ምሳሌ 7 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ምሳሌ 7:1-27

ከአመንዝራ ሴት መራቅ

1ልጄ ሆይ፤ ቃሌን ጠብቅ፤

ትእዛዜንም በውስጥህ አኑር።

2ትእዛዜን ጠብቅ፤ በሕይወት ትኖራለህ፤

ትምህርቴንም እንደ ዐይንህ ብሌን ተንከባከበው።

3በጣትህ ላይ እሰረው፤

በልብህ ጽላት ላይ ጻፈው።

4ጥበብን፣ “እኅቴ ነሽ” በላት፤

ማስተዋልንም፣ “ዘመዴ ነህ” በለው፤

5ከአመንዝራ ሴት፣

በአንደበቷም ከምታታልል ዘልዛላ ሴት ይጠብቁሃል።

6በቤቴ መስኮት፣

በዐይነ ርግቡ ወደ ውጭ ተመለከትሁ።

7ማስተዋል የጐደለውን ወጣት፣

ብስለት ከሌላቸው መካከል አየሁት፤

ከጕልማሶችም መካከል ለየሁት።

8የቤቷን አቅጣጫ ይዞ፣

በቤቷ ማእዘን አጠገብ ባለው መንገድ ያልፍ ነበር፤

9ቀኑ መሸትሸት ሲል፣

በውድቅት ሌሊት፣ በጽኑ ጨለማ።

10ከዚያም አንዲት ሴት ልታገኘው ወጣች፤

እንደ ዝሙት ዐዳሪ ለብሳ፣ ለማሳሳት ታጥቃ።

11ጯኺና ማን አለብኝ ባይ ናት፤

እግሮቿ ዐርፈው ቤት አይቀመጡም፤

12አንዴ በመንገድ፣ አንዴ በአደባባይ፣

በየማእዘኑም ታደባለች።

13አፈፍ አድርጋ ይዛ ሳመችው፤

ኀፍረቷንም ጥላ እንዲህ አለችው፤

14“በቤቴ የኅብረት መሥዋዕት7፥14 በተለምዶ የሰላም መሥዋዕት ይባላል። ማቅረብ ነበረብኝ፤

ዛሬ ስእለቴን ፈጸምሁ፤

15ስለዚህ አንተን ለማግኘት ወጣሁ፤

ፈልጌህ ነበር፤ ይኸው አገኘሁህ።

16ዐልጋዬን ከግብፅ የመጣ፣

ጌጠኛ በፍታ አልብሼዋለሁ።

17ዐልጋዬን፣

የከርቤ፣ የዓልሙንና የቀረፋ ሽቱ አርከፍክፌበታለሁ።

18ና፤ እስኪነጋ በጥልቅ ፍቅር እንርካ፤

በፍቅር ራሳችንን እናስደስት።

19ባሌ እቤት የለም፤

ሩቅ አገር ሄዷል።

20በገንዘብ የተሞላ ቦርሳ ወስዷል፤

ጨረቃዋ ሙሉ እስክትሆን አይመለስም።”

21በሚያግባቡ ቃላት አሳተችው፤

በለሰለሰ አንደበቷ አታለለችው።

22ለዕርድ እንደሚነዳ በሬ፣

ወደ ወጥመድ7፥22 የሱርሰት (የሰብዓ ሊቃናትም) ትርጕም እና ዕብራይስጡ ተላላ ይላሉ። እንደሚገባ አጋዘን፣7፥22 የዚህ ስንኝ የዕብራይስጡ ትርጓሜ በርግጠኝነት አይታወቅም።

ሳያንገራግር ተከተላት፤

23ፍላጻ ጕበቱን እስኪወጋው ድረስ፣

ሕይወቱን እንደሚያሳጣው ሳያውቅ፣

በርራ ወደ ወጥመድ እንደምትገባ ወፍ ሆነ።

24ልጆቼ ሆይ፤ አሁንም አድምጡኝ፤

የምለውንም ልብ ብላችሁ ስሙኝ።

25ልባችሁን ወደ መንገዷ አታዘንብሉ፤

ወደ ስሕተት ጐዳናዋም አትግቡ።

26አዋርዳ የጣለቻቸው ብዙ ናቸው፤

የገደለቻቸውም ስፍር ቍጥር የላቸውም።

27ቤቷ ወደ ሲኦል7፥27 ወይም መቃብር የሚወስድ፣

ወደ ሞት ማደሪያም የሚያወርድ ጐዳና ነው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 7:1-27

Za Mkazi Wachigololo

1Mwana wanga, mvera mawu anga;

usunge bwino malamulo angawa.

2Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo;

samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.

3Uchite ngati wawamangirira pa zala zako,

ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.

4Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,”

ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”

5Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo

ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.

6Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga

ndinasuzumira pa zenera.

7Ndinaona pakati pa anthu opusa,

pakati pa anyamata,

mnyamata wina wopanda nzeru.

8Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo,

kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.

9Inali nthawi yachisisira madzulo,

nthawi ya usiku, kuli mdima.

10Ndipo mkaziyo anadzakumana naye,

atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.

11(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve,

iye ndi wosakhazikika pa khomo.

12Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika,

ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).

13Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona

ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,

14“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano.

Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.

15Choncho ndinabwera kudzakumana nawe;

ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!

16Pa bedi panga ndayalapo

nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.

17Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira

za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.

18Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa;

tiye tisangalatsane mwachikondi!

19Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako;

wapita ulendo wautali:

20Anatenga thumba la ndalama

ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”

21Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo;

amukopa ndi mawu ake oshashalika.

22Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo

ngati ngʼombe yopita kukaphedwa,

monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,

23mpaka muvi utalasa chiwindi chake,

chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe,

osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.

24Tsono ana inu, ndimvereni;

mvetsetsani zimene ndikunena.

25Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu;

musasochere potsata njira zake.

26Paja iye anagwetsa anthu ambiri;

wapha gulu lalikulu la anthu.

27Nyumba yake ndi njira yopita ku manda,

yotsikira ku malo a anthu akufa.