ኢሳይያስ 21 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 21:1-17

በባቢሎን ላይ የተነገረ ትንቢት

1በባሕሩ ዳር ባለው ምድረ በዳ ላይ የተነገረ ንግር፤

ዐውሎ ነፋስ ከደቡብ እየጠራረገ እንደሚመጣ፣

ወራሪ ከአሸባሪ ምድር፣

ከምድረ በዳ ይመጣል።

2የሚያስጨንቅ ራእይ አየሁ፤

ከሓዲ አሳልፎ ይሰጣል፤ ዘራፊ ይዘርፋል።

ኤላም ሆይ፤ ተነሺ፤ ሜዶን ሆይ፤ ክበቢ፤

እርሷ ያደረሰችውን ሥቃይ ሁሉ አስቀራለሁ።

3ወገቤ በዚህ ሥቃይ ተሞላ፤

በምጥ ላይ እንዳለች ሴት ጭንቅ ያዘኝ፤

በሰማሁት ነገር ተንገዳገድሁ፤

ባየሁትም ነገር ተሸበርሁ።

4ልቤ ተናወጠ፤

ፍርሀት አንቀጠቀጠኝ፤

የጓጓሁለት ውጋጋን፣

ታላቅ ፍርሀት አሳደረብኝ።

5ማእዱን አሰናዱ፤

ምንጣፉን አነጠፉ፤

በሉ፤ ጠጡ!

እናንት ሹማምት ተነሡ፤

ጋሻውን በዘይት ወልውሉ!

6ጌታ እንዲህ አለኝ፤

“ሂድ፤ ጠባቂ አቁም፤

ያየውንም ይናገር፤

7በፈረሶች የሚሳብ፣

ሠረገሎችን ሲያይ፣

በአህያ ላይ የሚቀመጡትን፣

በግመል የሚጋልቡትን ሲመለከት፣

ያስተውል፤

በጥንቃቄም ያስተውል።”

8ጠባቂው ጮኸ፤21፥8 የሙት ባሕር ጥቅልልና የሱርስቱ ቅጅ ከዚህ ጋር ይስማማል፤ የማሶሬቱ ቅጅ ግን፣ አንበሳ ጮኸ ይላል። እንዲህም አለ፤

“ጌታ ሆይ፤ በየቀኑ ማማ ላይ ቆሜአለሁ፤

በየሌሊቱም በቦታዬ አለሁ።

9እነሆ፤ አንድ ሰው በፈረሶች በሚሳብ

በሠረገላ መጥቷል፤

እንዲህም ሲል መለሰ፣

‘ባቢሎን ወደቀች፣ ወደቀች!

የአማልክቷም ምስሎች ሁሉ፣

ተሰባብረው ምድር ላይ ወደቁ!’ ”

10በዐውድማ ላይ የተወቃህ ሕዝቤ ሆይ፤

ከሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

ከእስራኤል አምላክ፣

የሰማሁትን እነግርሃለሁ።

በኤዶም ላይ የተነገረ ትንቢት

11ስለ ኤዶም የተነገረ ንግር፤

አንዱ ከሴይር ጠርቶኝ፣

“ጠባቂ ሆይ፤ ሊነጋ ምን ያህል ቀረው?

ጠባቂ ሆይ፤ ሊነጋ ምን ያህል ቀረው?” አለኝ።

12ጠባቂውም መለሰ፤

“ይነጋል፤ ግን ተመልሶ ይመሻል፤

መጠየቅ ከፈለጋችሁ፣ ጠይቁ፤

ነገር ግን ተመልሳችሁ ኑ” አለ።

በዐረብ ላይ የተነገረ ትንቢት

13ስለ ዐረብ አገር የተነገረ ንግር፤

እናንተ በዐረብ ዱር የምትሰፍሩ፣

የድዳን ሲራራ ነጋዴዎች፣

14ለተጠሙ ውሃ አምጡ።

በቴማን የምትኖሩ፣

ለስደተኞች ምግብ አምጡ።

15ከሰይፍ፣

ከተመዘዘ ሰይፍ፣

ከተደገነ ቀስት፣

ከተፋፋመ ጦርነት ሸሽተዋልና።

16ጌታም እንዲህ አለኝ፤ “በውል የተቀጠረ ሠራተኛ ቀን እንደሚቈጥር፣ የቄዳር ክብር በአንድ ዓመት ውስጥ ያበቃለታል። 17የተረፈው ቀስተኛ፣ የቄዳር ጦረኛ ጥቂት ይሆናል፤ የእስራኤል አምላክ እግዚአብሔር ተናግሯልና።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 21:1-17

Za Chilango cha Babuloni

1Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja.

Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja,

kuchokera ku chipululu,

dziko lochititsa mantha.

2Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya:

Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga.

Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda!

Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.

3Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha,

ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka;

ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva,

ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.

4Mtima wanga ukugunda,

ndipo ndikunjenjemera ndi mantha;

chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna

chasanduka chinthu choopsa kwa ine.

5Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo,

akuyala mphasa,

akudya komanso kumwa!

Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo,

pakani mafuta zishango zanu!”

6Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi;

“Pita, kayike mlonda

kuti azinena zimene akuziona.

7Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo

ndipo akuyenda awiriawiri,

okwera pa bulu

kapena okwera pa ngamira,

mlondayo akhale tcheru kwambiri.”

8Ndipo mlondayo anafuwula kuti,

“Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera;

Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.

9Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta

ali ndi gulu la akavalo.

Mmodzi wa iwo akuti,

‘Babuloni wagwa, wagwa!

Mafano onse a milungu yake

agwa pansi ndipo aphwanyika!’ ”

10Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu,

ine ndikukuwuzani zimene ndamva

ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,

Mulungu wa Israeli.

Za Chilango cha Edomu

11Uthenga wonena za Duma:

Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti,

“Iwe mlonda, usikuwu utha liti?

Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”

12Mlonda akuyankha kuti,

“Kukucha, koma kudanso.

Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano;

ndipo ubwerenso udzafunse.”

Za Chilango cha Arabiya

13Uthenga wonena za Arabiya:

Inu anthu amalonda a ku Dedani,

amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,

14perekani madzi kwa anthu aludzu.

Inu anthu a ku Tema

perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.

15Iwo akuthawa malupanga,

lupanga losololedwa,

akuthawa uta wokokakoka

ndiponso nkhondo yoopsa.

16Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu. 17Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.