ማሕልየ መሓልይ 5 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ማሕልየ መሓልይ 5:1-16

ሙሽራው

1እኅቴ ሙሽራዬ፣ ወደ አትክልት ቦታዬ መጥቻለሁ፤

ከርቤዬን ከቅመሜ ጋር ሰብስቤአለሁ፤

የማር እንጀራዬን ከነወለላው በልቻለሁ፤

ወይኔንና ወተቴንም ጠጥቻለሁ።

ባልንጀሮቿ

ወዳጆች ሆይ፤ ብሉ፤ ጠጡ፤

እናንት ፍቅረኞች ሆይ፤ እስክትረኩ ጠጡ።

ሙሽራዪቱ

2እኔ ተኝቻለሁ፤ ልቤ ግን ነቅቷል፤

ስሙ! ውዴ በር ያንኳኳል፤ እንዲህ ይላል፤

“እኅቴ ወዳጄ፣ ርግቤ፣

አንቺ እንከን የሌለብሽ፤ ክፈቺልኝ።

ራሴ በጤዛ፣

ጠጕሬም በሌሊቱ ርጥበት ረስርሷል።”

3ቀሚሴን አውልቄአለሁ፤

ታዲያ እንዴት እንደ ገና ልልበስ?

እግሬን ታጥቤአለሁ፤

እንዴት እንደ ገና ላቈሽሸው?

4ውዴ እጁን በበሩ ቀዳዳ አሾለከ፤

ልቤም ስለ እርሱ ይታወክ ጀመር።

5ለውዴ ልከፍትለት ተነሣሁ፤

በከርቤ ነጠብጣብ የራሱት እጆቼ፣

በከርቤም ፈሳሽ የተነከሩት ጣቶቼ፣

የመወርወሪያውን እጀታ ያዙ።

6ለውዴ ከፈትሁለት፤

ውዴ ግን አልነበረም፤ ሄዷል፤

በመሄዱም ልቤ ደነገጠ፤5፥6 ወይም በተናገረ ጊዜ ልቤ ወደ እርሱ ሄደ

ፈለግሁት፤ ነገር ግን አላገኘሁትም፤

ጠራሁት፤ ነገር ግን አልመለሰልኝም።

7የከተማዪቱም ጠባቂዎች፣

በከተማዪቱ ውስጥ ሲዘዋወሩ አገኙኝ፤

እነዚህ የቅጥሩ ጠባቂዎች፣

ደበደቡኝ፤ አቈሰሉኝ፤

ልብሴንም ገፈፉኝ።

8እናንት የኢየሩሳሌም ቈነጃጅት ሆይ፤

እማጠናችኋለሁ፤

ውዴን ካገኛችሁት፣

ምን ትሉት መሰላችሁ?

በፍቅሩ መታመሜን ንገሩት።

ባልንጀሮቿ

9አንቺ ከሴቶች ሁሉ የተዋብሽ ሆይ፤

ውድሽ ከሌሎች እንዴት ቢበልጥ ነው?

እስከዚህ የምትማጠኚንስ፣

ውድሽ ከሌሎች እንዴት ቢበልጥ ነው?

ሙሽራዪቱ

10ውዴ ፍልቅልቅና ደመ ግቡ ነው፤

ከዐሥር ሺሆችም የሚልቅ ነው።

11ራሱ የጠራ ወርቅ፣

ጠጕሩ ዞማ፣

እንደ ቍራም የጠቈረ ነው።

12ዐይኖቹ፣

በጅረት አጠገብ እንዳሉ ርግቦች፣

በወተት የታጠቡ፣

እንደ ዕንቍም ጕብ ጕብ ያሉ ናቸው።

13ጕንጮቹ የሽቱ መዐዛ የሚያመጡ፣

የቅመማ ቅመም መደቦችን ይመስላሉ፤

ከንፈሮቹም ከርቤ እንደሚያንጠባጥቡ፣

ውብ አበቦች ናቸው።

14ክንዶቹ በዕንፈርጥ ያጌጠ፣

የወርቅ ዘንግን ይመስላሉ፤

ሰውነቱም በሰንፔር ፈርጥ5፥14 ወይም ላፒስ ላዙሊ ያጌጠ፣

አምሮ የተሠራ የዝኆን ጥርስን ይመስላል።

15እግሮቹ በንጹሕ ወርቅ መቆሚያ ላይ የተተከሉ፣

የዕብነ በረድ ምሰሶዎችን ይመስላሉ፤

መልኩ እንደ ሊባኖስ ነው፤

እንደ ዝግባ ዛፎቹም ምርጥ ነው።

16አፉ ራሱ ጣፋጭ ነው፤

ሁለንተናውም ያማረ ነው።

እናንተ የኢየሩሳሌም ቈነጃጅት ሆይ፤

ውዴ ይህ ነው፤ ባልንጀራዬም እርሱ ነው።

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 5:1-16

Mwamuna

1Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;

ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.

Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;

ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.

Abwenzi

Idyani abwenzi anga, imwani;

Inu okondana, imwani kwambiri.

Mkazi

2Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.

Tamverani, bwenzi langa akugogoda:

“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,

nkhunda yanga, wangwiro wanga.

Mutu wanga wanyowa ndi mame,

tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”

3Ndavula kale zovala zanga,

kodi ndizivalenso?

Ndasamba kale mapazi anga

kodi ndiwadetsenso?

4Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;

mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.

5Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,

ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,

zala zanga zinali mure chuchuchu,

pa zogwirira za chotsekera.

6Ndinamutsekulira wachikondi wanga,

koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.

Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.

Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.

Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.

7Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzindawo.

Anandimenya ndipo anandipweteka;

iwo anandilanda mwinjiro wanga,

alonda a pa khoma aja!

8Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,

mukapeza wokondedwa wangayo,

kodi mudzamuwuza chiyani?

Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.

Abwenzi

9Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?

Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani

kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi

pakati pa anthu 1,000.

11Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;

tsitsi lake ndi lopotanapotana,

ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.

12Maso ake ali ngati nkhunda

mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,

zitayima ngati miyala yamtengowapatali.

13Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya

zopatsa fungo lokoma.

Milomo yake ili ngati maluwa okongola

amene akuchucha mure.

14Manja ake ali ngati ndodo zagolide

zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.

Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu

woyikamo miyala ya safiro.

15Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,

yokhazikika pa maziko a golide.

Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,

abwino kwambiri ngati mkungudza.

16Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;

munthuyo ndi wokongola kwambiri!

Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,

inu akazi a ku Yerusalemu.