ናሆም 3 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ናሆም 3:1-19

ለነነዌ

1ለደም ከተማ ወዮላት!

ሐሰት፣ ዘረፋም ሞልቶባታል፤

ብዝበዛዋ ተግዞ አያልቅም።

2የጅራፍ ድምፅ፣

የመንኰራኵር ኳኳቴ፣

የፈጣን ፈረስ ኰቴ፣

የሠረገሎች ድምፅ ተሰምቷል።

3ፈረሰኛው ይጋልባል፤

ሰይፍ ይንቦገቦጋል፤

ጦር ያብረቀርቃል።

የሞተው ብዙ ነው፤

ሬሳ በሬሳ ሆኗል፤

ስፍር ቍጥር የለውም፤

መተላለፊያ አልተገኘም።

4ይህ ሁሉ የሆነው ቅጥ ባጣች፣

አሳሳችና መተተኛ በሆነች ዘማዊት ምክንያት ነው፤

እርሷም በዝሙቷ አሕዛብን፣

በጥንቈላዋም ሕዝቦችን ባሪያ ያደረገች ናት።

5የሰራዊት ጌታ እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“እኔ በጠላትነት ተነሥቼብሻለሁ፤

ቀሚስሽን እስከ ፊትሽ እገልበዋለሁ፤

ዕርቃንሽን ለአሕዛብ፣

ኀፍረትሽንም ለነገሥታት አሳያለሁ።

6ቈሻሻ እደፋብሻለሁ፤

እንቅሻለሁ፤

ማላገጫም አደርግሻለሁ።

7የሚያዩሽ ሁሉ ከአንቺ እየሸሹ፣

‘ነነዌ ፈራርሳለች፤ ማን ያለቅስላታል?’ ይላሉ፤

የሚያጽናናሽንስ ከወዴት አገኛለሁ?”

8አንቺ በአባይ ወንዝ አጠገብ ካለችው፣

በውሃ ከተከበበችው፣

ከኖእ አሞን3፥8 አንዳንዶች ቴብስ ይላሉ። ትበልጫለሽን?

ወንዙ መከላከያዋ፣

ውሃውም ቅጥሯ ነው።

9ኢትዮጵያና ግብፅ ወሰን የለሽ ኀይሏ ናቸው፤

ፉጥና ሊቢያም ረዳቶቿ ነበሩ።

10ይሁን እንጂ በምርኮ ተወሰደች፤

ተሰድዳም ሄደች።

በየመንገዱ ማእዘን ላይ፣

ሕፃናቷ ተፈጠፈጡ፤

በመሳፍንቷ ላይ ዕጣ ተጣለ፤

ታላላቅ ሰዎቿ ሁሉ በሰንሰለት ታሰሩ።

11አንቺ ደግሞ ትሰክሪአለሽ፤

ትደበቂአለሽ፣

ከጠላትም መሸሸጊያ ትፈልጊአለሽ።

12ምሽጎችሽ ሁሉ ሊበሉ እንደ ደረሱ

የመጀመሪያ በለስ ፍሬ ናቸው፤

በሚወዛወዙበት ጊዜ፣

ፍሬዎቹ በበላተኛው አፍ ውስጥ ይወድቃሉ።

13እነሆ፤ ጭፍሮችሽ፣

ሁሉም ሴቶች ናቸው!

የምድርሽ በሮች፣

ለጠላቶችሽ ወለል ብለው ተከፍተዋል፤

መዝጊያዎቻቸውንም እሳት በልቷቸዋል።

14ለከበባው ውሃ ቅጅ፤

መከላከያሽን አጠናክሪ፤

የሸክላውን ዐፈር ፈልጊ፤

ጭቃውን ርገጪ፤

ጡቡንም ሥሪ።

15በዚያ እሳት ይበላሻል፤

ሰይፍ ይቈርጥሻል፤

እንደ ኵብኵባም ይግጥሻል።

እንደ ኵብኵባ እርቢ፤

እንደ አንበጣም ተባዢ።

16ከሰማይ ከዋክብት እስኪበልጡ ድረስ፣

የነጋዴዎችሽን ቍጥር አበዛሽ፤

ምድሪቱን ግን እንደ አንበጣ ግጠው አሟጠጡ፤

ከዚያም በርረው ሄዱ።

17ጠባቂዎችሽ እንደ አንበጣ፣

መኳንንትሽም በብርድ ቀን

በቅጥር ሥር እንደሚቀመጥ ኵብኵባ ናቸው፤

ፀሓይ ሲወጣ ግን ይበርራሉ፤

የት እንደሚበርሩም አይታወቅም።

18የአሦር ንጉሥ ሆይ፤ እረኞችህ3፥18 ገዦች ማለት ነው። አንቀላፉ፤

መኳንንትህ ዐርፈው ተኙ፤

ሕዝብህ ሰብሳቢ ዐጥተው፣

በተራራ ላይ ተበትነዋል።

19ቍስልህን ሊፈውስ የሚችል የለም፤

ስብራትህም ለሞት የሚያደርስ ነው።

ስለ አንተ የሰማ ሁሉ፣

በውድቀትህ ደስ ብሎት ያጨበጭባል፤

ወሰን የሌለው ጭካኔህ

ያልነካው ማን አለና?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 3:1-19

Tsoka la Ninive

1Tsoka kwa mzinda wopha anthu,

mzinda wodzaza ndi mabodza,

mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo,

mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!

2Kulira kwa zikwapu,

mkokomo wa mikombero,

kufuwula kwa akavalo

ndiponso phokoso la magaleta!

3Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo,

kungʼanima kwa malupanga

ndi kunyezimira kwa mikondo!

Anthu ambiri ophedwa,

milumilu ya anthu akufa,

mitembo yosawerengeka,

anthu akupunthwa pa mitemboyo.

4Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere,

wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga,

amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake,

ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndikutsutsana nawe.

Ndidzakuvula chovala chako.

Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako

ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.

6Ndidzakuthira zonyansa,

ndidzakuchititsa manyazi

ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.

7Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati,

‘Ninive wasanduka bwinja,

adzamulira ndani?’

Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”

8Kodi ndiwe wopambana Tebesi,

mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo,

wozunguliridwa ndi madzi?

Mtsinjewo unali chitetezo chake,

madziwo anali linga lake.

9Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto,

Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.

10Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa

ndipo anapita ku ukapolo.

Ana ake anawaphwanyitsa pansi

mʼmisewu yonse ya mu mzindamo.

Anachita maere ogawana anthu ake otchuka,

ndipo anthu ake onse amphamvu

anamangidwa ndi maunyolo.

11Iwenso Ninive udzaledzera;

udzabisala

ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.

12Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu

yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha;

pamene agwedeza mitengoyo,

nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.

13Tayangʼana ankhondo ako,

onse ali ngati akazi!

Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako;

moto wapsereza mipiringidzo yake.

14Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu,

limbitsani chitetezo chanu!

Pondani dothi,

ikani mʼchikombole,

konzani khoma la njerwa!

15Kumeneko moto udzakupserezani;

lupanga lidzakukanthani

ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala.

Chulukanani ngati ziwala,

chulukanani ngati dzombe!

16Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu

mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga,

koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko

ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.

17Akalonga ako ali ngati dzombe,

akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe

limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira,

koma pamene dzuwa latuluka limawuluka,

ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.

18Iwe mfumu ya ku Asiriya,

abusa ako agona tulo;

anthu ako olemekezeka amwalira.

Anthu ako amwazikira ku mapiri

popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.

19Palibe chimene chingachize bala lako;

chilonda chako sichingapole.

Aliyense amene amamva za iwe

amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako,

kodi alipo amene sanazilawepo

nkhanza zako zosatha?