ሚክያስ 6 – NASV & CCL

New Amharic Standard Version

ሚክያስ 6:1-16

የእግዚአብሔር ክስ በእስራኤል ላይ

1እግዚአብሔር የሚለውን ስሙ፤

“ተነሡ፤ ጕዳያችሁን በተራሮች ፊት አቅርቡ፤

ኰረብቶች እናንተ የምትሉትን ይስሙ፤

2“ተራሮች ሆይ፤ የእግዚአብሔርን ክስ አድምጡ፤

እናንት የምድር ጽኑ መሠረቶችም፣ ስሙ፤

እግዚአብሔር ከሕዝቡ ጋር ክርክር አለውና፤

ከእስራኤልም ጋር ይፋረዳል።

3“ሕዝቤ ሆይ፤ ምን አድርጌሃለሁ?

ሸክም የሆንሁብህስ እንዴት ነው?

እስቲ መልስልኝ!

4ከግብፅ አወጣሁህ፤

ከባርነት ምድርም ተቤዠሁህ፤

እንዲመሩህ ሙሴን፣

አሮንንና ማርያምን ላክሁልህ።

5ሕዝቤ ሆይ፤

የሞዓብ ንጉሥ ባላቅ የመከረውን፣

የቢዖር ልጅ በለዓም የመለሰለትንም እስቲ አስቡ፤

የእግዚአብሔርን የጽድቅ ሥራ ታውቁ ዘንድ፣

ከሰጢም እስከ ጌልገላ የተጓዛችሁትን ዐስቡ።”

6ምን ይዤ በእግዚአብሔር ፊት ልቅረብ፣

በልዑል አምላክ ፊት ልስገድ?

የሚቃጠለውን መሥዋዕት፣

ከአንድ ዓመት ጥጃ ጋር ይዤ በፊቱ ልቅረብን?

7በአንድ ሺሕ አውራ በጎች፣

በዐሥር ሺሕ የዘይት ፈሳሽ እግዚአብሔር ደስ ይለዋልን?

ስለ በደሌ የበኵር ልጄን፣

ስለ ነፍሴም ኀጢአት የሆዴን ፍሬ ላቅርብለትን?

8ሰው ሆይ፤ መልካም የሆነውን አሳይቶሃል፤

እግዚአብሔር ከአንተ የሚፈልገው ምንድን ነው?

ፍትሕን ታደርግ ዘንድ፣ ምሕረትንም ትወድድ ዘንድ፣

በአምላክህም ፊት በትሕትና ትራመድ ዘንድ አይደለምን?

የእስራኤል በደልና ቅጣት

9ስምህን መፍራት ጥበብ ነው፤

ስሙ! እግዚአብሔር ከተማዪቱን እንዲህ እያለ ይጣራል፤

“በትሩን አስቡ፤ ያዘጋጀውም ማን እንደ ሆነ አስታውሱ6፥9 የዚህ ስንኝ የዕብራይስጡ ትርጕም በርግጠኝነት አይታወቅም።

10የክፋት ቤት ሆይ፤

በግፍ የተገኘ ሀብታችሁን፣

በሐሰተኛ መስፈሪያ የሰበሰባችሁትን አስጸያፊ ነገር እረሳዋለሁን?

11አባይ ሚዛን የያዘውን ሰው፣

ሐሰተኛ መመዘኛ በከረጢት የቋጠረውን ንጹሕ ላድርገውን?

12ባለጠጎቿ ግፈኞች፣

ሰዎቿ ሐሰተኞች ናቸው፤

ምላሳቸውም አታላይ ናት።

13ስለዚህ አንተን አጠፋሃለሁ፣

ከኀጢአትህ የተነሣ አፈራርስሃለሁ።

14ትበላለህ፤ ነገር ግን አትጠግብም፤

ሆድህ እንዳለ ባዶውን6፥14 የዚህ ቃል የዕብራይስጡ ትርጕም በርግጠኝነት አይታወቅም። ይቀራል፤

ታከማቻለህ፤ ነገር ግን አይጠራቀምልህም፤

የሰበሰብኸውን ለሰይፍ አደርገዋለሁና።

15ትዘራለህ፤ ነገር ግን አታጭድም፤

የወይራ ዘይት ትጨምቃለህ፤ ነገር ግን ዘይቱን አትቀባም፤

ወይንን ትቈርጣለህ፤ ነገር ግን የወይን ጠጅ አትጠጣም።

16የዖምሪን ሥርዐት፣

የአክዓብን ቤት ልምድ ሁሉ የሙጥኝ ብለሃል፤

ትውፊታቸውንም ተከትለሃል።

ስለዚህ አንተን ለውድመት፣

ሕዝብህን ለመዘባበቻ አሳልፌ እሰጣለሁ፤

አሕዛብም ይሣለቁብሃል6፥16 የሰብዓ ሊቃናት ትርጕም ከዚህ ጋር ሲስማማ የዕብራይስጡ ግን የሕዝቤን ስድብ ትሸከማለህ ይላል።።”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 6:1-16

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

1Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;

zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.

2Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;

tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.

Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;

Iye akutsutsa Aisraeli.

3“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?

Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.

4Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto

ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.

Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,

pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.

5Anthu anga, kumbukirani

zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani

ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.

Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,

kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

6Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova

ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?

Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,

ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?

7Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,

kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?

Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?

Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?

8Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.

Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?

Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo

ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

9Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda

ndi nzeru kuopa dzina lanu.

“Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.

10Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala

chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,

ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?

11Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,

ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?

12Anthu ake olemera amachita zachiwawa;

anthu ake ndi abodza

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.

13Choncho, ndayamba kukuwonongani,

kukusakazani chifukwa cha machimo anu.

14Mudzadya, koma simudzakhuta;

mudzakhalabe ndi njala.

Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,

chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.

15Mudzadzala, koma simudzakolola.

Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.

Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.

16Inu mwatsatira malangizo a Omuri

ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,

ndi khalidwe lawo lonse.

Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe

ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;

mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”