ኢሳይያስ 30 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 30:1-33

ወዮ ለእንቢተኛ ሕዝብ

1“ለዐመፀኞች ልጆች ወዮላቸው”

ይላል እግዚአብሔር

“የእኔ ያልሆነውን ሐሳብ ይከተላሉ፤

ከመንፈሴ ያልሆነውን ቃል ኪዳን ያደርጋሉ፤

በኀጢአት ላይ ኀጢአት ይጨምራሉ።

2እኔን ሳይጠይቁ፣

ወደ ግብፅ ይወርዳሉ፤

የፈርዖንን ከለላ፣

የግብፅንም ጥላ ለመጠጊያነት ይፈልጋሉ።

3ነገር ግን የፈርዖን ከለላ ውርደት ይሆንባችኋል፤

የግብፅም ጥላ ኀፍረት ያመጣባችኋል።

4ምንም እንኳ ሹሞች በጣኔዎስ ቢኖሯቸውም፣

መልእክተኞቻቸው ሓኔስ ቢደርሱም፣

5ውርደትና ኀፍረት ብቻ እንጂ

ርዳታም ሆነ ረብ በማያስገኙላቸው፣

ምንም ጥቅም በማይሰጧቸው ሰዎች ምክንያት

ሁሉም ለኀፍረት ይዳረጋሉ።”

6በኔጌቭ ስላሉት እንስሳት የተነገረ ንግር፤

መልእክተኞች ሀብታቸውን በአህያ፣

ውድ ዕቃዎቻቸውን በግመል ጭነው፣

ተባዕትና እንስት አንበሶች፣

መርዘኛና ተወርዋሪ እባቦች በሚኖሩበት፣

መከራና ጭንቅ ባለበት ምድር ዐልፈው፣

ወደማይጠቅማቸው ወደዚያ ሕዝብ፣

7ርዳታዋም ፈጽሞ ዋጋ ቢስ ወደ ሆነው ወደ ግብፅ ይሄዳሉ።

ስለዚህ ስሟን፣

ረዓብ፣ ምንም የማትጠቅም ብዬ እጠራታለሁ።

8አሁንም ሂድ፤ በሰሌዳ ላይ ጻፍላቸው፤

በጥቅልል መጽሐፍ ላይ ክተብላቸው፤

ለሚመጡትም ዘመናት፣

ለዘላለም ምስክር ይሆናል፤

9እነዚህም የእግዚአብሔርን ትእዛዝ ለመስማት የማይፈልጉ፣

ዐመፀኛ ሕዝቦችና አታላይ ልጆች ናቸው።

10ባለ ራእዮችን፣

“ከእንግዲህ ራእይን አትዩ” ይላሉ፤

ነቢያትንም እንዲህ ይላሉ፤

“እውነተኛውን ትንቢት ከእንግዲህ አትንገሩን፤

ደስ የሚያሰኘውን ንገሩን፤

የሚያማልለውን ተንብዩልን።

11ከዚህ መንገድ ፈቀቅ በሉ፤

ከጐዳናውም ራቁ፤

ከእስራኤል ቅዱስ ጋር

ፊት ለፊት አታጋጥሙን።”

12ስለዚህ፣ የእስራኤል ቅዱስ እንዲህ ይላል፤

“ይህን ቃል ስላቃለላችሁ፣

ግፍን ስለ ታመናችሁ፣

ማታለልን ስለ ተደገፋችሁ፣

13ስለዚህ ይህ ኀጢአት፣

ተሰነጣጥቆ ሊወድቅ እንደ ደረሰ፣

ሳይታሰብ ድንገት እንደሚወድቅ ረዥም ቅጥር ይሆንባችኋል።

14ከስብርባሪዎቹም መካከል፣

ለፍም መጫሪያ፣

ለውሃ መጥለቂያ ገል እስከማይገኝ ድረስ፣

ምንም ሳይቀር ክፉኛ እንደሚንኰታኰት፣

የሸክላ ዕቃ ይደቅቃል።”

15የእስራኤል ቅዱስ ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“በመመለስና በማረፍ ትድናላችሁ፤

በጸጥታና በመታመን ትበረታላችሁ፤

እናንተ ግን ይህን አላደረጋችሁም፤

16ደግሞም ‘አይሆንም፣ በፈረስ እንሸሻለን’ አላችሁ፤

ስለዚህ ትሸሻላችሁ።

ደግሞም፣ ‘በፈጣን ፈረስ እናመልጣለን’ አላችሁ፤

ስለዚህ አሳዳጆቻችሁም ፈጣን ይሆናሉ።

17በተራራ ዐናት ላይ እንደ ተተከለ ሰንደቅ ዐላማ፣

በኰረብታም ላይ እንደ ቆመ ምልክት

ሆናችሁ እስክትቀሩ ድረስ

በአንድ ሰው ዛቻ፣

ሺሕ ሰው ይሸሻል፤

በአምስት ሰው፣

ሁላችሁ ትሸሻላችሁ።”

18እግዚአብሔር ግን ምሕረት ሊያደርግላችሁ ይታገሣል፤

ርኅራኄም ሊያሳያችሁ ይነሣል።

እግዚአብሔር የፍትሕ አምላክ ነውና፣

እርሱን በመተማመን የሚጠባበቁት የተባረኩ ናቸው።

19በኢየሩሳሌም የምትኖሩ የጽዮን ሕዝብ ሆይ፤ ከእንግዲህ ወዲህ አታለቅሱም። ለርዳታ ወደ እርሱ ስትጮኹ እንዴት ምሕረት አያደርግላችሁ! ጩኸትህን እንደ ሰማም ፈጥኖ ይመልስልሃል። 20ጌታ የጭንቀት እንጀራና የመከራ ውሃ ቢሰጥህም፣ አስተማሪህ ከእንግዲህ አይሰወርብህም፤ ዐይኖችህም አስተማሪህን ያያሉ። 21ወደ ቀኝም ሆነ ወደ ግራ ዘወር ብትል ጆሮህ ከኋላህ፣ “መንገዱ ይህ ነው፤ በእርሱ ሂድ” የሚል ድምፅ ይሰማል። 22ከዚያም በብር የተለበጡትን ጣዖቶችህንና በወርቅ የተለበዱ ምስሎችህን ታዋርዳለህ፤ “ከዚህ ወግዱ!” ብለህም እንደ መርገም ጨርቅ ትጥላቸዋለህ።

23በምድርም ለዘራኸው ዘር ዝናብን ይሰጥሃል፤ ከመሬትም የሚገኘው ፍሬ ምርጥና የተትረፈረፈ ይሆናል። በዚያን ቀን ከብቶችህ በትልቅ ሜዳ ላይ ይሰማራሉ። 24የዕርሻ በሬዎችና አህዮች በመንሽና በላይዳ የተለየውን ገፈራና ድርቆሽ ይበላሉ። 25በታላቁ የዕልቂት ቀን ምሽጎች ሲፈርሱ፣ በረጅም ተራራ ሁሉና ከፍ ባለውም ኰረብታ ሁሉ ላይ ወራጅ ወንዝ ይፈስሳል። 26እግዚአብሔር የሕዝቡን ስብራት ሲጠግን፣ ያቈሰለውንም ሲፈውስ፣ ጨረቃ እንደ ፀሓይ ታበራለች፤ የፀሓይም ብርሃን እንደ ሰባት ቀን ብርሃን ሰባት ዕጥፍ ይደምቃል።

27እነሆ፤ የእግዚአብሔር ስም፣

ከሚነድድ ቍጣ፣ ጥቅጥቅ ካለና ከሚትጐለጐል የጢስ ደመና ጋር ከሩቅ ይመጣል፤

ከንፈሮቹ ቍጣን የተሞሉ ናቸው፤

ምላሱም የሚባላ እሳት ነው።

28እስትንፋሱ እንደሚጠራርግ፣

እስከ ዐንገት እንደሚደርስም የውሃ ሙላት ነው፤

መንግሥታትን በጥፋት ወንፊት ያበጥራቸዋል፤

በሕዝቦችም መንጋጋ፣

መንገድ የሚያስት ልጓም ያስገባል።

29በሌሊት የተቀደሰ በዓል ስታከብሩ

እንደምትዘምሩ፣

ትዘምራላችሁ፤

ወደ እግዚአብሔር ተራራ፣

ወደ እስራኤል ዐለት፣

ሰዎች ዋሽንት እየነፉ በደስታ እንደሚወጡ፣

የእናንተም ልብ እንዲሁ ሐሤት ያደርጋል።

30እግዚአብሔር በሚነድድ ቍጣና በሚባላ እሳት፣

በወጀብና በነጐድጓድ፣ በበረዶም ድንጋይ፣

ግርማ የተሞላበትን ድምፁን ሰዎች እንዲሰሙ አድርጎ ያሰማል፤

ክንዱም ስትወርድ ያሳያቸዋል።

31የእግዚአብሔር ድምፅ አሦርን ያስደነግጣል፤

በትሩም ይመታቸዋል።

32እግዚአብሔር የሚያወርድባቸው የቅጣት

በትር ሁሉ፣

በከበሮና በበገና ድምፅ የታጀበ ነው፤

በጦርነትም ክንዱን አሳይቶ መታቸው።

33ከቀድሞ ጀምሮ ቶፌት የተባለ የማቃጠያ

ስፍራ ተዘጋጅቷል፤

ለንጉሡም ተበጅቷል፤

ማንደጃ ጕድጓዱም ሰፊና ጥልቅ ነው፤

በውስጡም ብዙ እሳትና ማገዶ አለ፤

የእግዚአብሔርም እስትንፋስ

እንደ ፈሳሽ ድኝ ያቀጣጥለዋል።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 30:1-33

Tsoka kwa Mtundu Wopanduka

1Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira

amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine,

nachita mgwirizano wawowawo

koma osati motsogozedwa ndi Ine.

Choncho amanka nachimwirachimwira.

2Amapita ku Igupto kukapempha thandizo

koma osandifunsa;

amathawira kwa Farao kuti awateteze,

ku Igupto amafuna malo opulumulira.

3Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu,

malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.

4Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani,

ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,

5aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi

chifukwa cha anthu opanda nawo phindu,

amene sabweretsa thandizo kapena phindu,

koma manyazi ndi mnyozo.”

6Uthenga wonena za nyama za ku Negevi:

Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa,

mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi,

mphiri ndi njoka zaululu.

Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo,

kupita nazo kwa mtundu wa anthu

umene sungawathandize.

7Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe.

Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha

Rahabe chirombo cholobodoka.

8Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita,

ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona

ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha

masiku a mʼtsogolo.

9Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi

osafuna kumvera malangizo a Yehova.

10Iwo amawuza alosi kuti,

‘Musationerenso masomphenya!’

Ndipo amanena kwa mneneri kuti,

‘Musatinenerenso zoona,’

mutiwuze zotikomera,

munenere za mʼmutu mwanu.

11Patukani pa njira ya Yehova,

lekani kutsata njira ya Yehova;

ndipo tisamvenso mawu

a Woyerayo uja wa Israeli!”

12Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti,

“Popeza inu mwakana uthenga uwu,

mumakhulupirira zopondereza anzanu

ndipo mumadalira kuchita zoyipa,

13choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu

pa khoma lalitali ndi lopendama

limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.

14Lidzaphwanyika ngati mbiya

imene yanyenyekeratu,

mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale

lopalira moto mʼngʼanjo

kapena lotungira madzi mʼchitsime.”

15Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi:

“Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka,

ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu,

koma inu munakana zimenezi.

16Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa,

tidzakwera pa akavalo aliwiro.’

Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro,

koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.

17Anthu 1,000 mwa inu adzathawa

poona mdani mmodzi;

poona adani asanu okha

nonsenu mudzathawa.

Otsala anu

adzakhala ngati mbendera pa phiri,

ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”

18Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima,

iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo.

Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo.

Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!

19Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani. 20Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo. 21Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.” 22Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”

23Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka. 24Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo. 25Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono. 26Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.

27Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali,

ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka.

Iye wayankhula mwaukali kwambiri,

ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.

28Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira,

wa madzi ofika mʼkhosi.

Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza;

Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo,

kuti ziwasocheretse.

29Ndipo inu mudzayimba

mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika.

Mudzasangalala

ngati anthu oyimba zitoliro

popita ku phiri la Yehova,

thanthwe la Israeli.

30Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova

ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo

ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa,

mphenzi, namondwe ndi matalala.

31Asiriya adzaopa liwu la Yehova,

ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.

32Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo,

anthu ake adzakhala akuvina nyimbo

zoyimbira matambolini ndi azeze,

Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.

33Malo otenthera zinthu akonzedwa kale;

anakonzera mfumu ya ku Asiriya.

Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu,

ndipo muli nkhuni zambiri;

mpweya wa Yehova,

wangati mtsinje wa sulufule,

udzayatsa motowo pa nkhunizo.