ኢዮብ 21 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 21:1-34

ኢዮብ

1ኢዮብም እንዲህ ሲል መለሰ፤

2“ቃሌን በጥንቃቄ ስሙ፤

የምታጽናኑኝም በዚህ ይሁን፤

3ንግግሬን በትዕግሥት አድምጡ፤

ከተናገርሁ በኋላ፣ መሣለቅ ትችላላችሁ።

4“በውኑ ቅርታዬ በሰው ላይ ነውን?

ትዕግሥት ማጣትስ አይገባኝምን?

5ተመልከቱኝና ተገረሙ፤

አፋችሁን በእጃችሁ ለጕሙ።

6ስለዚህ ነገር ባሰብሁ ቍጥር እደነግጣለሁ፤

ሰውነቴም በፍርሀት ይንቀጠቀጣል።

7ኀጢአተኞች ለምን በሕይወት ይኖራሉ?

ለምን ለእርጅና ይበቃሉ? ለምንስ እያየሉ ይሄዳሉ?

8ዘራቸው በዐይናቸው ፊት፣

ልጆቻቸውም በዙሪያቸው ጸንተው ሲኖሩ ያያሉ፤

9ቤታቸው ያለ ሥጋት በሰላም ይኖራል፤

የእግዚአብሔርም በትር የለባቸውም።

10ኮርማቸው ዘሩ በከንቱ አይወድቅም፤

ያስረግዛል፤ ላማቸውም ሳትጨነግፍ ትወልዳለች።

11ልጆቻቸውን እንደ በግ መንጋ ያሰማራሉ፤

ሕፃናታቸውም ይቦርቃሉ።

12በከበሮና በክራር ይዘፍናሉ፤

በዋሽንትም ድምፅ ይፈነጫሉ።

13ዕድሜያቸውን በተድላ ያሳልፋሉ፤

በሰላምም21፥13 ወይም በፍጥነት ማለት ነው። ወደ መቃብር21፥13 በዕብራይስጡ፣ ሲኦል ይላል። ይወርዳሉ።

14እግዚአብሔርንም እንዲህ ይሉታል፤ ‘አትድረስብን!

መንገድህንም ማወቅ አንፈልግም።

15እናገለግለው ዘንድ፣ ሁሉን ቻይ አምላክ ማን ነው?

ወደ እርሱ ብንጸልይስ ምን እናገኛለን?’

16ይሁንና ብልጽግናቸው በእጃቸው አይደለም፤

ከኀጢአተኞች ምክር እርቃለሁ።

17“የኀጢአተኞች መብራት የጠፋው ስንት ጊዜ ነው?

የእግዚአብሔር ቍጣ መከራ የመጣባቸው፣

መቅሠፍትም የደረሰባቸው ስንት ጊዜ ነው?

18በነፋስ ፊት እንዳለ ገለባ፣

በዐውሎ ነፋስም እንደ ተወሰደ ዕብቅ የሆኑት ስንት ጊዜ ነው?

19እናንተ፣ ‘እግዚአብሔር የሰውን ቅጣት ለልጆቹ ያከማቻል’ ትላላችሁ፤

ነገር ግን ያውቀው ዘንድ ለሰውየው ለራሱ ይክፈለው፤

20ዐይኖቹ የራሱን ውድቀት ይዩ፤

ሁሉን ከሚችል አምላክ21፥17-20 17፡18 ቃለ አጋኖዎች ሲሆኑ፣ 19፡20 ደግሞ ብያኔዎች ናቸው። ቍጣ ይጠጣ።

21ሰው ወራቱ በተገባደደ ጊዜ፣

ለቀሪ ቤተ ሰቡ ምን ይገድደዋል?

22“ከፍ ባሉት ላይ ለሚፈርድ አምላክ፣

ዕውቀትን ሊያስተምረው የሚችል አለን?

23አንድ ሰው በፍጹም ተድላ ደስታ እየኖረ፣

በሙሉ ብርታቱም እያለ ይሞታል፤

24ሰውነቱ21፥24 የዚህ ቃል የዕብራይስጡ ትርጕም በትክክል አይታወቅም። በምቾት፣

ዐጥንቱም በሥብ ተሞልቶ እያለ በሞት ይለያል።

25ሌላው ሰው ደግሞ አንዳች መልካም ነገር ሳያይ፣

በተመረረች ነፍስ ይሞታል፤

26ሁለቱም በዐፈር ውስጥ አንድ ላይ ይተኛሉ፤

ትልም ይወርሳቸዋል።

27“እነሆ፣ ምክራችሁን፣

በእኔ ላይ ያሤራችሁትንም ተረድቻለሁ።

28እናንተ፣ ‘የትልቁ ሰው ቤት፣

ኀጢአተኛውም የኖረበት ድንኳን የት አለ?’ አላችሁ፤

29መንገደኞችን አልጠየቃችሁምን?

የነገሯችሁንስ ነገር በጥሞና አላዳመጣችሁምን?

30ክፉ ሰው በመቅሠፍት ቀን እንደሚጠበቅ፣

በቍጣም ቀን እንደሚተርፍ21፥30 ወይም ለመቅሠፍት ቀን ተጠብቆ እንደሚቈይ ማለት ነው። አታውቁምን?

31ተግባሩን ፊት ለፊት የሚነግረው ማን ነው?

የእጁንስ ማን ይሰጠዋል?

32ወደ መቃብር ይወስዱታል፤

ለመቃብሩም ጠባቂ ይደረግለታል።

33የሸለቈው ዐፈር ምቹ ይሆንለታል፤

ሰው ሁሉ ይከተለዋል፤

ስፍር ቍጥር የሌለው ሕዝብ21፥33 ወይም ስፍር ቍጥር እንደ ሌለው ሕዝብ ማለት ነው። በፊቱ ይሄዳል።

34“መልሳችሁ ከሐሰት በስተቀር ሌላ አይገኝበትም!

ታዲያ፣ በማይረባ ነገር እንዴት ልታጽናኑኝ ትችላላችሁ?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 21:1-34

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Mvetserani bwino mawu anga;

ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.

3Ndiloleni ndiyankhule

ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.

4“Kodi ine ndikudandaulira munthu?

Tsono ndilekerenji kupsa mtima?

5Ndipenyeni ndipo mudabwe;

mugwire dzanja pakamwa.

6Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri;

thupi langa limanjenjemera.

7Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo,

amakalamba ndi kusanduka amphamvu?

8Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo,

zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.

9Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha;

mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.

10Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa;

ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.

11Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa;

makanda awo amavinavina pabwalo.

12Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze;

amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.

13Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero

ndipo amatsikira ku manda mwamtendere.

14Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’

Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.

15Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire?

Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?

16Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo,

koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.

17“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa?

Nʼkangati kamene tsoka limawagwera?

Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?

18Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo,

ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?

19Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’

Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.

20Mulole kuti adzionere yekha chilango chake,

kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.

21Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo,

pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?

22“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru,

poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?

23Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse,

ali pa mtendere ndi pa mpumulo,

24thupi lake lili lonenepa,

mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.

25Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima,

wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.

26Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda

ndipo onse amatuluka mphutsi.

27“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,

ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.

28Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti,

matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’

29Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo?

Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?

30Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka,

kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?

31Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo?

Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?

32Iye amanyamulidwa kupita ku manda

ndipo anthu amachezera pa manda ake.

33Dothi la ku chigwa limamukomera;

anthu onse amatsatira mtembo wake,

ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.

34“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo

palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”