ምሳሌ 28 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ምሳሌ 28:1-28

1ክፉ ሰው ማንም ሳያሳድደው ይሸሻል፤

ጻድቅ ግን እንደ አንበሳ ልበ ሙሉ ነው።

2አገር ስታምፅ፣ ገዦቿ ይበዛሉ፤

አስተዋይና ዐዋቂ ሰው ግን ሥርዐትን ያሰፍናል።

3ድኾችን የሚያስጨንቅ ሰው፣28፥3 ወይም ድኻ

ሰብል እንደሚያጠፋ ኀይለኛ ዝናብ ነው።

4ሕግን የሚተዉ ክፉዎችን ያወድሳሉ፤

ሕግን የሚጠብቁ ግን ይቋቋሟቸዋል።

5ክፉዎች ፍትሕን አያስተውሉም፤

እግዚአብሔርን የሚሹ ግን ሙሉ በሙሉ ያውቁታል።

6በአካሄዱ ነውር የሌለበት ድኻ፣

መንገዱ ጠማማ ከሆነ ባለጠጋ ይሻላል።

7ሕግን የሚጠብቅ አስተዋይ ልጅ ነው፤

ከሆዳሞች ጋር ጓደኛ የሚሆን ግን አባቱን ያዋርዳል።

8በከፍተኛ ወለድ ሀብቱን የሚያካብት፣

ለድኻ ለሚራራ፣ ለሌላው ሰው ያከማችለታል።

9ሕግን ላለመስማት ጆሮውን የሚደፍን፣

ጸሎቱ እንኳ አስጸያፊ ነው።

10ቅኖችን በክፉ መንገድ የሚመራ፣

በቈፈረው ጕድጓድ ይገባል፤

ንጹሓን ግን መልካም ነገርን ይወርሳሉ።

11ባለጠጋ ራሱን ጠቢብ አድርጎ ይቈጥር ይሆናል፤

አስተዋይ የሆነ ድኻ ግን መርምሮ ያውቀዋል።

12ጻድቃን ድል ሲነሡ ታላቅ ደስታ ይሆናል፤

ክፉዎች ሥልጣን ሲይዙ ግን ሕዝብ ይሸሸጋል።

13ኀጢአቱን የሚሰውር አይለማም፤

የሚናዘዝና የሚተወው ግን ምሕረትን ያገኛል።

14እግዚአብሔርን ዘወትር የሚፈራ ሰው ቡሩክ ነው፤

ልቡን የሚያደነድን ግን መከራ ላይ ይወድቃል።

15ታዳጊ በሌለው ሕዝብ ላይ የተሾመ ጨካኝ ገዥ፣

እንደሚያገሣ አንበሳ ወይም ተንደርድሮ እንደሚይዝ ድብ ነው።

16ጨካኝ ገዥ ማመዛዘን ይጐድለዋል፤

አለአግባብ የሚገኝን ጥቅም የሚጸየፍ ግን ዕድሜው ይረዝማል።

17የሰው ደም ያለበት ሰው፣

ዕድሜ ልኩን ሲቅበዘበዝ ይኖራል፤

ማንም ሰው አይርዳው።

18አካሄዱ ነቀፋ የሌለበት ሰው ክፉ አያገኘውም፤

መንገዱ ጠማማ የሆነ ግን ድንገት ይወድቃል።

19መሬቱን የሚያርስ የተትረፈረፈ ምግብ ያገኛል፤

ከንቱ ተስፋን ይዞ የሚጓዝ ግን ድኽነትን ይወርሳል።

20ታማኝ ሰው እጅግ ይባረካል፤

ሀብት ለማግኘት የሚጣደፍ ግን ከቅጣት አያመልጥም።

21አድልዎ ማድረግ መልካም አይደለም፤

ሰው ግን ለቍራሽ እንጀራ ሲል በደል ይፈጽማል።

22ስስታም ሀብት ለማከማቸት ይስገበገባል፤

ድኽነት እንደሚጠብቀውም አያውቅም።

23ሸንጋይ አንደበት ካለው ይልቅ፣

ሰውን የሚገሥጽ ውሎ ዐድሮ ይወደዳል።

24ከአባት ከእናቱ ሰርቆ፣

“ይህ ጥፋት አይደለም” የሚል የአጥፊ ተባባሪ ነው።

25ሥሥታም ሰው ጠብን ያነሣሣል፤

በእግዚአብሔር የሚታመን ግን ይባረካል።

26በራሱ የሚታመን ተላላ ነው፤

በጥበብ የሚመላለስ ግን ክፉ አያገኘውም።

27ለድኾች የሚሰጥ አይቸገርም፤

አይቷቸው እንዳላየ የሚሆን ግን ብዙ ርግማን ይደርስበታል።

28ክፉዎች ሥልጣን በሚይዙ ጊዜ ሕዝብ ይሸሸጋል፤

ክፉዎች በሚጠፉበት ጊዜ ግን ጻድቃን ይበዛሉ።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 28:1-28

1Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,

koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

2Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,

koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake

ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

4Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,

koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,

koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

6Munthu wosauka wa makhalidwe abwino

aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

7Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,

koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

8Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka

amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wokana kumvera malamulo

ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa

adzagwera mu msampha wake womwe,

koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;

koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,

koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,

koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa

ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza

koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu

adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;

wina aliyense asamuthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa

koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,

koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21Kukondera si kwabwino,

ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera

koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake

mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24Amene amabera abambo ake kapena amayi ake

namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”

ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25Munthu wadyera amayambitsa mikangano,

koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,

koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,

koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,

koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.