ኢሳይያስ 50 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 50:1-11

የእስራኤል ኀጢአትና የእግዚአብሔር ባሪያ ታዛዥነት

1እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“እናታችሁን የፈታሁበት

የፍቺ ወረቀት የት አለ?

ወይስ እናንተን የሸጥኋችሁ

ለየትኛው አበዳሪዬ ነው?

እነሆ፤ ስለ ኀጢአታችሁ ተሸጣችኋል፤

ስለ መተላለፋችሁም እናታችሁ ተፈትታለች።

2በመጣሁ ጊዜ ለምን በዚያ ሰው አልነበረም?

በተጣራሁስ ጊዜ የሚመልስ ሰው እንዴት በዚያ ታጣ?

ስለ እናንተ ወጆ ለመክፈል ክንዴ ዐጥራ ነበርን?

እናንተንስ ለማዳን ኀይል አነሰኝን?

እነሆ፤ በተግሣጼ ባሕሩን አደርቃለሁ፤

ወንዞችን ምድረ በዳ አደርጋለሁ፤

ዓሦቻቸው ውሃ በማጣት ይሸታሉ፤

በጥማትም ይሞታሉ።

3ሰማይን ጨለማ አለብሰዋለሁ፤

ማቅን መሸፈኛው አደርጋለሁ።”

4ልዑል እግዚአብሔር የተባ አንደበት ሰጥቶኛል፤

ስለዚህ ደካሞችን ብርቱ ለማድረግ ምን ማለት እንዳለብኝ ዐውቃለሁ፤

በየማለዳው ያነቃኛል፤

በመማር ላይ እንዳለ ተማሪ ለመስማት ጆሮዬን ያነቃዋል።

5ልዑል እግዚአብሔር ጆሮዬን ከፍቶታል፤

እኔም ዐመፀኛ አይደለሁም፤

ወደ ኋላም አላፈገፈግሁም።

6ለሚገርፉኝ ጀርባዬን፣

ጢሜን ለሚነጩ ጕንጬን ሰጠሁ፤

ፊቴን ከውርደት፣

ከጥፋትም አልሰወርሁም።

7ጌታ እግዚአብሔር ስለሚረዳኝ አልዋረድም፤

ስለዚህ ፊቴን እንደ ባልጩት ድንጋይ

አድርጌአለሁ፤

እንደማላፍርም ዐውቃለሁ።

8ንጹሕ መሆኔን የሚያረጋግጥልኝ በአጠገቤ አለ፤

ታዲያ ማን ሊከስሰኝ ይችላል?

እስቲ ፊት ለፊት እንጋጠም!

ተቃዋሚዬስ ማን ነው?

እስቲ ይምጣ!

9የሚረዳኝ እርሱ ጌታ እግዚአብሔር ነው፤

የሚፈርድብኝስ ማን ነው?

እነሆ፤ ሁሉም እንደ ልብስ ያረጃሉ፤

ብልም ይበላቸዋል።

10ከእናንተ እግዚአብሔርን የሚፈራ፣

የባሪያውንም ቃል የሚሰማ ማን ነው?

ያ ሰው በጨለማ የሚሄድ ከሆነና፣

ብርሃንም ከሌለው፣

በእግዚአብሔር ስም ይታመን፤

በአምላኩም ይደገፍ።

11አሁን ግን እናንተ እሳት አንድዳችሁ፣

የራሳችሁን የሚንቦገቦግ ችቦ የያዛችሁ ሁሉ፣

በሉ በእሳታችሁ ብርሃን ሂዱ፤

ባንቦገቦጋችሁትም የችቦ ብርሃን ተመላለሱ።

እንግዲህ ከእጄ የምትቀበሉት ይህ ነው፤

በሥቃይም ትጋደማላችሁ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 50:1-11

Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki

1Yehova akuti,

“Kalata imene ndinasudzulira amayi

anu ili kuti?

Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,

ndinakugulitsani kwa ati?

Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;

amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.

2Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?

Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?

Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?

Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?

Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,

mitsinje ndinayisandutsa chipululu;

nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;

ndipo zinafa ndi ludzu.

3Ndinaphimba thambo ndi mdima

ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”

4Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula

kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.

Mmawa mulimonse amandidzutsa,

amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.

5Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,

ndipo sindinakhale munthu wowukira

ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.

6Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya

masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;

sindinawabisire nkhope yanga

anthu ondinyoza ndi ondilavulira.

7Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,

sindidzachita manyazi.

Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,

chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.

8Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,

ndaninso amene adzandiyimba mlandu?

Abwere kuti tionane maso ndi maso!

Mdani wanga ndi ndani?

Abweretu kuti tilimbane!

9Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.

Ndaninso amene adzanditsutsa?

Onse adzatha ngati chovala

chodyedwa ndi njenjete.

10Ndani mwa inu amaopa Yehova

ndi kumvera mawu a mtumiki wake?

Aliyense woyenda mu mdima,

popanda chomuwunikira,

iye akhulupirire dzina la Yehova

ndi kudalira Mulungu wake.

11Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto

ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,

lowani mʼmoto wanu womwewo.

Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.

Ndipo ine Yehova

ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.