እግዚአብሔር ተናገረ
1እግዚአብሔርም በዐውሎ ነፋስ ውስጥ ሆኖ ለኢዮብ መለሰለት፤ እንዲህም አለው፤
2“ዕውቀት በጐደለው ቃል፣
ዕቅዴን የሚያጨልም ይህ ማን ነው?
3እስቲ እንደ ወንድ ወገብህን ታጠቅ፤
እኔ ልጠይቅህ፣
አንተም መልስልኝ።
4“ምድርን በመሠረትሁ ጊዜ አንተ የት ነበርህ?
በርግጥ የምታስተውል ከሆንህ ንገረኝ።
5ካወቅህ፣ መጠኗን ለይቶ ማን ወሰነ?
በላይዋስ መለኪያ ገመድ የዘረጋ ማን ነው?
6መሠረቶቿ ምን ላይ ተተከሉ?
የማእዘን ድንጋይዋንስ ማን አቆመ?
7ይህም የሆነው የንጋት ከዋክብት በዘመሩበት ጊዜ፣
መላእክትም38፥7 ወይም፣ የእግዚአብሔር ልጆች እልል ባሉበት ጊዜ ነበር።
8“ባሕር ከማሕፀን በወጣ ጊዜ፣
በር የዘጋበት ማን ነው?
9ደመናውን ልብሱ፣
ጨለማንም መጠቅለያው አደረግሁለት፣
10ድንበር ወሰንሁለት፤
መዝጊያና መወርወሪያውን አበጀሁለት።
11‘እስከዚህ ድረስ ትመጣለህ፤ ማለፍ ግን አትችልም፤
የዕቡይ ማዕበልህም ገደብ ይህ ነው’ አልሁት።
12“ከተወለድህ ጀምሮ ንጋትን አዝዘህ ታውቃለህን?
ወይስ ወጋገን ስፍራውን እንዲይዝ አድርገሃል?
13በዚህም የምድርን ዳርቻ ይዞ፣
ክፉዎችን ከላይዋ እንዲያራግፍ አድርገሃልን?
14ምድር ከማኅተም በታች እንዳለ የሸክላ ጭቃ ቅርጿ ይወጣል፤
ቅርጿ እንደ ልብስ ቅርጽ ጐልቶ ይታያል።
15ክፉዎች ብርሃናቸውን ተከልክለዋል፤
ከፍ ያለው ክንዳቸውም ተሰብሯል።
16“ወደ ባሕር ምንጭ ወርደህ ታውቃለህን?
ወይስ ወደ ጥልቀቱ ገብተህ በመሠረቱ ላይ ተመላልሰሃልን?
17የሞት ደጆች ተገልጠውልሃልን?
የሞትንስ ጥላ በሮች አይተሃልን?
18የምድርን ስፋት ታውቃለህን?
ይህን ሁሉ ዐውቀህ ከሆነ፣ ንገረኝ።
19“ወደ ብርሃን መኖሪያ የሚያደርሰው መንገድ የትኛው ነው?
የጨለማ መኖሪያስ ወዴት ነው?
20ወደ ማደሪያቸው ልትወስዳቸው ትችላለህን?
የመኖሪያቸውን መንገድ ታውቃለህ?
21ያን ጊዜ ተወልደሃል! ዕድሜህ ትልቅ ነውና፣
አንተስ በርግጥ ሳታውቅ አትቀርም!
22“ወደ በረዶው መጋዘን ገብተሃልን?
የዐመዳዩንስ ማከማቻ አይተሃልን?
23ይኸውም ለመከራ ጊዜ፣
ለጦርነትና ለውጊያ ቀን ያስቀመጥሁት ነው።
24መብረቅ ወደሚሠራጭበት ቦታ የሚያደርሰው መንገድ፣
የምሥራቅም ነፋስ በምድር ላይ ወደሚበተንበት ስፍራ የሚወስደው የትኛው ነው?
25ለዝናብ መውረጃን፣
ለመብረቅም መንገድን ያበጀ ማን ነው?
26በዚህም ማንም የማይኖርበትን ምድር፣
ሰውም የሌለበትን ምድረ በዳ የሚያጠጣ፣
27ባድማውንና በረሓውን መሬት የሚያጠግብ፣
ሣርም እንዲበቅልበት የሚያደርግ ማን ነው?
28ዝናብ አባት አለውን?
የጤዛን ጠብታ ማን ወለደው?
29በረዶ ከማን ማሕፀን ይወጣል?
የሰማዩንስ ዐመዳይ ማን ይወልዳል?
30ውሆች እንደ ድንጋይ ይጠነክራሉ፤
የጥልቁ ገጽ እንደ በረዶ ይጋገራል።
31“ፕልያዲስ የተባሉትን ውብ ከዋክብት ልትለጕም፣
ወይም የኦርዮንን ማሰሪያ ልትፈታ ትችላለህን?
32ማዛሮት የተባለውን የከዋክብት ክምችት በወቅቱ38፥32 ወይም በወቅቱ የሚወጣ የንጋት ኮከብ ልታወጣ፣
ወይም ድብ የተባለውን ኮከብና ልጆቹን ልትመራ ትችላለህ?
33የሰማያትን ሥርዐት ታውቃለህ?
ይህንስ በምድር ላይ እንዲሠለጥን ማድረግ ትችላለህ?
34“ድምፅህን ወደ ደመናት አንሥተህ፣
ራስህን በጐርፍ ማጥለቅለቅ ትችላለህን?
35መብረቆችን መስደድ ትችላለህ?
እነርሱስ፣ ‘እነሆ፤ እዚህ አለን’ ይሉሃል?
36ለልብ38፥36 በዕብራይስጡ የዚህ ቃል ትርጕም በትክክል አይታወቅም። ጥበብን፣
ለአእምሮም ማስተዋልን የሰጠ ማን ነው?
37ትቢያ ሲጠጥር፣
ጓሎችም እርስ በርስ ሲጣበቁ፣
38ደመናትን ለመቍጠር ጥበብ ያለው ማን ነው?
የሰማያትንስ የውሃ ገንቦ ዘንበል ማድረግ ማን ይችላል?
39“ለአንበሳዪቱ ዐድነህ ግዳይ ታመጣለህን?
የተራቡ የአንበሳ ግልገሎችንስ ታጠግባለህን?
40እነርሱ በዋሻ ውስጥ ያደባሉ፤
በደን ውስጥም ይጋደማሉ።
41ልጆቿ ወደ እግዚአብሔር ሲጮኹ፣
ምግብ ዐጥተው ሲንከራተቱ፣
ለቍራ መብልን የሚሰጥ ማን ነው?
Yehova Ayankhula
1Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga
poyankhula mawu opanda nzeru?
3Onetsa chamuna;
ndikufunsa
ndipo undiyankhe.
4“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi?
Ndiwuze ngati ukudziwa.
5Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa!
Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6Kodi maziko ake anawakumba potani,
kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi
ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa,
pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake
ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10pamene ndinayilembera malire ake
ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire
apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa,
kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi
ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo;
zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa,
ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja
kapena pa magwero ake ozama?
17Kodi anakuonetsapo zipata za imfa?
Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa?
Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti?
Nanga mdima umakhala kuti?
20Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi?
Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale!
Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana
kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23zimene ndazisungira nthawi ya mavuto
ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani
kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula,
nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu,
chipululu chopandamo munthu,
27kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa
ndi kumeretsamo udzu?
28Kodi mvula ili ndi abambo ake?
Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29Kodi madzi owundana anawabereka ndani?
Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala,
pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi?
Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake
kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa?
Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo
kuti igwetse mvula ya chigumula?
35Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime?
Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36Kodi ndani anayika nzeru mu mtima,
ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo?
Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38pamene fumbi limasanduka matope,
ndipo matopewo amawumbika?
39“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi
ndi kukhutitsa misona ya mikango
40pamene ili khale mʼmapanga mwawo
kapena pamene ikubisala pa tchire?
41Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani
pamene ana ake akulirira kwa Mulungu
ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?