ኢዮብ 41 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 41:1-34

1“ሌዋታንን41፥1 ምናልባት ዐዞ ሊሆን ይችላል። በመንጠቆ ልታወጣው፣

ወይም ምላሱን በገመድ ልታስረው ትችላለህን?

2መሰነጊያ በአፍንጫው ልታስገባ፣

ወይም ጕንጩን በሜንጦ ልትበሳ ትችላለህን?

3እርሱ እንድትምረው ይለማመጥሃል?

በለስላሳ ቃላትስ ይናገርሃል?

4ለዘላለም ባሪያ ታደርገው ዘንድ፣

ከአንተ ጋር ይዋዋላልን?

5እንደ ወፍ አልምደኸው ከእርሱ ጋር ልትጫወት ትችላለህ?

ወይስ ለሴት አገልጋዮችህ መጫወቻነት ታስረዋለህን?

6ነጋዴዎችስ በእርሱ ላይ ይከራከራሉን?

ለቸርቻሪዎችስ ያከፋፍሉታል?

7ቈዳው ላይ ዐንካሴ ልትሰካ፣

ጭንቅላቱንም በዓሣ መውጊያ ጦር ልትበሳ ትችላለህን?

8እርሱን እስቲ ንካው፣

ግብግቡን ታስታውሳለህ፤ ከቶም አያላምድህም።

9እርሱን በቍጥጥር ሥር አውላለሁ ማለት ዘበት ነው፤

በዐይን ማየት እንኳ ብርክ ያስይዛል።

10ሊቀሰቅሰው የሚደፍር የለም፤

ማን ፊቱ ሊቆም ይችላል?

11ነክቶት በሰላም የሚሄድ ማን ነው?

ከሰማይ በታች ማንም የለም።41፥11 አንዳንድ ትርጕሞች፣ በዕዳ የሚጠይቀኝ ማን ነው? ከሰማይ በታች ያለው ሁሉ ንብረቴ ነው ይላሉ።

12“ስለ ብርታቱና ስለ አካላቱ ውበት፣

ስለ እጅና እግሩ ከመናገር አልቈጠብም።

13የደረበውን ልብስ ማን ሊያወልቅ ይችላል?

ማንስ ሊለጕመው ወደ መንጋጋው ይቀርባል?

14አስፈሪ ጥርሶቹ የተገጠገጡበትን፣

የአፉን ደጅ ማን ደፍሮ ይከፍታል?

15ጀርባው፣ አንድ ላይ የተጣበቁ፣

የጋሻ ረድፎች አሉት፤

16እጅግ የተቀራረቡ ስለሆኑ፣

ነፋስ በመካከላቸው አያልፍም፤

17እርስ በርስ የተገጣጠሙ ናቸው፤

አንዱ ከአንዱ ጋር ተጣብቋልና ማንም ሊለያያቸው አይችልም።

18እንጥሽታው የብርሃን ብልጭታ ያወጣል፤

ዐይኖቹም እንደ ማለዳ ጮራ ናቸው።

19ከአፉ ፍም ይወጣል፤

የእሳት ትንታግ ይረጫል።

20በሸንበቆ ማገዶ ላይ ከተጣደ ድስት እንደሚወጣ እንፋሎት፣

ከአፍንጫው ጢስ ይትጐለጐላል።

21እስትንፋሱ ከሰል ያቀጣጥላል፤

የእሳትም ነበልባል ከአፉ ይወጣል።

22ብርታት በዐንገቱ ውስጥ አለ፤

አሸባሪነትም በፊቱ እመር እመር ይላል።

23የሥጋው ንብርብር እርስ በርስ የተጣበቀ፣

በላዩ የጸናና ከቦታው የማይናጋ ነው።

24ደረቱ እንደ ዐለት የጠጠረ፣

እንደ ወፍጮ ድንጋይም የጠነከረ ነው።

25እርሱ በተነሣ ጊዜ፣ ኀያላን ይርዳሉ፤

በሚንቀሳቀስበትም ጊዜ ወደ ኋላ ያፈገፍጋሉ።

26ጦር፣ ፍላጻ ወይም ዐንካሴ፣

ሰይፍም ቢያገኘው አንዳች አይጐዳውም።

27እርሱ ብረትን እንደ አገዳ፣

ናስንም እንደ ነቀዘ ዕንጨት ይቈጥራል።

28ቀስት አያባርረውም፤

የወንጭፍ ድንጋይም ለእርሱ እንደ ገለባ ነው።

29ቈመጥ በእርሱ ፊት እንደ ገለባ ነው፤

ጦር ሲሰበቅ ይሥቃል።

30የሆዱ ሥር እንደ ሸካራ ገል ነው፤

እንደ መውቂያ መሣሪያም በጭቃ ላይ ምልክት ጥሎ ያልፋል።

31እንደሚፈላ ምንቸት ጥልቁን ያናውጠዋል፤

ባሕሩንም እንደ ሽቶ ብልቃጥ ያደርገዋል።

32ያለፈበትን መንገድ ብሩህ ያደርጋል፤

ቀላዩንም ሽበት ያወጣ ያስመስለዋል።

33ያለ ፍርሀት የተፈጠረ፣

እንደ እርሱ ያለ በምድር ላይ የለም።

34ከፍ ያሉትን ሁሉ በንቀት ይመለከታል፤

በትዕቢተኞችም ሁሉ ላይ ንጉሥ ነው።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 41:1-34

1“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba

kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?

2Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake,

kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?

3Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo?

Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?

4Kodi idzachita nawe mgwirizano

kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?

5Kodi udzasewera nayo ngati mbalame,

kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?

6Kodi anthu adzayitsatsa malonda?

Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?

7Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga,

kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?

8Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo,

ndipo iweyo sudzabwereranso.

9Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza;

kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.

10Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa.

Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?

11Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere?

Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.

12“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho,

za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.

13Ndani angasende chikopa chake?

Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?

14Ndani angatsekule kukamwa kwake,

pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?

15Kumsana kwake kuli mizere ya mamba

onga zishango zolumikizanalumikizana;

16Mambawo ndi olukanalukana

kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.

17Ndi olumikizanalumikizana;

ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.

18Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali;

maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.

19Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo

mumathetheka mbaliwali zamoto.

20Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi

ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.

21Mpweya wake umayatsa makala,

ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.

22Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake;

aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.

23Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo

ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.

24Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala,

ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.

25Ngʼonayo ikangovuwuka,

ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.

26Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu,

ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.

27Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe

ndi mkuwa ngati chikuni chowola.

28Muvi sungathe kuyithawitsa,

miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.

29Zibonga zimakhala ngati ziputu;

imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.

30Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo

imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.

31Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali,

imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.

32Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee,

kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.

33Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho,

nʼcholengedwa chopanda mantha.

34Chimanyoza nyama zina zonse;

icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”