ኤርምያስ 18 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኤርምያስ 18:1-23

በሸክላ ሠሪው ቤት

1ከእግዚአብሔር ወደ ኤርምያስ እንዲህ የሚል ቃል መጣ፦ 2“ተነሥተህ ወደ ሸክላ ሠሪው ቤት ውረድ፤ በዚያ መልእክቴን እሰጥሃለሁ።” 3እኔም ወደ ሸክላ ሠሪው ቤት ወረድሁ፤ ሸክላውንም በመንኰራኵር ላይ ይሠራ ነበር። 4ከጭቃ ይሠራው የነበረውም ሸክላ በእጁ ላይ ተበላሸ፤ ሸክላ ሠሪውም በሚፈልገው ሌላ ቅርጽ መልሶ አበጀው።

5የእግዚአብሔርም ቃል ወደ እኔ እንዲህ ሲል መጣ፤ 6“የእስራኤል ቤት ሆይ፤ ሸክላ ሠሪው እንደሚሠራው፣ እኔ በእናንተ ላይ መሥራት አይቻለኝምን?” ይላል እግዚአብሔር፤ “የእስራኤል ቤት ሆይ፤ ጭቃው በሸክላ ሠሪው እጅ እንዳለ፣ እናንተም እንዲሁ በእጄ ውስጥ ናችሁ። 7አንድ ሕዝብ ወይም መንግሥት እንዲነቀል፣ እንዲፈርስና እንዲጠፋ በተናገርሁ ጊዜ፣ 8ያስጠነቀቅሁት ሕዝብ ከክፋቱ ቢመለስ፣ እኔ ላደርስበት ያሰብሁትን ክፉ ነገር እተዋለሁ። 9በሌላም ጊዜ አንድን ሕዝብ ወይም መንግሥት አንጸውና እተክለው ዘንድ ተናግሬ፣ 10በፊቴ ክፉ ነገር ቢያደርግና ባይታዘዘኝ፣ አደርግለታለሁ ብዬ ያሰብሁትን መልካም ነገር አስቀርበታለሁ።

11“አሁንም እንግዲህ ለይሁዳ ሕዝብና በኢየሩሳሌም ለሚኖሩ እንዲህ በላቸው፤ ‘እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤ “እነሆ፤ ጥፋትን እያዘጋጀሁላችሁ ነው፤ ክፋትንም እየጠነሰስሁላችሁ ነው። ስለዚህ ሁላችሁ ከክፉ መንገዳችሁ ተመለሱ፤ መንገዳችሁንና ተግባራችሁን አቅኑ።” ’ 12እነርሱ ግን፣ ‘በከንቱ አትድከም፤ ባቀድነው እንገፋበታለን፤ እያንዳንዳችንም የክፉ ልባችንን እልኸኝነት እንከተላለን’ ይላሉ።”

13ስለዚህ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“እስቲ አሕዛብን፣

‘እንዲህ ዐይነት ነገር በመካከላችሁ ተሰምቶ ያውቃል?’ ብላችሁ ጠይቁ።

ድንግሊቱ እስራኤል፣

እጅግ ክፉ ነገር አድርጋለች።

14የሊባኖስ ተራራ ድንጋያማ ተረተር፣

በረዶ ተለይቶት ያውቃልን?

ከጋራው የሚወርደውስ ቀዝቃዛ ውሃ፤

መፍሰሱን ያቋርጣልን?18፥14 በዕብራይስጡ የዚህ ዐረፍተ ነገር ትርጕም በግልጽ አይታወቅም።

15ሕዝቤ ግን ረስቶኛል፤

ለማይረቡ ነገሮች ዐጥኗል፣

በራሱ መንገድ፣

በቀደሞው ጐዳና ተሰናክሏል፤

በሻካራው መሄጃ፣

ባልቀናውም ጥርጊያ መንገድ ሄዷል።

16ምድራቸው ባድማ፣

ለዘላለም መሣለቂያ ይሆናል፤

በዚያ የሚያልፍ ሁሉ ይደነቃል፤

በመገረምም ራሱን ይነቀንቃል።

17ከምሥራቅ እንደሚወጣ ነፋስ፣

በጠላቶቻቸው ፊት እበትናቸዋለሁ፤

በመጥፊያቸው ቀን፣

ጀርባዬን እንጂ ፊቴን አላሳያቸውም።”

18እነርሱም፣ “ሕግ ከካህናት፣ ምክር ከጠቢባን፣ ቃልም ከነቢያት ስለማይታጣ ኑና በኤርምያስ ላይ እንማከር፤ ኑ፤ በአንደበታችን እናጥቃው፣ እርሱ የሚናገረውንም ሁሉ አንስማ” አሉ።

19እግዚአብሔር ሆይ፤ ስማኝ፤

ባላንጣዎቼ የሚሉትን አድምጥ።

20የመልካም ተግባር ወሮታው ክፉ ነውን?

እነርሱ ግን ጕድጓድ ቈፈሩልኝ፤

ቍጣህን ከእነርሱ እንድትመልስ፣

በፊትህ ቆሜ፣

ስለ እነርሱ እንደ ተናገርሁ ዐስብ።

21ስለዚህ ልጆቻቸውን ለራብ፣

ለሰይፍም ስለት አሳልፈህ ስጥ፤

ሚስቶቻቸው የወላድ መካን፣ መበለትም ይሁኑ፤

ወንዶቻቸው በሞት ይቀሠፉ፤

ጕልማሶቻቸው በጦር ሜዳ ለሰይፍ ይዳረጉ።

22ሊይዙኝ ጕድጓድ ስለ ቈፈሩ፣

ለእግሮቼም በስውር ወጥመድ ስለ ዘረጉ፣

በድንገት ወራሪ ስታመጣባቸው፣

ከቤታቸው ጩኸት ይሰማ።

23አንተ ግን እግዚአብሔር ሆይ፤

ሊገድሉኝ ያሤሩብኝን ሤራ ሁሉ ታውቃለህ፤

በደላቸውን ይቅር አትበል፤

ኀጢአታቸውንም ከፊትህ አትደምስስ፤

በፊትህ ወድቀው የተጣሉ ይሁኑ፤

በቍጣህም ጊዜ አትማራቸው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 18:1-23

Ku Nyumba ya Wowumba Mbiya

1Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.” 3Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero. 4Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

5Kenaka Yehova anandiwuza kuti, 6“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya. 7Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga, 8ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira. 9Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu. 10Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.

11“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’ 12Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’ ”

13Yehova akuti,

“Uwafunse anthu a mitundu ina kuti:

Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi?

Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita

chinthu choopsa kwambiri.

14Kodi chisanu chimatha pa matanthwe

otsetsereka a phiri la Lebanoni?

Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera

ku phiri la Lebanoni adzamphwa?

15Komatu anthu anga andiyiwala;

akufukiza lubani kwa mafano achabechabe.

Amapunthwa mʼnjira

zawo zakale.

Amayenda mʼnjira zachidule

ndi kusiya njira zabwino.

16Dziko lawo amalisandutsa chipululu,

chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse;

onse odutsapo adzadabwa kwambiri

ndipo adzapukusa mitu yawo.

17Ngati mphepo yochokera kummawa,

ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo;

ndidzawafulatira osawathandiza

pa tsiku la mavuto awo.”

18Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”

19Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni;

imvani zimene adani anga akunena za ine!

20Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino?

Komabe iwo andikumbira dzenje.

Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu

kudzawapempherera

kuti muwachotsere mkwiyo wanu.

21Choncho langani ana awo ndi njala;

aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga.

Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye;

amuna awo aphedwe ndi mliri,

anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.

22Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo

mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe.

Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo

ndipo atchera msampha mapazi anga.

23Koma Inu Yehova, mukudziwa

ziwembu zawo zonse zofuna kundipha.

Musawakhululukire zolakwa zawo

kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu.

Agonjetsedwe pamaso panu;

muwalange muli wokwiya.”