ኢዮብ 23 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 23:1-17

ኢዮብ

1ኢዮብም እንዲህ ሲል መለሰ፤

2“ዛሬም ሐዘኔ መራራ ነው፤

እያቃሰትሁ እንኳ እጁ23፥2 በሰብዓ ሊቃናት ትርጕም፣ በሱርስትና በዕብራይስጡ ላይ፣ እጅ በላዬ ይላል። በላዬ ከብዳለች።

3እርሱን የት እንደማገኘው ባወቅሁ፤

ወደ መኖሪያውም መሄድ በቻልሁ!

4ጕዳዬን በፊቱ አቀርብ ነበር፤

አፌንም በሙግት እሞላው ነበር።

5የሚመልስልኝ ቃል ምን እንደ ሆነ ባወቅሁ ነበር፤

የሚለኝንም ባስተዋልሁ ነበር።

6በታላቅ ኀይሉ ከእኔ ጋር ይሟገት ይሆን?

አይደለም፤ ይልቁን ያደምጠኛል።

7ቅን ሰው ጕዳዩን በእርሱ ፊት ያቀርባል፤

እኔም ከፈራጄ ለዘላለም ነጻ እሆናለሁ።

8“ዳሩ ግን ወደ ምሥራቅ ብሄድ፣ በዚያ የለም፤

ወደ ምዕራብም ብሄድ፣ እርሱን አላገኘውም፤

9በሰሜን እየሠራ ሳለ አላየውም፤

ወደ ደቡብ በሚዞርበት ጊዜ ደብዛው አይገኝም።

10ግን እኔ የምሄድበትን መንገድ ያውቃል፤

ከፈተነኝም በኋላ እንደ ወርቅ እወጣለሁ።

11እግሮቼ ርምጃውን በጥብቅ ተከታትለዋል፤

ፈቀቅ ሳልል መንገዱን ጠብቄአለሁ።

12ከአፉ ከወጣው ትእዛዝ አልራቅሁም፣

የአንደበቱን ቃል ከዕለት እንጀራዬ አብልጬ ይዣለሁ።

13“እርሱ ግን ራሱን ችሎ ብቻውን የሚኖር ነው፤ የሚቋቋመውስ ማን ነው?

እርሱ የፈቀደውን ያደርጋል።

14በእኔ ላይ የወሰነውን ይፈጽማል፤

ይህን የመሰለ ዕቅድም ገና ብዙ አለው።

15በፊቱ የደነገጥሁትም ለዚህ ነው፤

ይህን ሁሉ ሳስብ እፈራለሁ።

16እግዚአብሔር ልቤን አባባው፤

ሁሉንም የሚችል አምላክ አስደነገጠኝ።

17ይህም ሆኖ ሳለ ጨለማው፣

ፊቴንም የጋረደው ጽልመት ልሳኔን አልዘጋውም።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.