስቀኑኝ፤

በከንቱ ጣዖቶቻቸው አስቈጡኝ።

እኔም ሕዝብ ባልሆነው አስቀናቸዋለሁ።

በማያስተውልም ሕዝብ አስቈጣቸዋለሁ።

22በቍጣዬ እሳት ተቀጣጥሏልና፤

እርሱ እስከ ሲኦል ዘልቆ ይነድዳል።

ምድርን እስከ ሰብሏ ይበላል፤

የተራሮችንም መሠረት ያቀጣጥላል።

23“በመዓት ላይ መዓት አመጣባቸዋለሁ።

ፍላጻዬንም በእነርሱ ላይ እጨርሳለሁ።

24የሚያጠፋ ራብ፣ በልቶ የሚጨርስ ቸነፈርና ከባድ

መቅሠፍት እሰድድባቸዋለሁ፤

የአራዊትን ሹል ጥርስ፣ በምድር የሚሳብ የእባብ መርዝም

እሰድድባቸዋለሁ።

25ሰይፍ መንገድ ላይ ያስቀራቸዋል፤

ቤታቸውም ውስጥ ድንጋጤ ይነግሣል፤

ጕልማሳውና ልጃገረዷ፣

ሕፃኑና ሽማግሌው ይጠፋሉ።

26እበትናቸዋለሁ፤ ከሰዎችም መካከል መታሰቢያቸውን

አጠፋለሁ አልሁ፤

27ነገር ግን ጠላቶቻቸው እንዳይታበዩ፣

‘ድል ያደረገችው እጃችን እንጂ፣

እግዚአብሔር (ያህዌ) ይህን ሁሉ አላደረገም’ እንዳይሉ፣

የጠላትን መነሣሣት ሠጋሁ።”

28አእምሮ የጐደላቸው፣

ማስተዋልም የሌላቸው ናቸው።

29አስተዋዮች ቢሆኑ ኖሮ ይህን በተገነዘቡ፣

መጨረሻቸውም ምን እንደሚሆን ባስተዋሉ ነበር።

30መጠጊያ ዐለታቸው ካልሸጣቸው፣

እግዚአብሔር (ያህዌ) ካልተዋቸው በቀር፣

አንድ ሰው እንዴት ሺሑን ያሳድዳል?

ሁለቱስ እንዴት ዐሥር ሺሑን እንዲሸሹ ያደርጋሉ?

31የእነርሱ መጠጊያ ዐለት እንደ እኛ መጠጊያ

ዐለት አይደለምና፤ ጠላቶቻችንም እንኳ ይህን አይክዱም።

32ወይናቸው ከሰዶም ወይን፣

ከገሞራም ዕርሻ ይመጣል፤

የወይናቸው ፍሬ በመርዝ፣

ዘለላቸውም በምሬት የተሞላ ነው።

33ወይናቸው የእባብ መርዝ፣

የመራዥ እባብም መርዝ ነው።

34“ይህ በእኔ ዘንድ ተጠብቆ ያለ፣

በመዝገቤስ የታተመ አይደለምን?

35በቀል የእኔ ነው፤ እኔ ብድራትን እመልሳለሁ፤

ጊዜው ሲደርስ እግራቸው ይሰናከላል፤

የመጥፊያቸው ቀን ቀርቧል፤

የሚመጣባቸውም ፍርድ ፈጥኖባቸዋል።”

36ኀይላቸው መድከሙን፣

ባሪያም ሆነ ነጻ ሰው አለመቅረቱን በሚያይበት ጊዜ፣

እግዚአብሔር (ያህዌ) ለሕዝቡ ይፈርዳል፤

ለአገልጋዮቹም ይራራል።

37እንዲህም ይላል፤ “መጠጊያ ዐለት የሆኗቸው፣

እነዚያ አማልክታቸው የት አሉ?

38የመሥዋዕታቸውን ሥብ የበሉ፣

የመጠጥ ቍርባናቸውንም የወይን ጠጅ የጠጡ አማልክት ወዴት ናቸው?

እስቲ ይነሡና ይርዷችሁ!

እስቲ መጠለያ ይስጧችሁ!

39“እኔ ራሴ እርሱ እንደ ሆንሁ እዩ፤

ከእኔም በቀር ሌላ አምላክ የለም፤

እገድላለሁ፤ አድናለሁም፤

አቈስላለሁ፤ እፈውሳለሁም፤

ከእጄም የሚያስጥል ማንም የለም።

40እጄን ወደ ሰማይ አነሣለሁ፤

ለዘላለምም ሕያው እንደ ሆንሁ እናገራለሁ፤

41የሚያብረቀርቅ ሰይፌን ስዬ፣

እጄ ለፍርድ ስትይዘው፣

ባላጋራዎቼን እበቀላቸዋለሁ፤

የሚጠሉኝንም እንደ ሥራቸው እከፍላቸዋለሁ።

42ሰይፌ ሥጋ በሚበላበት ጊዜ፣

ፍላጾቼ በደም እንዲሰክሩ አደርጋለሁ፤

ደሙ የታረዱትና የምርኮኞች፣

የጠላት አለቆችም ራስ ደም ነው።”

43አሕዛብ ሆይ፤ ከሕዝቡ ጋር ደስ ይበላችሁ32፥43 ወይም፣ ሕዝቦች ሆይ፤ ደስ ይበላችሁ።32፥43 የማሶሬቱ ቅጅ፣ የሙት ባሕር ጥቅልል እንዲሁም የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም፣ ሕዝቦች ሆይ፤ መላእክት ሁሉ ለእርሱ ይስገዱ ይላሉ።

እርሱ የአገልጋዮቹን ደም ይመልሳል፤

ጠላቶቹንም ይበቀላል።

ምድሪቱንና ሕዝቡን ይቤዣቸዋልና።

44ሙሴም ከነዌ ልጅ ከኢያሱ ጋር መጥቶ የዚህን መዝሙር ቃሎች በሕዝቡ ጆሮ ተናገረ። 45ሙሴም እነዚህን ቃሎች ሁሉ ለመላው እስራኤል ተናግሮ ከጨረሰ በኋላ፣ 46እንዲህ አላቸው፤ የዚህን ሕግ ቃሎች ሁሉ በጥንቃቄ ይጠብቁ ዘንድ ልጆቻችሁን እንድታዝዟቸው፣ እኔ ዛሬ በግልጥ የምነግራችሁን ቃሎች ሁሉ በልባችሁ አኑሩ። 47ቃሎቹ ለእናንተ ሕይወታችሁ እንጂ እንዲሁ ባዶ ቃሎች አይደሉም፤ በእነርሱ ዮርዳኖስን ተሻግራችሁ፣ በምትወርሷትም ምድር ረዥም ዘመን ትኖራላችሁ።

ሙሴ በናባው ተራራ ላይ መሞቱ

48በዚያችም ዕለት እግዚአብሔር (ያህዌ) ሙሴን እንዲህ አለው፤ 49“ከኢያሪኮ ማዶ ባለው የሞዓብ ምድር፣ ከዓባሪም ተራሮች አንዱ ወደ ሆነው ወደ ናባው ተራራ ወጥተህ ለእስራኤላውያን ርስት አድርጌ የምሰጣትን የከነዓንን ምድር አሻግረህ ተመልከት። 50ወንድምህ አሮን በሖር ተራራ ላይ እንደ ሞተና ወደ ወገኖቹ እንደ ተሰበሰበ ሁሉ፣ አንተም በወጣህበት በዚያ ተራራ ላይ ሙት፤ ወደ ወገኖችህም ተሰብሰብ። 51ይህ የሚሆንበት ምክንያት ሁለታችሁም በጺን ምድረ በዳ፣ በቃዴስ በመሪባ ውሃ አጠገብ በእኔ ላይ መታመናችሁን በእስራኤላውያን ፊት ስላጐደላችሁና ቅድስናዬንም በእስራኤላውያን መካከል ስላላከበራችሁ ነው። 52ስለዚህ ምድሪቱን ከሩቅ ሆነህ ታያታለህ እንጂ፣ ለእስራኤል ሕዝብ ወደምሰጣት ምድር አትገባም።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 32:1-52

1Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;

imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.

2Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula

ndipo mawu anga atsike ngati mame,

ngati mvumbi pa udzu watsopano,

ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.

3Ndidzalalikira dzina la Yehova.

Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!

4Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,

njira zake zonse ndi zolungama.

Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,

Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.

5Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,

iwo si ana akenso,

koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.

6Kodi mukumubwezera Yehova chotere,

inu anthu opusa ndi opanda nzeru?

Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,

amene anakupangani ndi kukuwumbani?

7Kumbukirani masiku amakedzana;

ganizirani za mibado yakalekale.

Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,

akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.

8Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,

pamene analekanitsa anthu onse,

anayikira malire anthu onse

molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.

9Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,

Yakobo ndiye cholowa chake.

10Anamupeza mʼchipululu,

ku malo owuma ndi kopanda kanthu.

Anamuteteza ndi kumusamalira;

anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,

11ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake

nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,

chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo

ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.

12Yehova yekha ndiye anamutsogolera;

popanda thandizo la mulungu wachilendo.

13Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko

ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.

Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,

ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,

14pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,

ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,

pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani

ndiponso tirigu wabwino kwambiri.

Munamwa vinyo wa thovu lofiira.

15Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;

atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.

Anasiya Mulungu amene anamulenga

ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.

16Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo

ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.

17Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,

milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,

milungu yongobwera kumene,

milungu imene makolo anu sankayiopa.

18Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;

munayiwala Mulungu amene anakubalani.

19Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana

chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.

20Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,

ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani;

pakuti ndi mʼbado wopotoka,

ana amene ndi osakhulupirika.

21Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu

ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe.

Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake;

ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.

22Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,

umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa.

Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake

ndipo udzapsereza maziko a mapiri.

23“Ndidzawawunjikira masautso

ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.

24Ndidzawatumizira njala yoopsa,

malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo;

ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta,

ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.

25Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;

mantha adzalamulira nyumba zawo.

Anyamata ndi atsikana adzafa,

ngakhalenso makanda ndi okalamba.

26Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza

ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,

27koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,

mwina adani anga sadzandimvetsetsa

ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife;

Yehova sanachite zonsezi.’ ”

28Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,

iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.

29Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi

ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!

30Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000

kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse,

Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa,

Yehova akanapanda kuwataya?

31Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,

ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.

32Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu

ndiponso ku minda ya ku Gomora.

Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha

ndipo maphava ake ndi owawa.

33Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,

ululu woopsa wa mphiri.

34“Kodi zimenezi sindinazisunge

ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?

35Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.

Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera;

tsiku lawo la masautso layandikira

ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”

36Yehova adzaweruza anthu ake

ndipo adzachitira atumiki ake chifundo

pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha

ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.

37Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,

thanthwe limene ankabisalamo,

38milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo

ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?”

Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni!

Ibwere kuti idzakutetezenitu!

39“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!

Palibe mulungu wina koma Ine ndekha.

Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo,

ndavulaza ndipo ndidzachiritsa,

ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.

40Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,

‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,

41pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira

ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,

ndidzabwezera chilango adani anga

ndi kulanga onse odana nane.

42Mivi yanga idzakhuta magazi awo

pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:

magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,

mitu ya atsogoleri a adani.’ ”

43Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,

pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;

adzabwezera chilango adani ake

ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.

44Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”

Mose Adzafera pa Phiri la Nebo

48Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”