ኢሳይያስ 22 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 22:1-25

ስለ ኢየሩሳሌም የተነገረ ትንቢት

1ስለ ራእይ ሸለቆ የተነገረ ንግር፤

እስቲ ምን ቢጨንቃችሁ ነው

ሁላችሁም ሰገነት ላይ የወጣችሁት?

2አንቺ ጫጫታ የሞላብሽ ከተማ፤

የውካታና የፈንጠዝያ ከተማ ሆይ፤

የተገደሉብሽ በሰይፍ የተሠዉ አይደሉም፤

በጦርነትም አልሞቱም።

3መሪዎችሽ በሙሉ በአንድ ላይ ሸሽተዋል፤

ቀስት እንኳ ሳያነሡ ተማርከዋል፤

ጠላት ገና በሩቅ ሳለ የሸሻችሁ ሁሉ፣

ተይዛችሁ በአንድነት ታስራችኋል።

4ስለዚህ፣ “ከእኔ ራቁ፤

አምርሬ ላልቅስበት፣

ስለ ሕዝቤ ጥፋት፣

ልታጽናኑኝ አትሞክሩ” አልሁ።

5ጌታ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

በራእይ ሸለቆ፣

የመጯጯኺያ፣ የመረገጥና የሽብር፣

ቅጥሮችን የማፈራረስ፣

ወደ ተራሮችም የሚጮኽበት ቀን አለው።

6ኤላም የፍላጻ ሰገባ፣

ፈረሷንና ሠረገላዋን አዘጋጀች፤

ቂርም ጋሻዋን አነገበች።

7መልካሞቹ ሸለቆዎችሽ በሠረገሎች ተሞልተዋል፤

ፈረሰኞችም በከተማዪቱ በሮች ላይ ቆመዋል፤

8የይሁዳን መከላከያዎች ገልጧል።

በዚያን ቀን በዱር ግምጃ ቤት የነበረውን፣

የጦር መሣሪያ ተመለከትህ፤

9የዳዊት ከተማ

ብዙ ፍርስራሾች እንዳሉበት አያችሁ፤

በታችኛውም ኵሬ፣

ውሃ አጠራቀማችሁ።

10በኢየሩሳሌም ያሉትን ቤቶች ቈጠራችሁ፤

ቅጥሩን ለመጠገንም ቤቶቹን አፈረሳችሁ።

11ለጥንቱ ኵሬ ውሃ የሚሆን፣

በሁለቱ ቅጥሮች መካከል ውሃ ማጠራቀሚያ ሠራችሁ፤

ነገር ግን ይህን ያደረገውን አልተመለከታችሁም፤

ቀድሞ ዐቅዶ የሠራውንም አላስታወሳችሁም።

12በዚያን ቀን ጌታ፣ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

እንድታለቅሱና በዋይታ እንድትጮኹ፣

ጠጕራችሁን እንድትነጩ

ማቅም እንድትለብሱ ጠራችሁ።

13ነገር ግን እነሆ፤ ተድላና ደስታ፣

ፍሪዳ መጣልና ሙክት ማረድ፣

ሥጋ መብላትና የወይን ጠጅ መጠጣት አለ፤

“እንብላ እንጠጣ፣

ነገ እንሞታለንና” አላችሁ።

14የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር ይህን ገለጠልኝ፤ እንዲህም ሲል በጆሮዬ ሰማሁ፤ “ይህ ኀጢአት እስከምትሞቱበት ቀን ድረስ አይሰረይላችሁም” ይላል ጌታ፣ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

15ጌታ፣ የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“ሂድና ይህን መጋቢ፣

የቤቱንም ኀላፊ ሳምናስን እንዲህ በለው፤

16‘እዚህ ምን ታደርጋለህ?

በዚህ ስፍራ ለራስህ መቃብርን እንድታዘጋጅ፣

በከፍታውም ላይ መቀበሪያህን እንድትወቅር፣

ሬሳህ የሚያርፍበትንም ዐለት እንድትጠርብ ማን ፈቀደልህ?’

17“አንተ ኀያል ሰው ሆይ፤ ተጠንቀቅ፤

እግዚአብሔር አጥብቆ ሊይዝህ፣ በእጆቹም ጨብጦ ሊወረውርህ ነው።

18አዙሮ አዙሮ እንደ ሩር አጡዞ፣

ወደ ሰፊ አገር ይወነጭፍሃል፤

አንተ የጌታህ ቤት ዕፍረት!

በዚያ ትሞታለህ፤

የክብር ሠረገሎችህም እዚያ ይቀራሉ።

19ከማዕረግህ አወርድሃለሁ፤

ከኀላፊነትህም ትባረራለህ።

20“በዚያን ቀን አገልጋዬን፣ የኬልቅያስን ልጅ ኤልያቄምን እጠራለሁ፤ 21መጐናጸፊያህን አለብሰዋለሁ፤ መታጠቂያህን አስታጥቀዋለሁ፤ ሥልጣንህንም አስረክበዋለሁ። እርሱም በኢየሩሳሌም ለሚኖሩ፣ ለይሁዳም ቤት አባት ይሆናል። 22የዳዊትን ቤት መክፈቻ በጫንቃው ላይ አደርጋለሁ፤ እርሱ የሚከፍተውን ማንም አይዘጋም፤ የሚዘጋውንም ማንም አይከፍትም። 23በአስተማማኝ ስፍራ እንደ ካስማ እተክለዋለሁ፤ ለአባቱም ቤት የክብር ዙፋን22፥23 ወይም፣ መቀመጫ ተብሎ መተርጐም ይችላል። ይሆናል። 24የቤተ ሰቡ ክብር፣ ልጅና የልጅ ልጅ፣ እንዲሁም ከማሰሮ ጀምሮ እስከ ጋን ድረስ ያለ የቤት ዕቃ ሁሉ በእርሱ ላይ ይንጠለጠላል።

25“በዚያ ቀን” ይላል የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር፣ “በአስተማማኝ ስፍራ የተተከለ ካስማ ይነቀላል፤ ተሰብሮም ይወድቃል፤ በእርሱም ላይ የተንጠለጠለው ሸክም ወድቆ ይከሰከሳል፤” እግዚአብሔር ይህን ተናግሯልና።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 22:1-25

Za Chilango cha Yerusalemu

1Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya:

Kodi chachitika nʼchiyani,

kuti nonsenu mukwere pa madenga?

2Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya,

iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera?

Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga,

kapena kufera pa nkhondo.

3Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi;

koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe.

Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo,

ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.

4Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga;

ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa.

Musayesere kunditonthoza

chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”

5Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione

mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo

mʼChigwa cha Masomphenya.

Malinga agumuka,

komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.

6Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta

ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja.

Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.

7Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta,

ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;

8zonse zoteteza Yuda zachotsedwa.

Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana

zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;

9inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide

anali ndi malo ambiri ogumuka;

munasunga madzi

mu chidziwe chakumunsi.

10Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu

ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.

11Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime

chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale,

koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi,

kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.

12Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi;

kumeta mutu wanu mpala

ndi kuvala ziguduli.

13Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala;

munapha ngʼombe ndi nkhosa;

munadya nyama ndi kumwa vinyo.

Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa

pakuti mawa tifa!”

14Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.

15Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo,

amene amayangʼanira nyumba yaufumu:

16Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo

kuti udzikumbire manda kuno,

kudzikumbira manda pa phiri

ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?

17“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba

ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.

18Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira

ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu.

Kumeneko ndiko ukafere

ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako.

Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.

19Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako

ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.

20“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya. 21Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda. 22Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula. 23Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye. 24Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.

25“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’ ” Yehova wayankhula chomwechi.