ኢሳይያስ 58 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 58:1-14

እውነተኛ ጾም

1“በኀይል ጩኽ፤ ምንም አታስቀር፤

ድምፅህን እንደ መለከት አሰማ፤

ለሕዝቤ ዐመፃቸውን፣

ለያዕቆብም ቤት ኀጢአታቸውን ተናገር።

2ዕለት በዕለት ይፈልጉኛል፤

መንገዴን ለማወቅ የሚጓጉ ይመስላሉ፤

ትክክለኛውን ነገር እንደሚያደርግ፣

የአምላኩንም ትእዛዝ እንዳልተወ ሕዝብ ሁሉ፣

ተገቢ የሆነ ፍትሕ ይለምኑኛል፤

እግዚአብሔር ወደ እነርሱ እንዲቀርብ የሚወድዱም ይመስላሉ።

3‘አንተ ካልተቀበልኸው፣

ስለ ምን ብለን ጾምን?

አንተ ከጕዳይ ካልቈጠርኸው፣

ስለ ምን ራሳችንን አዋረድን?’ ይላሉ።

“ሆኖም በጾማችሁ ቀን የልባችሁን ታደርጋላችሁ፤

ሠራተኞቻችሁንም ትበዘብዛላችሁ።

4ጾማችሁ በጥልና በክርክር፣

በግፍ ጡጫና በመደባደብ ይፈጸማል፤

ከእንግዲህ ዛሬ እንደምትጾሙት ጾማችሁ፣

ድምፃችሁ ወደ ላይ እንደሚሰማ ተስፋ አታድርጉ።

5እኔ የመረጥሁት ጾም እንዲህ ዐይነቱን ነውን?

ሰውስ ራሱን የሚያዋርደው በእንዲህ ያለው ቀን ብቻ ነውን?

እንደ ደንገል ራስን ዝቅ ማድረግ ነውን?

ወይስ ማቅ ለብሶ በዐመድ ላይ መንከባለል ነውን?

ታዲያ ጾም ብለህ የምትጠራው ይህን ነውን?

እግዚአብሔርስ የሚቀበለው እንዲህ ያለውን ቀን ነውን?

6“እንግዲህ እኔ የመረጥሁት ጾም፣

የጭቈናን ሰንሰለት እንድትበጥሱ፣

የቀንበርን ገመድ እንድትፈቱ፣

የተጨቈኑትን ነጻ እንድታወጡ፣

ቀንበርን ሁሉ እንድትሰብሩ አይደለምን?

7ምግብህን ለተራበ እንድታካፍለው፣

ተንከራታቹን ድኻ ወደ ቤትህ እንድታስገባው፣

የተራቈተውን ስታይ እንድታለብሰው፣

የሥጋ ዘመድህንም ፊት እንዳትነሣው አይደለምን?

8ይህ ከሆነ ብርሃንህ እንደ ንጋት ጮራ ይፈነጥቃል፤

ፈውስህ ፈጥኖ ይደርሳል፤

ጽድቅህ58፥8 ወይም የአንተ ጻድቁ ቀድሞህ ይሄዳል፤

የእግዚአብሔር ክብር ደጀን ይሆንልሃል።

9የዚያን ጊዜ ትጣራለህ፤ እግዚአብሔርም ይመልስልሃል፤

ለርዳታ ትጮኻለህ፤ እርሱም፣ ‘አለሁልህ’ ይልሃል።

“የጭቈና ቀንበር፣

የክፋትን ንግግርና ጣት መቀሰርን ከአንተ ብታርቅ፣

10ለተራበው ብትራራለት፣

የተገፉት እንዲጠግቡ ብታደርግ፣

ብርሃንህ በጨለማ ያበራል፤

ሌሊትህም እንደ ቀትር ፀሓይ ይሆናል።

11እግዚአብሔር ሁልጊዜ ይመራሃል፤

ፀሓይ ባቃጠለው ምድር ፍላጎትህን ያሟላል፤

ዐጥንትህን ያበረታል፤

በውሃ እንደ ረካ የአትክልት ቦታ፣

እንደማይቋርጥም ምንጭ ትሆናለህ።

12ወገኖችህ የቀድሞ ፍርስራሾችን መልሰው ይሠራሉ፤

የጥንቱንም መሠረት ያቆማሉ፤

አንተም፣ የተናዱ ቅጥሮችን አዳሽ፣

ባለ አውራ መንገድ ከተሞችን ጠጋኝ ትባላለህ።

13“እግሮችህ ሰንበትን እንዳይሽሩ ብታሳርፍ፣

በተቀደሰው ቀኔ የልብህን ባታደርግ፣

ሰንበትን ደስታ፣

የእግዚአብሔርን ቅዱስ ቀን የተከበረ ብለህ ብትጠራው፣

በገዛ መንገድህ ከመሄድ፣

እንደ ፈቃድህ ከማድረግና ከከንቱ ንግግር ብትቈጠብ፣

14በዚያን ጊዜ በእግዚአብሔር ደስ ይልሃል፤

በምድር ከፍታዎች ላይ እንድትጋልብ፣

የአባትህን የያዕቆብን ርስት ጠግበህ እንድትበላ አደርግሃለሁ”

የእግዚአብሔር አፍ ይህን ተናግሯልና።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 58:1-14

Kusala Kwenikweni

1“Fuwula kwambiri, usaleke.

Mawu ako amveke ngati lipenga.

Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;

uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.

2Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;

amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,

kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola

ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.

Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo

ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.

3Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala

kudya pamene Inu simukulabadirapo?

Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa

pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,

ndipo mumazunza antchito anu onse.

4Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,

mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.

Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.

5Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,

kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?

Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango

ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?

Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,

tsiku lokondweretsa Yehova?

6“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:

Kumasula maunyolo ozunzizira anthu

ndi kumasula zingwe za goli,

kupereka ufulu kwa oponderezedwa

ndi kuphwanya goli lililonse?

7Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?

Osowa ndi ongoyendayenda,

kodi mwawapatsa malo ogona?

Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?

8Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,

ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;

chilungamo chanu chidzakutsogolerani

ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.

9Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;

mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,

ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.

10Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,

ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,

pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,

ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.

11Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;

adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa

ndipo adzalimbitsa matupi anu.

Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,

ngati kasupe amene madzi ake saphwa.

12Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,

ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;

inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.

Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

13“Muzisunga osaphwanya Sabata;

musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,

tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.

Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza

posayenda mʼnjira zanu,

kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,

14mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,

ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.

Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”

Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.