ኢሳይያስ 35 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 35:1-10

የተቤዠ ሕዝብ ደስታ

1ምድረ በዳውና ደረቁ ምድር ደስ ይላቸዋል፤

በረሓው ሐሤት ያደርጋል፤ ይፈካል፤

እንደ አደይም ያብባል።

2በደስታና በዝማሬ ሐሤት ያደርጋል፤

የሊባኖስ ክብር ይሰጠዋል፤

የቀርሜሎስንና የሳሮንን ግርማ ይለብሳል።

የአምላካችንን ታላቅ ግርማ፣

የእግዚአብሔርን ክብር ያያሉ።

3የደከሙትን እጆች አበርቱ፤

የላሉትንም ጕልበቶች አጽኑ፤

4የሚፈራ ልብ ላላቸው እንዲህ በሉ፤

“በርቱ፤ አትፍሩ፤

አምላካችሁ ይመጣል፤

ሊበቀል ይመጣል፤

እርሱም ብድራቱን ይዞ፣

ሊያድናችሁ ይመጣል።”

5በዚያን ጊዜም የዕውር ዐይኖች ይገለጣሉ፤

የደንቈሮም ጆሮዎች ይከፈታሉ።

6ዐንካሳ እንደ ሚዳቋ ይዘልላል፤

የድዳውም አንደበት በደስታ ይዘምራል፤

ውሃ ከበረሓ ይወጣል፤

ምንጮችም ከምድረ በዳ ይፈልቃሉ።

7ንዳዳማው ምድር ኵሬ ይሆናል፤

የተጠማው መሬት ውሃ ያመነጫል።

ቀበሮዎች በተኙባቸው ጕድጓዶች፣

ሣር፣ ሸንበቆና ደንገል ይበቅልበታል።

8በዚያ አውራ ጐዳና ይሆናል፤

“የተቀደሰ መንገድ” ተብሎ ይጠራል።

የረከሱ አይሄዱበትም፤

በመንገዱ ላይ ላሉት ብቻ ይሆናል፤

ገራገሮችም ከመንገዱ አይስቱም።

9አንበሳ አይኖርበትም፤

ነጣቂ አውሬም አይወጣበትም፤

እነዚህማ በዚያ ስፍራ አይገኙም፤

የዳኑት ብቻ በዚያ ይሄዳሉ፤

10እግዚአብሔር የዋጃቸው ይመለሳሉ።

እየዘመሩ ወደ ጽዮን ይገባሉ፤

ዘላለማዊ ደስታን እንደ አክሊል ይቀዳጁታል፤

ፍሥሓና ሐሤት ያገኛሉ፤

ሐዘንና ትካዜ ከዚያ ይሸሻሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 35:1-10

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

1Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;

dziko lowuma lidzakondwa

ndi kuchita maluwa. 2Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka

lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.

Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,

maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,

ukulu wa Mulungu wathu.

3Limbitsani manja ofowoka,

limbitsani mawondo agwedegwede;

4nenani kwa a mitima yamantha kuti;

“Limbani mtima, musachite mantha;

Mulungu wanu akubwera,

akubwera kudzalipsira;

ndi kudzabwezera chilango adani anu;

akubwera kudzakupulumutsani.”

5Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso

ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.

6Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,

ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.

Akasupe adzatumphuka mʼchipululu

ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,

7mchenga wotentha udzasanduka dziwe,

nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.

Pamene panali mbuto ya ankhandwe

padzamera udzu ndi bango.

8Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;

ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.

Anthu odetsedwa

sadzayendamo mʼmenemo;

zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.

9Kumeneko sikudzakhala mkango,

ngakhale nyama yolusa sidzafikako;

sidzapezeka konse kumeneko.

Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.

10Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.

Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;

kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.

Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,

ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.