ምሳሌ 26 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ምሳሌ 26:1-28

1በረዶ በበጋ፣ ዝናብ በመከር እንደማያስፈልግ ሁሉ፣

ክብርም ለተላላ አይገባውም።

2ክንፎቿን እንደምታርገበግብ ድንቢጥ ወይም ቱር እንደምትል ጨረባ፣

ከንቱ ርግማንም በማንም ላይ አይደርስም።

3ለፈረስ ዐለንጋ፣ ለአህያ መሸበቢያ፣

ለተላላ ጀርባም በትር ይገባዋል።

4ቂልን እንደ ቂልነቱ አትመልስለት፤

አለዚያ አንተም ራስህ እንደ እርሱ ትሆናለህ።

5ቂልን እንደ ቂልነቱ መልስለት፤

አለዚያ ጠቢብ የሆነ ይመስለዋል።

6በተላላ እጅ መልእክትን መላክ፣

የገዛ እግርን እንደ መቍረጥ ወይም ዐመፃን እንደ መጋት ነው።

7በቂል አንደበት የሚነገር ምሳሌ፣

ሰላላ የሽባ ሰው እግር ነው።

8ለተላላ ክብር መስጠት፣

በወንጭፍ ላይ ድንጋይ እንደ ማሰር ነው።

9በአላዋቂ አንደበት የሚነገር ምሳሌ፣

በሰካራም እጅ እንዳለ እሾኽ ነው።

10ቂልን ወይም የትኛውንም ዐላፊ አግዳሚ የሚቀጥር፣

ፍላጻውን በነሲብ እየወረወረ ወገኖቹን እንደሚያቈስል ቀስተኛ ነው።

11ውሻ ወደ ትፋቱ እንደሚመለስ ሁሉ፣

ተላላም ቂልነቱን ይደጋግማል።

12ራሱን እንደ ጠቢብ የሚቈጥረውን ሰው አይተሃልን?

ከእርሱ ይልቅ ለተላላ ተስፋ አለው።

13ሰነፍ፣ “በመንገድ ላይ አንበሳ አለ፤

አስፈሪ አንበሳ በአውራ ጐዳና ላይ ይጐማለላል” ይላል።

14መዝጊያ በማጠፊያው ላይ እንደሚዞር፣

ሰነፍም በዐልጋው ላይ ይገላበጣል።

15ሰነፍ እጁን ወጭት ውስጥ ያጠልቃል፤

ወደ አፉ ለመመለስ ግን እጅግ ይታክታል።

16በማስተዋል መልስ ከሚሰጡ ከሰባት ሰዎች ይልቅ፣

ሰነፍ ራሱን ጠቢብ አድርጎ ይቈጥራል።

17በሌሎች ጠብ ጥልቅ የሚል መንገደኛ፣

የውሻ ጆሮ እንደሚይዝ ሰው ነው።

18ትንታግ ወይም የሚገድል ፍላጻ እንደሚወረውር እብድ፣

19“ቀልዴን እኮ ነው” እያለ

ባልንጀራውን የሚያታልል ሰውም እንደዚሁ ነው።

20ዕንጨት ከሌለ እሳት ይጠፋል፤

አሾክሻኪ ከሌለም ጠብ ይበርዳል።

21ከሰል ፍምን፣ ዕንጨትም እሳትን እንደሚያቀጣጥል፣

አዋኪ ሰውም ጠብን ያባብሳል።

22የሐሜተኛ ቃል እንደ ጣፋጭ ጕርሻ ነው፤

ወደ ሰው ውስጠኛው ክፍል ዘልቆ ይገባል።

23ክፋትን በልብ ቋጥሮ ለስላሳ ቃል የሚናገር ከንፈር፣

በብር ፈሳሽ26፥23 ወይም በሚያብለጨልጭ ነገር እንደ ተለበጠ የሸክላ ዕቃ ነው።

24ተንኰለኛ በከንፈሩ ይሸነግላል፤

በልቡ ግን ክፋትን ይቋጥራል።

25ንግግሩ ማራኪ ቢሆንም አትመነው፤

ሰባት ርኩሰት ልቡን ሞልቶታልና።

26ተንኰሉ በሽንገላው ይሸፈን ይሆናል፤

ነገር ግን ክፋቱ በጉባኤ ይገለጣል።

27ጕድጓድ የሚምስ ራሱ ይገባበታል፤

ድንጋይ የሚያንከባልልም ተመልሶ በላዩ ላይ ይገለበጥበታል።

28ሐሰተኛ ምላስ የጐዳቻቸውን ትጠላለች፤

ሸንጋይ አንደበትም ጥፋትን ታመጣለች።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 26:1-28

1Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola,

ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.

2Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira,

ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.

3Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu,

choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.

4Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake,

kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.

5Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake,

kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.

6Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga

kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.

7Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu

ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.

8Kupereka ulemu kwa chitsiru

zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.

9Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa

ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.

10Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda,

ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.

11Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake

chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.

12Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo

kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.

13Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango,

mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”

14Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake,

momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.

15Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale;

zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.

16Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru

kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.

17Munthu wongolowera mikangano imene si yake

ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.

18Monga munthu wamisala amene

akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,

19ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake,

amene amati, “Ndimangoseka chabe!”

20Pakasowa nkhuni, moto umazima;

chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.

21Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto,

ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.

22Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma;

chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.

23Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi

ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.

24Munthu wachidani amayankhula zabwino

pamene mu mtima mwake muli chinyengo.

25Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire,

pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.

26Ngakhale amabisa chidani mochenjera,

koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.

27Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha;

ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.

28Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka,

ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.