ኢሳይያስ 17 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ኢሳይያስ 17:1-14

በደማስቆ ላይ የተነገረ ንግር

1ስለ ደማስቆ የተነገረ ንግር፤

“እነሆ፤ ደማስቆ ከእንግዲህ ከተማነቷ ይቀራል፤

የፍርስራሽ ክምር ትሆናለች።

2የአሮኤር ከተሞች ባድማ ይሆናሉ፤

የመንጎች መሰማሪያ ይሆናሉ፤

የሚያስፈራቸውም የለም።

3የተመሸገ ከተማ ከኤፍሬም፣

የመንግሥት ሥልጣን ከደማስቆ ይወርዳል፤

የሶርያም ቅሬታ

እንደ እስራኤላውያን ክብር ይሆናል”

ይላል የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር

4“በዚያን ቀን የያዕቆብ ክብር ይደበዝዛል፤

የሰውነቱም ውፍረት ይሟሽሻል።

5ዐጫጅ የቆመውን ሰብል ሰብስቦ፣

ዛላውንም በክንዱ እንደሚያጭድ፣

ይህም በራፋይም ሸለቆ

እንደሚለቀም ቃርሚያ ይሆናል።

6ሆኖም የወይራ ዛፍ ሲመታ፣

ሁለት ወይም ሦስት ፍሬ በቅርንጫፍ ራስ ላይ እንደሚቀር፣

አራት ወይም አምስት ፍሬ ችፍግ ባለው ቅርንጫፍ ላይ እንደሚቀር፣

እንዲሁ ጥቂት ቃርሚያ ይተርፋል”

ይላል የእስራኤል አምላክ እግዚአብሔር

7በዚያ ቀን ሰዎች ወደ ፈጣሪያቸው ይመለከታሉ፤

ዐይኖቻቸውም ወደ እስራኤል ቅዱስ ያያሉ።

8በእጃቸውም ወደ ሠሯቸው መሠዊያዎች አይመለከቱም፤

በጣቶቻቸው ላበጇቸው የዕጣን መሠዊያዎች፣

ለአሼራም የአምልኮ ዐምዶች

ክብር አይሰጡም።

9በዚያን ቀን በእስራኤል ልጆች ምክንያት የተተዉት ጠንካራ ከተሞች ጥሻና ውድማ እንደ ሆኑ ሁሉ፣ እነዚህ ሁሉ ባድማ ይሆናሉ።

10አዳኝ አምላክህን ረስተሃል፤

መሸሸጊያ ዐለትህንም አላስታወስህም፤

ስለዚህ ምርጥ ተክል ብትተክልም፣

እንግዳ ዘርንም ብትዘራ፣

11በተከልህበት ቀን እንዲበቅል፣

በዘራህበትም ማግስት እንዲያብብ ብታደርግ እንኳ፣

መከሩ በደዌና በማይሽር ሕመም ቀን፣

እንዳልነበረ ይሆናል።

12አቤት፤ የብዙ ሕዝቦች የቍጣ ድምፅ

እንደ ባሕር ሞገድ ይጮኻል!

አቤት፤ የሰዎች ከፍተኛ ጩኸት

እንደ ኀይለኛ ውሃ ያስገመግማል!

13ሰዎቹ እንደ ኀይለኛ ውሃ ጩኸት ቢያስገመግሙም፣

እርሱ ሲገሥጻቸው፣

በኰረብታ ላይ በነፋስ እንደሚበንን ትቢያ፣

በዐውሎ ነፋስ ፊት እንደሚበተን ገለባ ይበተናሉ።

14እነሆ፤ ሲመሽ ድንገተኛ ሽብር ሆነ!

ከመንጋቱ በፊት ግን አንዳቸውም አልተገኙም።

የዘረፉን ዕድል ፈንታ፣

የበዘበዙን ዕጣ ይህ ሆነ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.