ኢሳይያስ 47 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 47:1-15

የባቢሎን ውድቀት

1“አንቺ የባቢሎን47፥1 ወይም በዚህና በ5 ላይ ከለዳውያን ድንግል ልጅ ሆይ፤

ውረጂ፤ በትቢያ ላይ ተቀመጪ፤

አንቺ የባቢሎናውያን ልጅ ሆይ፤

ከዙፋንሽ ውረጂ፤ መሬት ላይ ተቀመጪ፤

ከእንግዲህ ውብ ወይም ለግላጋ፣

ተብለሽ አትጠሪም።

2ወፍጮ ወስደሽ እህል ፍጪ፤

መሸፋፈኛሽን አውልቂ፤

ቀሚስሽንም ከፍ ከፍ አድርጊ፤ ባትሽን ግለጪ፤

እየተንገዳገድሽ ወንዙን ተሻገሪ።

3ዕርቃንሽ ይገለጥ፤

ኀፍረትሽ ይታይ፤

እበቀላለሁ፤

እኔ ማንንም አልተውም።”

4የሚቤዠን የእስራኤል ቅዱስ፣

ስሙ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር ነው።

5“አንቺ የባቢሎናውያን ልጅ ሆይ፤

ወደ ጨለማ ግቢ፤ ዝም ብለሽም ተቀመጪ፤

ከእንግዲህ የመንግሥታት እመቤት

ተብለሽ አትጠሪም።

6ሕዝቤን ተቈጥቼ ነበር፤

ርስቴን አርክሼው ነበር፤

አሳልፌ በእጅሽ ሰጠኋቸው፤

አንቺ ግን አልራራሽላቸውም፤

በዕድሜ በገፉት ላይ እንኳ፣

እጅግ ከባድ ቀንበር ጫንሽባቸው።

7አንቺም፣ ‘እስከ መጨረሻው፣

ለዘላለም ንግሥት እሆናለሁ!’ አልሽ፤

ሆኖም እነዚህን ነገሮች አላስተዋልሽም፤

ፍጻሜያቸው ምን እንደሚሆንም አላሰብሽም።

8“አሁንም አንቺ ቅምጥል ፍጡር፣

በራስሽ ተማምነሽ የምትቀመጪ፣

በልብሽም፣

‘እኔ ነኝ፣ ከእኔ በቀር ሌላ የለም፤

ከእንግዲህ መበለት አልሆንም፤

የወላድ መካንም አልሆንም’ የምትይ ስሚ!

9እነዚህ ሁለት ነገሮች፣

መበለትነትና የወላድ መካንነት፣

አንድ ቀን ድንገት ይመጡብሻል፤

የቱን ያህል አስማት፣

የቱንም ያህል መተት ቢኖርሽ፣

በሙሉ ኀይላቸው ይመጡብሻል።

10በክፋትሽ ተማምነሽ፣

‘ማንም አያየኝም’ አልሽ፤

ደግሞም፣ ‘እኔ ነኝ፣ ከእኔ በቀር ሌላ የለም’

ባልሽ ጊዜ፣

ጥበብሽና ዕውቀትሽ አሳሳቱሽ።

11ጥፋት ይመጣብሻል፤

ነገር ግን በአስማትሽ እንዴት እንደምታርቂው አታውቂም፤

ወጆ ከፍለሽ ለማስወገድ የማትችዪው፣

ጕዳት ይወድቅብሻል፤

ያላሰብሽው አደጋ፣

ድንገት ይደርስብሻል።

12“በይ እንግዲህ፣ ከልጅነትሽ ጀምሮ የደከምሽባቸውን፣

አስማቶችሽን፣

ብዙ መተቶችን ቀጥዪባቸው፤

ምናልባት ይሳካልሽ፣

ምናልባትም ጠላቶችሽን ታሸብሪባቸው ይሆናል።

13የተቀበልሽው ምክር ሁሉ ድካም ብቻ ሆኖ አስቀርቶሻል፤

እነዚያ ከወር እስከ ወር ከዋክብትን አንጋጦ በማየት የሚተነብዩ፣

ኮከብ ቈጣሪዎች እስቲ ይምጡ፤

ከሚደርስብሽም ነገር እስቲ ያድኑሽ።

14እነሆ፣ እነርሱ ገለባ ናቸው፤

እሳት ይበላቸዋል፤

ከነበልባሉ ወላፈን የተነሣ፣

ራሳቸውን ማዳን አይችሉም።

ሰው የሚሞቀው ፍም አይኖርም፤

ተቀምጠው የሚሞቁትም እሳት የለም።

15ከልጅነት ጀምሮ አብረሻቸው የደከምሽው፣

አብረሽ የተገበያየሻቸው፣

ሊያደርጉ የሚችሉት ይህንኑ ብቻ ነው።

እያንዳንዱ በስሕተቱ ይገፋበታል፤

አንቺን ግን የሚያድን የለም።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 47:1-15

Kugwa kwa Babuloni

1“Tsika, ndi kukhala pa fumbi,

iwe namwali, Babuloni;

khala pansi wopanda mpando waufumu,

iwe namwali, Kaldeya

pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera

kumugwira mosamala.

2Tenga mphero ndipo upere ufa;

chotsa nsalu yako yophimba nkhope

kwinya chovala chako mpaka ntchafu

ndipo woloka mitsinje.

3Maliseche ako adzakhala poyera

ndipo udzachita manyazi.

Ndidzabwezera chilango

ndipo palibe amene adzandiletse.”

4Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

5“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,

iwe namwali, Kaldeya;

chifukwa sadzakutchulanso

mfumukazi ya maufumu.

6Ndinawakwiyira anthu anga,

osawasamalanso.

Ndinawapereka manja mwako,

ndipo iwe sunawachitire chifundo.

Iwe unachitira nkhanza

ngakhale nkhalamba.

7Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse

ngati mfumukazi.’

Koma sunaganizire zinthu izi

kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

8“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,

amene ukukhala mosatekesekawe,

umaganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.

Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,

ndipo ana anga sadzamwalira.’

9Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,

zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:

ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.

Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu

ngakhale ali ndi amatsenga ambiri

ndi mawula amphamvu.

10Iwe unkadalira kuyipa kwako

ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’

Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,

choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’

11Ngozi yayikulu idzakugwera

ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.

Mavuto adzakugwera

ndipo sudzatha kuwachotsa;

chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa

chidzakugwera mwadzidzidzi.

12“Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,

pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,

wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.

Mwina udzatha kupambana

kapena kuopsezera nazo adani ako.

13Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!

Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.

Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi

zimene ziti zidzakuchitikire.

14Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;

adzapsa ndi moto.

Sangathe kudzipulumutsa okha

ku mphamvu ya malawi a moto.

Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;

kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.

15Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,

anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito

ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.

Onse adzamwazika ndi mantha,

sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”