ኢዮብ 14 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢዮብ 14:1-22

1“ከሴት የተወለደ ሰው፣

ዘመኑ ዐጭርና በመከራ የተሞላ ነው፤

2እንደ አበባ ይፈካል፤ ይረግፋልም፤

እንደ ጥላ ይፈጥናል፤ አይጸናምም።

3እንደዚህ ባለ ሰው ላይ ዐይንህን ታሳርፋለህን?

ለፍርድስ በፊትህ ታቀርበዋለህን?14፥3 ሰብዓ ሊቃናት፣ ቩልጌትና ሱርስት እንዲሁ ሲሆን ዕብራይስጡ ግን ታቀርበኛለህን? ይላል

4ከርኩስ ነገር ውስጥ ንጹሕን ማን ሊያወጣ ይችላል?

አንድ እንኳ የሚችል የለም!

5የሰው ዕድሜ አስቀድሞ የተወሰነ ነው፤

የወራቱንም ብዛት ወስነህ አስቀምጠሃል፤

ሊያልፈው የማይችለውንም ገደብ አኖርህለት።

6እንግዲህ ዘመኑን እንደ ምንደኛ እስኪፈጽም ድረስ፣

ፊትህን ከእርሱ መልስ፤ ተወው።

7“ዛፍ እንኳ ቢቈረጥ፣

እንደ ገና ሊያቈጠቍጥ፣

አዳዲስ ቅርንጫፍም ሊያበቅል ተስፋ አለው።

8ሥሩ በምድር ውስጥ ቢያረጅ፣

ጕቶው በመሬት ውስጥ ቢበሰብስም፣

9የውሃ ሽታ ባገኘ ጊዜ ያቈጠቍጣል፤

እንደ ተተከለም ችግኝ ቅርንጫፍ ያወጣል።

10ሰው ግን ይሞታል፤ ክንዱንም ይንተራሳል፤

ነፍሱም ትወጣለች፤ ከእንግዲህስ የት ይገኛል?

11ውሃ ከባሕር ውስጥ እንደሚያልቅ፣

የወንዝ ውሃም ጠፍቶ እንደሚደርቅ፣

12እንደዚሁም ሰው ይተኛል፤ ቀናም አይልም፤

ሰማይ እስከሚያልፍ ድረስ አይነቃም፤

ከእንቅልፉም አይነሣም።

13“ምነው መቃብር14፥13 በዕብራይስጥ ሲኦል ማለት ነው። ውስጥ በሰወርኸኝ!

ቍጣህም እስከሚያልፍ በሸሸግኸኝ!

ምነው ቀጠሮ ሰጥተህ፣

ከዚያ በኋላ ባስታወስኸኝ!

14ሰው ከሞተ በኋላ ተመልሶ በሕይወት ይኖራል?

እድሳቴ14፥14 ወይም መፈታቴ እስከሚመጣ ድረስ፣

ተጋድሎ የሞላበትን ዘመኔን ሁሉ እታገሣለሁ።

15ትጠራኛለህ፤ እኔም እመልስልሃለሁ፤

የእጅህንም ሥራ ትናፍቃለህ።

16በዚያን ጊዜ በርግጥ ርምጃዬን ትከታተላለህ፤

ነገር ግን ኀጢአቴን አትቈጣጠርም።

17መተላለፌ በከረጢት ይቋጠራል፤

ኀጢአቴንም ትሸፍናለህ።

18“ተራራ እንደሚሸረሸርና እንደሚወድቅ፣

ዐለትም ከስፍራው እንደሚወገድ፣

19ውሃ ድንጋይን እንደሚቦረቡር፣

ጐርፍም ዐፈርን ዐጥቦ እንደሚወስድ፣

አንተም የሰውን ተስፋ ታጠፋለህ።

20አንድ ጊዜ ፈጽመህ ትበረታለህ፤ እርሱም ያልፋል፤

ገጽታውን ትቀይራለህ፤ ትሸኘዋለህም።

21ልጆቹ ቢከበሩ አያውቅም፤

ቢዋረዱም አያይም።

22የገዛ አካሉ ሕመም ብቻ ይሰማዋል፤

ለራሱም ብቻ ያለቅሳል።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 14:1-22

1“Munthu wobadwa mwa amayi

amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.

2Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;

amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.

3Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?

Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?

4Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?

Palibe ndi mmodzi yemwe!

5Masiku a munthu ndi odziwikiratu;

munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake

ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.

6Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule

kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.

7“Mtengo uli nacho chiyembekezo:

ngati wadulidwa, udzaphukiranso

ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.

8Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka

ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,

9koma pamene chinyontho chafika udzaphukira

ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.

10Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,

amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.

11Monga madzi amaphwera mʼnyanja

kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,

12momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;

mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka

kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.

13“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda

ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita!

Achikhala munandiyikira nthawi,

kuti pambuyo pake mundikumbukirenso.

14Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?

Masiku anga onse a moyo wovutikawu

ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.

15Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;

inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.

16Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga

koma simudzalondola tchimo langa.

17Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;

inu mudzaphimba tchimo langa.

18“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka

ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,

19monganso madzi oyenda amaperesera miyala

ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka,

momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.

20Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;

Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.

21Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;

akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.

22Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake

ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”