ኢዮብ 24 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 24:1-25

1“ሁሉን የሚችል አምላክ ለምን የፍርድ ቀን አይወስንም?

እርሱን የሚያውቁትስ ለምን ያን ቀን እንዲያው ይጠባበቃሉ?

2ሰዎች ድንበር ይገፋሉ፤

የሰረቁትን መንጋ ያሰማራሉ።

3የድኻ ዐደጉን አህያ ቀምተው ይሄዳሉ፤

የመበለቲቱንም በሬ በመያዣነት ይወስዳሉ።

4ችግረኛውን ከመንገድ ያስወግዳሉ፤

የምድሪቱም ድኾች ይሸሸጋሉ።

5በምድረ በዳ እንዳሉ የሜዳ አህዮች፣

ድኾች ምግብ ፍለጋ ይራወጣሉ፤

ከበረሓው ምድር ለልጆቻቸው ምግብ ይሻሉ።

6ከሜዳ መኖ ይሰበስባሉ፤

ከክፉዎች የወይን ቦታም ይቃርማሉ።

7ዕራቍታቸውን ያለ ልብስ ያድራሉ፤

በብርድም ጊዜ የሚለብሱት የላቸውም።

8ከተራራ በሚወርድ ዝናብ በስብሰዋል፤

መጠለያ ዐጥተው ቋጥኝ ዐቅፈዋል።

9አባት የሌለው ልጅ ከዕቅፍ ተነጥቋል፤

የድኻውም ልጅ በዕዳ ተይዟል።

10ዕራቍታቸውን ያለ ልብስ ይሄዳሉ፤

ነዶ ይሸከማሉ፤ ግን ይራባሉ።

11በየተረተሩ24፥11 ወይም ከወፍጮዎች መካከል የወይራ ዘይት ማለት ነው፤ ሆኖም የዚህ ቃል የዕብራይስጡ ትርጕም በትክክል አይታወቅም። የወይራ ዘይት ያወጣሉ፤

ወይን እየጠመቁ፣ ራሳቸው ግን ይጠማሉ፤

12የሟቾች ጣር ጩኸት ከከተማዋ ይሰማል፤

የቈሰሉት ሰዎች ነፍስ ለርዳታ ይጮኻል፤

እግዚአብሔር ግን ተጠያቂዎቹን ዝም ብሏል።

13“በብርሃን ላይ የሚያምፁ፣

ጐዳናውን የማያውቁ፣

በመንገዱም የማይጸኑ አሉ።

14ቀኑ ሲመሽ፣ ነፍሰ ገዳይ ይነሣል፤

ድኾችንና ችግረኞችን ይገድላል፤

በሌሊትም እንደ ሌባ ያደባል፤

15አመንዝራ በዐይኑ ድንግዝግዝታን ይጠባበቃል፤

‘ማንም አያየኝም’ ብሎ ያስባል፤

ፊቱንም ይሸፍናል።

16በጨለማ፣ ቤት ሰርስረው ይገባሉ፤

በቀን ግን ይሸሸጋሉ፤

ብርሃንንም አይፈልጉም።

17ድቅድቅ ጨለማ ለሁላቸው እንደ ንጋት24፥17 ወይም ለእነርሱ ንጋት እንደ ሞት ጥላ ነው ነው፤

አሸባሪውን ጨለማ24፥17 ወይም ከሞት ጥላ ማለት ነው። ይወዳጃሉ።

18“ይሁን እንጂ፣ በውሃ ላይ የሚኵረፈረፍ ዐረፋ ናቸው፤

የወይን ቦታው ሰው የማይደርስበት፣

ርስታቸው ርጉም ነው።

19ድርቅና ሙቀት የቀለጠውን በረዶ ከቦታው እንደሚያስወግድ፣

ሲኦልም24፥19 አንዳንድ ቅጆች፣ መቃብር ይሉታል ኀጢአተኞችን ትነጥቃለች።

20የተሸከመቻቸው ማሕፀን ትረሳቸዋለች፤

ትል ይቦጠቡጣቸዋል፤

ክፉዎች እንደ ዛፍ ይሰበራሉ፤

የሚያስታውሳቸውም የለም።

21የማትወልደውን መካኒቱን ይቦጠቡጣሉ፤

ለመበለቲቱም አይራሩም።

22ነገር ግን እግዚአብሔር ብርቱዎችን በኀይሉ ጐትቶ ይጥላል፤

ቢደላደሉም የሕይወት ዋስትና የላቸውም።

23ያለ ሥጋት እንዲኖሩ ትቷቸው ይሆናል፤

ዐይኖቹ ግን በመንገዳቸው ላይ ናቸው።

24ለጥቂት ጊዜ ከፍ ከፍ ይላሉ፤ ሆኖም ይጠፋሉ፤

ዝቅ ዝቅ ብለው፤ እንደ ሌሎቹ ይከማቻሉ።

እንደ እህል ራስም ይታጨዳሉ።

25“ይህ እንዲህ ካልሆነማ፣ የሚያስተባብለኝ ማን ነው?

ቃሌን ከንቱ የሚያደርገውስ ማን ነው?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 24:1-25

1“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze?

Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?

2Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo;

amadyetsa ziweto zimene aba.

3Amalanda abulu a ana amasiye

ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.

4Amachotsa mʼmisewu anthu osauka,

ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.

5Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu,

amayendayenda kufuna chakudya;

dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.

6Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake,

ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.

7Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala;

pa nthawi yozizira amasowa chofunda.

8Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri

ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.

9Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere;

ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.

10Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala;

amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.

11Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa;

amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.

12Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda,

anthu ovulala akulirira chithandizo.

Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.

13“Pali ena amene amakana kuwala,

amene safuna kuyenda mʼkuwalako

kapena kukhala mʼnjira zake.

14Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka

ndipo amakapha osauka ndi amphawi;

nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.

15Munthu wachigololo amadikira chisisira;

iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’

ndipo amaphimba nkhope yake.

16Mbala zimathyola nyumba usiku,

koma masana zimadzitsekera;

izo zimathawa kuwala.

17Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera.

Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.

18“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi;

minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo

kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.

19Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana

ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa.

20Mayi wowabereka amawayiwala,

mphutsi zimasangalala powadya;

anthu oyipa sakumbukiridwanso

koma amathyoka ngati mtengo.

21Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana,

ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.

22Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake;

ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.

23Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka,

koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.

24Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso;

amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse;

amadulidwa ngati ngala za tirigu.

25“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza

ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”