ኢሳይያስ 38 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 38:1-22

የሕዝቅያስ መታመም

1በዚያ ጊዜ ሕዝቅያስ ታመመ፤ ሞት አፋፍ ደረሰ፤ የአሞጽ ልጅ ነቢዩ ኢሳይያስም ወደ እርሱ መጥቶ፣ “እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤ ‘ከሕመምህ አትድንም፤ ትሞታለህና ቤትህን አሰናዳ’ ” አለው።

2ሕዝቅያስም ፊቱን ወደ ግድግዳ አዙሮ፣ እንዲህ ሲል ወደ እግዚአብሔር ጸለየ፤ 3እግዚአብሔር ሆይ፤ በፊትህ በታማኝነትና በፍጹም ልብ ደስ የሚያሰኝህንም በማድረግ እንዴት እንደ ኖርሁ አቤቱ ዐስብ።” ሕዝቅያስም አምርሮ አለቀሰ።

4የእግዚአብሔርም ቃል ወደ ኢሳይያስ እንዲህ ሲል መጣ፤ 5“ሂድና ለሕዝቅያስ እንዲህ ብለህ ንገረው፤ ‘የአባትህ የዳዊት አምላክ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤ “ጸሎትህን ሰምቻለሁ፤ እንባህንም አይቻለሁ፤ በዕድሜህም ላይ ዐሥራ አምስት ዓመት እጨምርልሃለሁ። 6አንተንና ይህችን ከተማ ከአሦር ንጉሥ እጅ እታደጋለሁ፤ ለከተማዋም እከላከልላታለሁ።”

7“ ‘እግዚአብሔር የገባልህን ቃል እንደሚፈጽምልህ፣ የእግዚአብሔር ምልክት ይህ ነው፤ 8በአካዝ የሰዓት መቍጠሪያ ደረጃ ላይ፣ የወረደውን የፀሓይ ጥላ በዐሥር ደረጃ ወደ ኋላ እንዲመለስ አደርጋለሁ።’ ” ስለዚህ ወርዶ የነበረው የፀሓይ ጥላ ያንኑ ያህል ወደ ኋላ ተመለሰ።

9የይሁዳ ንጉሥ ሕዝቅያስ ከሕመሙ ከተፈወሰ በኋላ የጻፈው ጽሕፈት፤

10እኔ፣ “በዕድሜዬ እኩሌታ፣

በሲኦል ደጆች ማለፍ አለብኝን?

የቀረውንስ ዘመኔን ልነጠቅ ይገባልን?” አልሁ።

11እንዲህም አልሁ፤ “ዳግም እግዚአብሔርን

እግዚአብሔርን በሕያዋን ምድር አላይም፤

ከእንግዲህም የሰውን ዘር አላይም፤

በዚህ ዓለም ከሚኖሩትም ጋር አልሆንም።

12ቤቴ እንደ እረኛ ድንኳን ተነቀለ፤

ከእኔም ተወሰደ፤

ሕይወቴን እንደ ሸማኔ ጠቀለልሁ፤

ከመጠቅለያ ቈርጦኛል፤

ከጧት እስከ ማታ ልትጨርሰኝ ፈጠንህ።

13እስከ ማለዳ በትዕግሥት ጠበቅሁ፤

እርሱ ግን እንደ አንበሳ ዐጥንቶቼን ሁሉ ሰባበረ፤

ከጧት እስከ ማታም ልትጨርሰኝ ፈጠንህ።

14እንደ ጨረባ፣ እንደ ሽመላም ተንጫጫሁ፤

እንደ ርግብ አልጐመጐምሁ፤

ዐይኖቼ ወደ ሰማይ በመመልከት ደከሙ፤

ጌታ ሆይ፤ ተጨንቄአለሁና ታደገኝ!”

15እንግዲህ ምን እላለሁ?

እርሱ ተናግሮኛል፤ ራሱ ደግሞ ይህን አድርጓል፤

ስለ ነፍሴ ጭንቀት፣

ዕድሜዬን ሁሉ በትሕትና እሄዳለሁ።

16ጌታ ሆይ፤ ሰዎች በእነዚህ ነገሮች ይኖራሉ፤

መንፈሴም እንዲሁ በእነዚህ ሕይወትን ያገኛል፤

ፈወስኸኝ፤

በሕይወትም አኖርኸኝ።

17እነሆ፤ በሥቃይ የተጨነቅሁት፣

ለጥቅሜ ሆነ፤

ከጥፋት ጕድጓድ፣

በፍቅርህ ጠበቅኸኝ፤

ኀጢአቴንም ሁሉ፣

ወደ ኋላህ ጣልህ።

18ሲኦል አያመሰግንህም፤

ሞት አያወድስህም፤

ወደ ጕድጓድ የሚወርዱ፣

የአንተን ታማኝነት ተስፋ አያደርጉም።

19እኔ ዛሬ እንደማደርገው፣

ሕያዋን እነርሱ ያመሰግኑሃል።

ስለ አንተ ታማኝነትም፣

አባቶች ለልጆቻቸው ይነግራሉ።

20እግዚአብሔር ያድነኛል፤

ስለዚህ በዕድሜ ዘመናችን ሁሉ፣

በእግዚአብሔር ቤተ መቅደስ፣

አውታር ባለው መሣሪያ እንዘምራለን።

21ኢሳይያስም፣ “የበለስ ጥፍጥፍ ወስዳችሁ በዕባጩ ላይ አድርጉለት፤ እርሱም ይፈወሳል” ብሎ ነበር።

22ሕዝቅያስም፣ “ወደ እግዚአብሔር ቤተ መቅደስ እወጣ ዘንድ ምልክቱ ምንድን ነው?” ብሎ ነበር።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 38:1-22

Kudwala kwa Hezekiya

1Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

4Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

7“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

9Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10Ine ndinaganiza kuti

ndidzapita ku dziko la akufa

pamene moyo ukukoma.

11Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,

mʼdziko la anthu amoyo,

sindidzaonanso mtundu wa anthu

kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.

12Nyumba yanga yasasuka

ndipo yachotsedwa.

Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,

ngati munthu wowomba nsalu;

kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.

13Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;

koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,

ndipo mwakhala mukundisiya.

14Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,

ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.

Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.

Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15Koma ine ndinganene chiyani?

Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.

Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,

ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.

16Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.

Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.

Munandichiritsa ndi

kundikhalitsa ndi moyo.

17Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere

kuti ndikhale ndi moyo;

Inu munandisunga

kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko

chifukwa mwakhululukira

machimo anga onse.

18Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,

akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.

Iwo amene akutsikira ku dzenje

sangakukhulupirireni.

19Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,

monga mmene ndikuchitira ine lero lino;

abambo amawuza ana awo za

kukhulupirika kwanu.

20Yehova watipulumutsa.

Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe

masiku onse a moyo wathu

mʼNyumba ya Yehova.

21Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”