ኢሳይያስ 24 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 24:1-23

እግዚአብሔር ምድርን ፈጽሞ ያጠፋታል

1እነሆ፤ እግዚአብሔር ምድርን ባድማ ያደርጋታል፤

ፈጽሞ ያጠፋታል፤

የፍርስራሽ ክምር ያደርጋታል፤

ነዋሪዎቿንም ይበትናል።

2ነገሩ ሁሉ አንድ ዐይነት ይሆናል፤

በሕዝቡ ላይ የሚሆነው በካህኑ፣

በአገልጋዩ ላይ የሚሆነው በጌታው፣

በአገልጋይዋ ላይ የሚሆነው በእመቤቷ፣

በገዥው ላይ የሚሆነው በሻጩ፣

በተበዳሪው ላይ የሚሆነው በአበዳሪው፣

በብድር ከፋይ ላይ የሚሆነው በብድር ሰጪው ይሆናል።

3ምድር ፈጽሞ ባድማ ትሆናለች፤

ጨርሶም ትበዘበዛለች፤

እግዚአብሔር ይህን ቃል ተናግሯልና።

4ምድር ትደርቃለች፤ ትረግፋለች፤

ዓለም ትዝላለች፤ ትረግፋለች፤

የምድርም መሳፍንት ይዝላሉ።

5ምድር በሕዝቧ ትረክሳለች፤

ሕግን ጥሰዋል፤

ሥርዐትን ተላልፈዋል፤

ዘላለማዊውንም ኪዳን አፍርሰዋል።

6ስለዚህ ርግማን ምድርን ትበላለች፤

ሕዝቦቿም ስለ በደላቸው ይቀጣሉ፤

ስለዚህ የምድር ነዋሪዎች ተቃጥለዋል፤

በጣም ጥቂት የሆኑት ቀርተዋል።

7አዲሱ የወይን ጠጅ ዐለቀ፤ የወይኑም ተክል ደረቀ፤

ደስተኞችም ሁሉ አቃሰቱ።

8የከበሮ ደስታ ጸጥ አለ፤

የጨፋሪዎች ጩኸት አበቃ፤

ደስ የሚያሰኘውም በገና እረጭ አለ።

9ከእንግዲህ እየዘፈኑ የወይን ጠጅ አይጠጡም፤

መጠጡም ለሚጠጡት ይመርራል።

10የፈራረሰችው ከተማ ባድማ ሆነች፤

የየቤቱም መግቢያ ተዘጋ።

11በየአደባባዩ የወይን ጠጅ ያለህ እያሉ ይጮኻሉ፤

ደስታው ሁሉ ወደ ሐዘን ይለወጣል፤

ሐሤቱም ሁሉ ከምድር ገጽ ጠፍቷል።

12ከተማዪቱ ፈጽማ ፈርሳለች፤

በሮቿም ደቅቀው ወድቀዋል።

13የወይራ ዛፍ ሲመታ፣

የወይንም ዘለላ ሲቈረጥ ቃርሚያ እንደሚቀር ሁሉ፣

በምድሪቱ ላይ፣

በሕዝቦችም ላይ እንዲሁ ይሆናል።

14ድምፃቸውን ከፍ ያደርጋሉ፤ በደስታም ይጮኻሉ፤

ከምዕራብም የእግዚአብሔርን ክብር ያስተጋባሉ።

15ስለዚህ በምሥራቅ ለእግዚአብሔር ክብር ስጡ፤

ከባሕር ደሴቶችም፣

የእስራኤልን አምላክ፣ የእግዚአብሔርን ስም ከፍ ከፍ አድርጉ።

16“ለጻድቁ ክብር ይሁን” የሚል ዝማሬ፣

ከምድር ዳርቻ ሰማን፤

እኔ ግን፣ “ከሳሁ፤ መነመንሁ፤

ወዮልኝ!

ከዳተኞች አሳልፈው ሰጡ፤

ከዳተኞች በክሕደታቸው አሳልፈው ሰጡ” አልሁ።

17በምድር የምትኖር ሕዝብ ሆይ፤

ሽብር፣ ጕድጓድና ወጥመድ ይጠብቁሃል።

18ከሽብር ድምፅ የሚሸሽ፣

ወደ ጕድጓድ ይገባል፤

ከጕድጓድ የወጣም፣

በወጥመድ ይያዛል።

የሰማይ መስኮቶች ተከፍተዋልና፤

የምድርም መሠረት ተናወጠ።

19ምድር ተከፈለች፤

ምድር ተሰነጠቀች፤

ምድር ፈጽማ ተናወጠች።

20ምድር እንደ ሰካራም ዞረባት፤

ነፋስ እንደሚወዘውዘውም ጐጆ ሆነች፣

የዐመፅዋ ሸክም ከባድ ስለሆነ ትወድቃለች፤

እንደ ገናም አትነሣም።

21በዚያ ቀን እግዚአብሔር

በላይ በሰማያት ያሉትን ኀይሎች፣

በታችም በምድር ያሉትን ነገሥታት ይቀጣቸዋል።

22በጕድጓድ ውስጥ እንዳሉ እስረኞች፣

በአንድ ላይ ይታጐራሉ፤

በእስር ቤት ይዘጋባቸዋል24፥22 ወይም፣ ይላቀቃሉ

ከብዙ ቀንም በኋላ ለፍርድ ይቀርባሉ።

23የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

በጽዮን ተራራና በኢየሩሳሌም፣

በሽማግሌዎቹም ፊት በክብሩ ይነግሣል፤

ጨረቃ ትሸማቀቃለች፤ ፀሓይም ታፍራለች።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 24:1-23

Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi

1Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi

ndi kulisandutsa chipululu;

Iye adzasakaza maonekedwe ake

ndi kumwaza anthu ake onse.

2Aliyense zidzamuchitikira mofanana:

wansembe chimodzimodzi munthu wamba,

antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,

antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,

wogula chimodzimodzi wogulitsa,

wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,

okongola chimodzimodzi okongoza.

3Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu

ndi kusakazikiratu.

Yehova wanena mawu awa.

4Dziko lapansi likulira ndipo likufota,

dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,

anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.

5Anthu ayipitsa dziko lapansi;

posamvera malangizo ake;

pophwanya mawu ake

ndi pangano lake lamuyaya.

6Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;

anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,

iwo asakazika

ndipo atsala ochepa okha.

7Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;

onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.

8Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,

phokoso la anthu osangalala latha,

zeze wosangalatsa wati zii.

9Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;

akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.

10Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;

nyumba iliyonse yatsekedwa.

11Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;

chimwemwe chonse chatheratu,

palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.

12Mzinda wasanduka bwinja

zipata zake zagumuka.

13Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi

ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.

Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,

kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.

14Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;

anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.

15Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;

ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.

16Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda

“Wolungamayo.”

Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!

Tsoka kwa ine!

Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,

inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”

17Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje

ndi msampha zikukudikirani.

18Aliyense wothawa phokoso la zoopsa

adzagwa mʼdzenje;

ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo

adzakodwa ndi msampha.

Zitseko zakumwamba zatsekulidwa,

ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.

19Dziko lapansi lathyokathyoka,

ndipo lagawika pakati,

dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.

20Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera

likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba;

lalemedwa ndi machimo ake.

Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.

21Tsiku limenelo Yehova adzalanga

amphamvu a kumwamba

ndiponso mafumu apansi pano.

22Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi

ngati amʼndende amene ali mʼdzenje.

Adzawatsekera mʼndende

ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.

23Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi;

pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira;

pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu,

ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.